Tuesday, March 2, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Chotsani ndale mu ulimi wamthirira—Jalavikuba

by Martha Chirambo
01/10/2015
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Inkosi Jalavikuba ya m’boma la Mzimba yapempha boma kuika alimi patsogolo ndi kuchotsa ndale muulimi wamthirira.

Mfumuyi idanena izi Loweruka lapitali m’dera la kumpoto m’boma la Mzimba pachionetsero cha ulimi wamthirira pomwenso idawapepesa alimiwa ati chifukwa salabadiridwa.irrigation-farming

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Jalavikuba adati chifukwa boma lalowetsapo ndale paulimi wamthirira, ulimiwu sukupita patsogolo. Ndale, iye adati, zikulowa pa momwe kontilakiti zomangira masikimu a mthirira zikuperekedwera.

“Ndale zatisaukitsa, atsogoleri andale, amipingo ndi ife mafumu tiyeni tisiye ndale ndi kuchita chitukuko. Atolankhani mukanene chilungamo, ine si wandale,” adatero Jalavikuba.

Iye adati ndi zomvetsa chisoni kuti ngakhale dziko lino limadalira ulimi pachuma chake, boma silikuikapo mtima kwambiri.

“Alimi paokha akuyesetsa, mbali yatsala ndi ya boma kuti liziwapatsa thandizo loyenera,” iye adatero.

Jalavikuba adakumbutsanso alimiwo kuti ulimi ndi bizinesi ndipo aziikirapo khama.

Koma alimiwo adadandaula kuti ulimi wamthirirawu akuumva kuwawa kaamba ka ngalande  zomwe sizikugwiritsidwa ntchito chimangireni.

Iwo adati yemwe adamanga ngalandezo adamanga mwachinyengo moti zina zidagumuka chifukwa chochepa simenti, pamene zina sizitha kuthirira minda chifukwa zili mmunsi kwambiri.

Mmodzi mwa alimiwo, Austin Chavula, yemwe ndi wapampando wa sikimu ya Ndau, adati boma likufunika liunikenso momwe ntchitoyo adayigwirira.

Povomerezana ndi Chavula, Edward Mvula, wapampando wa sikimu ya Chanolo, adati alimiwa akusowa pogwira ngakhale boma lidaononga ndalama zankhaninkhani pokumbitsa ngalande m’chaka cha 2011.

“Pakadalipano tikupempha boma litiganizire potipatsa simenti yokonzeranso ngalandezi kuti mthirira uyende bwino,” Chavula adatero.

Ndipo wachiwiri kwa wapampando wa komiti ya Nyumba ya Malamulo pazaulimi, Joseph Chidanti Malunga, adati komiti yake ipereka madandaulowo kuboma ndipo akukhulupirira kuti lichita kafukufuku pankhaniyi.

Malunga, yemwenso ndi phungu wa Nyumba ya Malamulo m’dera la kummwera cha kumadzulo m’boma la Nsanje, adati n’zodabwitsa kuti dziko lino likuitanitsa chakudya kunja pamene lili ndi kuthekera kodzilimira.

“Ngati boma lingaike mtima powapatsa anthu zipangizo zowayenereza paulimi, sindikuona chifukwa chogulira chimanga kumaiko ena,” Malunga adatero.

Iye adati chofunika ndi kudzikonzekeretsa poika ndondomeko zogwirizana ndi momwe zinthu zikuyendera.

Ndipo Agnes Nyalonje, phungu wa derali yemwe adakonza chionetserocho, adati dera lake lili ndi kuthekera kodyetsa gawo lalikulu la dziko lino.

Dera la kumpoto m’boma la Mzimba, monga madera ambiri m’dziko muno, lidakhudzika ndi ng’amba ndipo anthuwa apulumukira ulimi wamthirira.n

 

Previous Post

School dragged to court over land

Next Post

Derby On

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Next Post
The two giants captured during the previous encounter

Derby On

Opinions and Columns

My Turn

Tackling global slowdowns

March 1, 2021
People’s Tribunal

Burglary at the hill

February 28, 2021
Search Within

Perseverance landed, is alive and well

February 28, 2021
Emily Mkamanga

Tasting your own salt in politics

February 28, 2021

Trending Stories

  • Olela: We are excited

    K5bn Sunbird Waterfront hotel opens May

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • We won’t give Up—Chakwera

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Court declares Escom private company

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.