Monday, April 12, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Covid-19 yakolera

by Steven Pembamoyo
30/05/2020
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Chiwerengero cha Amalawi amene apezeka ndi kachirombo ka coronavirus chatumphuka m’sabata ikuthayi kuchoka pa 101 kufika pa 203.

Izi zachitika pamene komiti yoona za matenda a Covid-19 Lachinayi idalengeza kuti adapeza anthu 102 amene adachokera ku Zimbabwe ndi South Africa adapezeka ndi matendawa.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

Covid Stadium | The Nation Online
Ena mwa omwe adafika ku Kamuzu Stadium

Amalawi 441 amene adafika m’dziko muno kuchoka m’dziko la South Africa, m’sabatayi adathawa kumalo amene amawasunga ku Kamuzu Stadium mumzinda wa Blantyre. Ndipo dzikoli limyembekeza kulandiranso anthu ena pafupifupi 300 kuchokera ku South Africa dzulo.

Msonkhano wapadera wa komiti ya Covid-19 omwe udali ku Bingu International Convention Centre mumzinda wa Lilongwe Lachinayi, udakambirana mwakuya nkhani zina ndi zina za matendawa koma adagwirizana kuti kuthawa kwa anthu ku Kamuzu Stadium kudachitika kaamba ka kunyozera.

Chiwerengero chambiri cha anthu omwe adapezeka ndi coronavirus m’dziko muno mwezi umodzi wapitawu amakhala anthu omwe adangofika kumene kuchoka m’mayiko okhudzidwa kwambiri ngati Tanzania ndi South Africa.

Koma unduna wa zaumoyo wati kubwera kwa abalewa kusabweretse nkhawa iliyonse chifukwa boma lapanga kale zoyenera kuti anthuwo apimidwe n’kutsimikizika kuti ali bwino asadabwerere m’nyumba zawo.

Mneneri waundunawu Joshua Malango wati ngakhale boma likupanga zotheka kuti kubwera kwa anthuwo kusasokoneze nkhondo yolimbana ndi coronavirus, anthu nawo ali ndi udindo waukulu.

“Takhala tikunena kuti asilikali amphamvu pa nkhondoyi ndi anthu eni ake. Anthu akuyenera kutsatira zomwe amauzidwa kupanga kuti apewe matendawo basi,” adatero Malango.

Mmodzi mwa anthu obwererawo amene sanafune kutchulidwa wadandaula kuti boma silikuonetsa chidwi pa anthuwo chifukwa likuwasunga pamtetete kubwalo la masewero la Kamuzu Stadium ku Blantyre.

“Chifikireni tikungokhala kuno akuti tidikire zotsatira za zomwe adatiyeza ngati tabwera n’kachilomboko kapena ayi koma tikukhala pamtetete,” adatero odandaulayo.

Apo n’kuti anthuwo asanathawe.

Polankhula kwa atolankhani Lachinayi, wapampando wa komiti yapadera ya Covid-19 Dr John Phuka adati kuthawa kwa anthuwo, komwe kudachitika anthu enanso atathawa malo osungirako anthu kwa Kameza mumzinda wa Blantyre, ndi phunziro.

“Takhazikitsa komiti yapadera imene iziunikira momwe anthu ofika kuchoka kunja tikuwalandirira ndi cholinga choti mavuto awa asaonekenso. Ndipepese kwa onse ochoka kunja amene akuoneka kuti anatopa ndi ulendo wochoka ku Joni komanso zochitika,” adatero Phuka.

Koma Malango wati boma lakonza kale malo omwe anthuwo akasungidweko ndipo likhala likulengeza za malo oterowo komanso kusamutsa anthuwo kupita nawo m’malowo.

“Boma likamapanga zinthu limakhala litakonza kale mapulani. Zonsezo zili kale m’mapulani aboma,” adatero Malango.

Woyendetsa ntchito za zaumoyo Dr Charles Mwansambo adati bwalo la Kamuzu Stadium lidasankhidwa ngati pofikira chabe potsata mpata woti anthuwo asathinane malo amodzi mpaka atatengedwera kumalo okhazikika.

Dziko la Malawi lidazemba mbindikiro wa m’nyumba wa masiku 21 kuyambira pa 18 April 2020 mpaka pa 9 May 2020 gulu la zaufulu wa anthu la HRDC litakatenga chiletso polingalira kuti anthu ambiri adalibe chakudya cha panthawi yonse ya mbindikirowo.

M’maiko ena omwe m’bindikirowo udatheka, boma limathandiza anthu ake ndi chakudya komanso ndalama zogulira zinthu zogwiritsa ntchito pa m’bindikirowo.

Avatar
Steven Pembamoyo
Previous Post

Clubs get K840m from K2.3bn gate revenue

Next Post

Zipani zakonzeka kusankha makomishona

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
Adalembera zipani: Mutharika

Zipani zakonzeka kusankha makomishona

Opinions and Columns

Political Uncensored

Managing the dream

April 11, 2021
My Thought

Malawi needs fixing, not politicking

April 11, 2021
People’s Tribunal

Don’t intimidate Nyasaland Union of Teachers

April 11, 2021
Emily Mkamanga

Longevity in power no solution

April 11, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Malawi Airlines is yet to post a profit since it took to the skies

    Malawi Airlines faces liquidation

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MHC houses risk demolition

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Shareholders, Airtel tussle in court

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MLS wants APM, Muhara property seized

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Industrial disputes choke IRC

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.