Saturday, February 27, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

‘Fodya n’kunazale’

by Dailes Banda
01/10/2015
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Pamene alimi a fodya ali yakaliyakali kukonzekera ulimi wa 2015/16, mlangizi wa zaulimi wa fodya m’boma la Rumphi, Charles Jere, walangiza alimi kuti atsatire ndondomeko ndi malangizo oyenera popanga nazale ya fodya pofuna kupindula ndi ulimi wawo.

Pocheza ndi Uchikumbe posachedwapa, Jere adati nazale ya fodya si ili ngati ya ndiwo zamasamba kaamba koti imafuna chisamaliro chapadera chifukwa kupanda kutero palibe chimene mlimi wa fodya angapindule ndi fodya n’chifukwa chake pali mawu akuti “fodya n’kunazale”.Fodya_Tobacco_nursary

RelatedHeadlines

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

“Choyamba mlimi akuyenera kupeza malo omwe aikepo nazale yake. Malowa akuyenera kukhala kufupi ndi madzi oyenda kapena omwe akuoneka opanda tizilombo toyambitsa matenda a mtundu wina ulionse,” adatero Jere.

Jere adati mlimi akuyenera kutipula nazale kutengera ndi kukula kwa munda wake. Mlangiziyu adati paekala imodzi bedi la nazale likuyenera kukhala lotalika mamita 30 ndi mita imodzi mlifupi pomwe hekitala imafunika mabedi atatu a muyezo woterewu.

“Akapanga bedi lija mlimi akuyenera kutenga mapesi a chimanga n’kuwasanja pabedi lija ndipo akatero awaotche ndi cholinga chofuna kupha tizilombo tomwe tidali mudothi tomwe tikadatha kuononga fodya panazalepo.

“Apa adikire masiku awiri kapena atatu kuti ayambe kufesa fodya panazalepo,” adafotokoza Jere.

Iye adati mlimi ayenera kuthira feteleza wokwana makilogalamu atatu asadafese fodya uja. Akafesa fodyayo athire mankhwala kuti aphe tizilombo monga nyerere zomwe zikhoza kudya mbewuyo.

“Mankhwala ena ofunika kuthira panazale ndi amene amapha tizilombo toyambitsa matenda ena mufodya,” adatero Jere.

Malinga ndi Jere, mankhwalawa amafunika kusungunula mutheka la madzi a mukheni ndi kuwathira panazale paja pataikidwa kale maudzu.

Akatero mlimi akuyenera kuthirira nazale ija kamodzi patsiku, koma fodya uja akayamba kumera pamafunika kuthirira kawiri patsiku ndipo kuchuluka kwa madzi kuziyenderana ndi kusunga madzi kwa dothi. n

Previous Post

FMB increases cricket sponsorship

Next Post

Yona sets hype for derby by ‘betting’ car

Related Posts

HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols
Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

February 19, 2021
Next Post
Malunga: I only knew about it at the stadium

Yona sets hype for derby by ‘betting’ car

Opinions and Columns

My Diary

Light that came with Covid-19

February 27, 2021
Guest Spot

Resurgence of albino killings deplorable

February 27, 2021
Back Bencher

Is violence a boomerang effect in DPP?

February 27, 2021
Off the Shelf

Sacrificial lambs of a dysfunctional system

February 27, 2021

Trending Stories

  • Chiyembekeza (L) and Kusamba Dzonzi during the briefing

    Admarc secures K430bn to revamp operations

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Censorship Board acts on ‘Aunt Nellie’ videos

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Grace Chinga makes posthumous return

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Mlusu in tight spot on budget

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Dodma wants Covid-19 funds back from councils

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.