Wednesday, May 18, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Covid-19 ikufala ngati moto

by Steven Pembamoyo
18/12/2021
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Komiti yoongolera zolimbana ndi mliri wa Covid-19 m’dziko muno yachenjeza kuti kachirombo koyambitsa matendawa kakufala ngati moto wolusa zomwe zachititsa kuti komitiyo ikhazikitse malamulo ena omwe ayambe kugwira ntchito Lolemba.

Nduna ya zaumoyo a Khumbize Kandodo Chiponda, omwe ndi mmodzi mwa apampando a komitiyo adalengeza malamulo atsopanowo Lachinayi pamsonkhano wa atolankhani ku Lilongwe.

Anthu pamzere kufuna kubayitsa katemera wa Covid-19

Iwo adalengezanso kuti Lachitatu lokha anthu 318 adapezeka ndi kachirombo ka corona, pomwe Lachiwiri adapezeka anthu 235 kufikitsa anthu onse omwe ali ndi kachiromboka pa 1 391 kuchoka pa anthu atatu m’mbuyomo pomwe boma linkakhwefulako malamulo opewera matenda.

A Chiponda amalengeza zomwe komiti yawo idagwirizana itakumana Lachitatu pomwe adapeza kuti dziko la Malawi lachoka pamzere woyamba ndipo lafika pamzere wachiwiri.

“Kuti mumvetsetse, tikamanena za mizere tikunena za kukula kwa vuto m’dziko. Mzere woyamba ndiye kuti zinthu ziliko bwino pomwe mzere wachisanu ndiye kuti zafika pa kayakaya, ndiye ife tafika pamzere wachiwiri tsopano,” adatero a Chiponda.

Izi zikutsimikiza zomwe madotolo ndi akadaulo pa zaumoyo adanena Lolemba pamsonkhano wa atolankhani kuti matendawa avuta kwambiri nyengo ya zisangalaloyi chifukwa anthu ambiri adanyozera kubayitsa katemera.

Pulezidenti wa madotolo m’dziko muno a Victor Mithi adati padakalipano m’zipatala maka malo osamalirako odwala Covid-19 kukudutsa mphepo koma akuyembekezera ntchito yobetsa nayo tulo zisangalalo zikafika.

“Panopa zikuoneka zopepuka koma tikamayandikira Khrisimasi mpaka mwezi wa January kukhala ntchito moti ogwira ntchito zachipatala adzakhala opanikizika, kusowa popumira,” adatero a Mithi.

Pomwe mkulu woona za umoyo m’madera a Ben Chilima adati matendawa afala kwambiri nyengo ya zisangalalo chifukwa chazochitika nthawiyi komanso polingalira kuti anthu ambiri sadabayitse katemera.

“Taonera m’maiko aanzathu komwe corona yatsopano yotchedwa Omicron yavuta, anthu ambiri omwe akumavutika zedi mwina kufa kumene ikawagwira ndi omwe sadalandire katemera ndiye kuno kwathu zikuoneka kuti ambiri sadabayitse,” adatero a Chilima.

Malingana ndi a Chiponda, katemera wokwana 1 587 487 ndiye adaperekedwa kwa anthu mmalo mwa anthu 11 miliyoni omwe boma lidakonza zoti libaye.

A Chiponda adati katemerayo akadalipo wambiri koma anthu akadakhulupilirabe zabodza zokhudza katemera wa corona yemwe munthu akabayitsa amatetezeka kuti asadwale mwa kayakaya akagwidwa ndi mliriwo.

Ngakhale talowa m’nyengo yazisangalalo, malamulo atsopano omwe ayambe kugwira ntchito Lolemba akuti malo omwera mowa azitsekedwa 10 koloko usiku komanso ngati anthu akukumana m’nyumba, asapitirire anthu 10.

Izi zikutanthauza kuti anthu omwe amakhulupirira kumwa zoledzeretsa ndi kuchezera akati akondwa ufulu wawo walandira malire.

Malamulo ena akuti mkumano wa mkati ngati kutchalitchi, kumpira, kumsonkhano ndi ku zoimbaimba anthu asamapose 100 koma pabwalo asamapose 250 komanso galimoto yonyamula anthu 10 kuyambira Lolemba izinyamula anthu 6 basi.

Kuyambira pachiyambi cha Covid-19 mu 2019, anthu 62 933 ndiwo adadwalako, anthu 59 000 adachira, anthu 2 310 adamwalira nayo ndipo anthu 1 391 ndiwo akudwala panopa.

Previous Post

Zisangalalo zafika, samalani

Next Post

Batatawala bail ruling Monday

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post
Arrested: Abdul Karim Batatawala

Batatawala bail ruling Monday

Opinions and Columns

Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022
My Thought

Two years of nothing but development rallies

May 15, 2022

Trending Stories

  • A fleet of UTM vehicles: The movement says it is funded by well-wishers

    UTM party vehicle issue goes to MRA

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • What bloody chieftaincy!

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • PAC clears Macra director general, cautions board

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Firm discovers copper deposits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Investment pledges jump to K666 billion

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.