Sunday, January 17, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Chisankho chachibwereza chilipo pa 6 June

by Steven Pembamoyo
07/04/2017
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Bungwe loyendetsa zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) lakhazikitsa pa 6 June 2017 kuti Amalawi adzaponye voti yachibwereza kummwera cha kummawa kwa Lilongwe patangotha mwezi bwalo lamilandu la apilo litagamula kuti chisankho cha kuderali sichidayende bwino.

Chigamulochi chidaperekedwa potsatira dandaulo la yemwe ankaimira chipani cha Malawi Congress Party (MCP) Ulemu Msungama kuti chinyengo chidachitika pachisankhocho.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

votting | The Nation Online
Voters will still use voter ID cards in 2019

Chigamulochi chitaperekedwa, zipani zandale zidapempha MEC kuti ichititse chisankho chachibwereza kuderalo msanga kuti anthu akhale ndi phungu wowaimirira ku Nyumba ya Malamulo chifukwa chigamulocho chidatanthauza kuti deralo lilibe phungu.

Pachisankho cha pa 20 May, 204, MEC idalengeza kuti Bentley Namasasu wa Democratic Progressive Party (DPP) ndiye adapambana koma Msungama adakamang’ala ku bwalo la mirandu za chigamulochi.

Wachiwiri kwa mlembi wa chipani cha MCP Eisenhower Mkaka, mneneri wachipani cha Peoples Party (PP) Noah Chimpeni ndi mneneri wa United Democratic Front (UDF) Ken Ndanga adati MEC isapange chidodo pa zopangitsa chisankho chachibwereza.

Mobweretsa chilimbikitso pa nkhawa ya za vuto la ndalama zopangitsira chisankhochi lomwe bungwe la MEC lidanena poyamba, bungweri lati chisankhochi chilipo pa 6 June 2017.

“Potsatila chigamulo cha bwalo la mirandu la apilo, bungwe la MEC lidapangitsa msonkhano pa 4 April omwe lidafotokozera zipani ndi okhudzidwa ena kuti lipangitsa chisankho ku dera la ku mmwera cha ku mmawa kwa Lilongwe pa 6 June 2017,” chidatero chikalata chomwe bungweli lidatulutsa.

Chikalatachi chidatinso pofuna kuti bungweli lisawononge ndalama zambiri, chisankhochi chichitika limodzi ndi zisankho zina monga kumpoto kwa Lilongwe Msozi, chisankho cha khansala wa kumpoto kwa Mayani ku Dedza ndi khansala wa kwa Mtsiliza ku Lilongwe.

Bungwe la MEC lati makandideti akale ndi atsopano ndi olandilidwa kupikisana nawo motsatana ndi malamulo a zisankho.

Pa zisankhozi, bungwe la MEC lati omwe adzaloledwe kuponya voti ndi okhawo omwe adalembetsa m’kaundula wa 2014 ndipo sipadzakhala zosintha malo okaponyera voti.

Zipani za MCP, PP ndi UDF zati nkhaniyi ndi yabwino koma zati mpofunika kuwonetsetsa kuti pasadzachitikenso zachinyengo zomwe zingadzapangitse kuti zotsatira za chisankhochi zidzakanidweso.

Previous Post

Worsening poverty should worry APM

Next Post

‘Malawi can solve food insecurity’

Related Posts

Malango: Covid-19 ikadalipo
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Asiko: Commercial agriculture is one way out of poverty

‘Malawi can solve food insecurity’

Trending Stories

  • covid death | The Nation Online

    Tonse owes ‘ife tonse’ an apology

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Nocma in race against time

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Imbibers defy Covid-19 guidelines

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 mars cabinet review

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Locked with hubby’s brother

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Bottom Up

For 20 Pounds John Chilembwe was betrayed

January 16, 2021
My Diary

Tonse owes ‘ife tonse’ an apology

January 16, 2021
Off the Shelf

Accomplices in genocide

January 16, 2021
Back Bencher

On verge of collapse due to Covid-19

January 16, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

WhatsApp us

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.