Wednesday, June 29, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Esiteti, anthu ayanjana pa za malo

by Nation Online
03/07/2021
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Esiteti ya Lujeri yalola anthu pafupifupi 5 000 amene adalowerera malo a esitetiyo ku Mulanje kuyambira zaka za m’ma 2000 kukhala pamalowo popanda zovuta zilizonse.

Mkulu wa bungwe la Centre for Democracy and Economic Development Initiative (Cdedi) Silvester Namiwa wati wakondwa chifukwa esitetiyo yalola kulekera anthuwo malowo, pomwe bungwelo likupitiriza kumenya nkhondo kuti anthu a ku Thyolo ndi Mulanje apezenso malo amene atsamunda adawalanda.

Namiwa: Anthu akupambana nkhondo

“Takondwa kuti a Lujeri alola kumvana ndi anthuwo. Apa zikusonyeza kuti pang’onopang’ono nkhondoyi anthu apambana,” adatero a Namiwa.

Malinga ndi amene amaimira anthuwo pamlandu umene udali kubwalo lalikulu, a Charles Kusiwa adati chimkulirano pakati pa anthuwo ndi esitetiyo udadza pomwe anthuwo adalowerera kumpoto ndi kummawa kwa esitetiyo. Esitetiyo siyimafuna kupereka malowo kwa anthu pomwe anthuwo nawo samafuna kuchoka.

“Pa 23 December chaka chatha, esitetiyo idapita kukhoti n’kukasumira agulupu a Gladstone, T/A Njema ndi 10 ena, kuwadzudzula kuti alowerera malo a esiteti,” adatero a Kusiwa.

Woweruza kubwalo la milandu lalikulu Mike Tembo ndiye adakhala pakati pa esitetiyo ndi anthuwo ndipo adanenetsa kufunika kwa chiyanjano pakati pa eni esiteti komanso anthu a m’deralo. Zokambirana zidatenga maola asanu kufika adagwirizana kuti esitetiyo isathothe anthuwo.

“Woweruza adanenetsa kuti anthu adalowerera kale malowo ndipo adamanga kale pokhala ndipo adabzala mbewu ya tiyi choncho kuwathotha kukadangobweretsa mavuto ena,” adatero a Kusiwa.

Nkhani ya malo imavuta kwambiri m’maboma a Mulanje ndi Thyolo kumene alo ambiri ali m’manja mwa maesiteti a tiyi ndi khofi. Mmbuyomu a Vincent Wandale aali kumenyera kuti mabomawo akhala dziko palokha kuti nkhaniyi athane nayo.

Previous Post

Alinafe Banda-Malisawa: First female president for the MIPS

Next Post

Capital City derby postponed

Related Posts

Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Katundu wa a Mtambo adali kuseri kwa ofesi za khonsolo
Nkhani

Agona ku maofesi a khonsolo ya Mzuzu

June 4, 2022
Nkhani

Woimba abedwa mumzinda wa mzuzu

May 28, 2022
Next Post

Capital City derby postponed

Opinions and Columns

My Turn

US court threatens women’s rights

June 29, 2022
People’s Tribunal

Two years later and we are still singing same song

June 26, 2022
Big Man Wamkulu

Wife’s relatives have taken over my house

June 26, 2022
My Thought

Stop cyber harassment

June 26, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • ACB cleared Sattar contract—Documents

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Britain squeezes Zuneth Sattar

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MET says cold, wet weather will continue

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mwanamvekha wants his case dismissed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K243bn Malawi trade deal on rocks

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.