Monday, January 25, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Gulewamkulu ndi mankhwala

by Bobby Kabango
17/09/2016
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Matenda akagwa pakhomo, makolo amakhala ndi njira zochuluka zothetsera matendawo malinga ndi zikhulupiriro zawo. Ena okhulupirira gulewamkulu akuti ngati m’thupi mwabaya, akangovina wodwala amachira pomwepo. M’mudzi mwa Siledi kwa Senior Chief Kanduku m’boma la Mwanza muli mayi wina amene ati adachira gulewamkulu atapalasa. BOBBY KABANGO akucheza ndi mkulu wa dambwe kumeneko, Maxwell Kondwerani.

Gulewamkulu akuti ndi mankhwala
Gulewamkulu akuti ndi mankhwala

Tidziwane maudindo wawa…

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Ndili ndi maudindo angapo, ndine nduna ya mfumu m’dera lino. Ndimamemeza anthu am’mudzi muno ngati pali zina kuti zichitike kapena mfumu yaitana. Ngati anthu am’mudzi muno ali ndi zochita zina monga mwa zikhulupiriro zawo amandifikira kuti ndipereke uthenga kwa mfumu yathu yomwe imaloleza zochitikazo komanso kudambwe ndili ndi gawo langa.

Tikambe nkhani ya gulewamkulu…

Mufuna ndikambe nkhani iti kumeneku? Pajatu zakudabwe saulula, mumadziwa zimenezo?

Inde koma, n’zabwinobwino, osati zofwala gule.

Chabwino, nkhani yake ndi yotani yomwe mufuna ticheze?

Tikumva kuti guleyu ndi mankhwala, ndi zoona?

Ndi zoona. Ife Achewa timakhulupirira zimenezi. Izi kuno zimachitika ngati mizimu yalamula kuti tichite.

Zimakhala bwanji kuti mpaka zifike poitana gule?

Timakhala talamulidwa ndi mizimu kuti gulewamkulu avine ndi cholinga chochotsa matendawa. Izi sizitheka popanda kulamulidwa ndi mizimu.

Talongosolani chiyambi chake chimakhala chotani kuti mizimu ilamule?

Munthu ngati akudwala, timayenda naye mwa asing’anga momwe timakaombeza za chiyambi cha matendawo. Kumeneko n’komwe amanena ngati matendawo akufunika kuvinira gule kapena angomwa mankhwala. Apa ndikutanthauza kuti sizingatheke kuti mungoyamba kuvinira matenda ngati mizimu sidanene.

Akati gule akavine zimakhala bwanji?

Amanena kuti mukatenge chikho cha msunje ndipo tikaikemo ufa ndi kukanda. Apa mumayamba kumuzungulitsa chikho chija. Pomwe mukuzunguliza chikho chija mumaimba nyimbo. Tikatha amati tikataye patsinde pa mtengo. Pomwe tikuchita izi ng’oma zimakhala zikusweka komanso zilombo zikuvina.

Taimbani nyimboyo ndimve…

Timati….Tidzutsire wathuyu bwino, ngati ndi mizimu wathuyu adzuke. Mizimu mudzutse wathu pofika mawa…

Kodi matendawa amakhala atafika pothiphwa kwambiri?

Eee! Matenda amakhala afika povuta ndipo tikamati tidzutsire wathuyu ndiye kuti amakhala salinso mwakanthu.

Akamati mukavine gulewamkuluyo amakupatsani mankhwala alionse?

Palibe mankhwala alionse omwe amatipatsa ndipo machiritso amagona pamenepo. Mukavina ndi kutsata zomwe akunenazo matenda amathera pomwepo.

Ndani amayenera kupezeka pamwambo ngati umenewo?

Akuluakulu a gule amapezeka pamalopo komanso mwini mbumbayo. Pomwe tikusankha mwini mbumba timayenera kusankha yemwe adalowa gule wamkulu osangotenga aliyense.

Kodi zimatheka kuti gule avine chikhalirecho sindiwe wolowa?

Sizingatheke. Kuno zimachitika chifukwa aliyense adameta kapena kuti kugula njira.

Kodi munthu amachira?

Kwambiri ndipo chitsanzo chabwino ndi matenda omwe tidali nawo miyezi yapitayi. Mayi ameneyo adalumidwapo ndi njoka kawiri, titapita naye kokaombeza adatiuza kuti tikufunika tikamuvinire gulewamkulu. Tidapempha mfumu kuti timuvinire. Tidachita izi ndipo adachira tsiku lomwelo. n

Previous Post

Msonda: Tsamba loyoyoka mu PP?

Next Post

League leaders Eagles, 2nd-placed Silver face-off

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Eagles players celebrating a previous win

League leaders Eagles, 2nd-placed Silver face-off

Trending Stories

  • covid 2 | The Nation Online

    SA returnees in forced quarantine

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • court rebuffs apm on frozen account

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Citizens power brings change

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • AG disowns K750m compensation signature

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Emily Mkamanga

Citizens power brings change

January 24, 2021
Search Within

The rural farmer needs to take centre stage

January 24, 2021
My Thought

Spread hope not fear

January 24, 2021
Big Man Wamkulu

Hot babe wants to trap me, should I ran?

January 24, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.