Sunday, February 28, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Chithunzithunzi cha gogo wathu

by Tadeyo
11/10/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Mukunyasitsa nkhope mwayambana ndi ndani Munthu wokwiya saoneka bwino

Amakhala ngati mtembvo omwe ukanka kumanda Maliro ake ochita kupha ndi mwala

RelatedHeadlines

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

Iyi ndi nyimbo ya Phungu Joseph Nkasa imene inkaphulika malo aja timakonda pa Wenela tsiku limenelo.

Kuchipululu

Kalekalelo, anasankha wolakwika

Waumphawi, ndi umbuli

Anasankha wolakwika

Koma Gervazzio! Sindidziwa kuti amaganiza chiyani posankha nyimbo.

Posakhalitsa idatulukira basi. Adatulukamo Moya Pete, tsinya lili kuno!

“Mumandinena kwambiri, kuti ndinatenga mbuzi 200 kupita kukaonana ndi Bani Kimwezi wa Nations Unie. Nonsense! Nonsense! Mulibe nzeru nonse, kodi simudziwa ndili nawo ochuluka makobidi? Kafunseni mabanki a ku Switzerland! Izi ndi zangazanga ndalama. N’kati ndikuuzeni, pamwezi ndimalandira K1 400 ndiye mukati ndimayenda kuti ndizidya ndalama zanu. Nonsense!” adatero tisanamupatse moni.

Pomwepo, adayamba kukwapula basiyo mokwiya.

“Nonsense kwambiri. Sindidya pakhomo panu. Ndikapita ndi mbuzi 601 dziko lija la Amerigo Vesipusi mwati ndalakwa? Kodi enatu anabwera masauzande!” adazaza Moya Pete.

Inetu ndimadabwa kuti munthu akangolawa zamchere ndithu amapenga ngati mbuzi! Abiti Patuma amaganizanso chimodzimodzi.

“Akulu, khazikitsani mtima pansi. Sikuti mukamalankhula ndi mkwiyo ndiye kuti mukunena zoona. Ndipo enafe timaona kuti munthu akamakalipa, kutenga aliyense ngati chidzukulu chake, timadziwa kuti pali chimene akubisa. Timakumbukatu za Adona Hilida, Mpando Wamkulu ngakhalenso uyu mwati ndani uyu…. Mfumu Mose,” adatero Abiti Patuma.

Abale anzanga, chiwanda choyenda ndi mapazi ichi.

“Ndakwiya kwambiri. Ndikhozanso kuzisiya kwambiri! Kodi mwaiwala kuti gogo uja naye ankakwera ndege monga enanu muchitira kabaza? Bwanji simunkamutsutsa? Ine ndikangoti ndilaweko kabaza wa ndegeyu mwati mfwemfwemfwe! Nonsense!” adatero Moya Pete, uku akunyamula tambula ya madzi ozizira.

Adamwa. Adanyambitira. Adatafunira ngati m’madzimo mudali nsenga.

Gogo amanenedwa apatu ndi uja adandipeza ndikulima osavala ndili kwathu kwa Kanduku. Inde, gogo yemwe uja adapita uku ndi uko kukanena kuti adandipeza ndili buno bwamuswe!

“Mwaiwalatu china chake akulu. Gogo mukunenayo ulamuliro wake udali wayekhayekha ndipo padalibe omutsutsa. Ifetu tikamakutsutsani timakufunirani zabwino,” adatero Gervazzio.

“Ana osakhwima paliombo. Mwaiwala kale zazikulu zimene ndakuchitirani? Munali yani, anthu oipa mwapanga bwanji?” adafunsa Moya Pete.

Palibe adayankha. Aliyense adafa nalo phwete.

“Tsoka lake, mukakhala kuchipinda kwanuko, kudikira kumwa wamkaka tiyi mumaona ngati zonse zikuyenda. Kodi inuyo a Dizilo Petulo Palibe mudawauza anthu kuti mudzathana ndi zoti tizichita Jump Carefully? Nanga zolipira kundagala mudanenapo? Taipa lero?” adatero Abiti Patuma.

Abale anzanga, palibe icho ndidatolapo.

Anga adali malingaliro a chithunzithunzi cha gogo wankhanza ndi bodza uja! Gwira bango, upita ndi madzi. n

 

Previous Post

Down but not out

Next Post

Sonye, star of all seasons

Related Posts

HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols
Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

February 19, 2021
Next Post
Sonye 4 | The Nation Online

Sonye, star of all seasons

Opinions and Columns

My Diary

Light that came with Covid-19

February 27, 2021
Guest Spot

Resurgence of albino killings deplorable

February 27, 2021
Back Bencher

Is violence a boomerang effect in DPP?

February 27, 2021
Off the Shelf

Sacrificial lambs of a dysfunctional system

February 27, 2021

Trending Stories

  • Court has declared Escom a private firm

    Court declares Escom private company

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K1.7bn Chisale assets seized

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • What the hell is APM doing with BJ?

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • HRDC alleges threats, intimidation from investor

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.