Thursday, May 26, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Jombo ikudiliza matimu

by Bobby Kabango
24/08/2013
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Chalaka bakha nkhuku singatole. Linda madzi apite ndiye udziti wadala. Miyambiyi ndiyo idatsanuka m’sabatayi kaamba ka jombo yomwe idathudzula Nyerere komanso kudiriza Maule mwachipongwe.

Oyambirira kudandaula ndi jombo adali neba winayu ku Zomba kumene amati zikamuyendera. Iye adanyang’wa kuti adadya kale mkango wa umuna ndipo udatsala ndi waukazi koma awo adali maloto amasana chifukwa pakutha pa mphindi 90 kumva kuti maliro a neba ayikidwa ku Thodwe koma nkhope anthu amakaonera ku Chinamwali.

Neba winayu timati mwina zimuyendera atangothyola banki ya ku Lilongwe koma kupita pa Dedza kumvanso kuti matenda akula ndipo amugoneka pachipatala cha Dedza.

Zikatere chikho chimasiya kukoma chifukwa maso ndi zokamba za anthu zimakhala pa matimu awiriwa. Koma mmene jombo ikufikira zikukayikitsa ngati matimu enawa azifika pena ndi mipikisano yathu.

Bwanji jomboyi izisewera payokha kapena izikumana ndi anyamata oyenda ndi unyolo?

Tikuganiza kuti manebawa adakakhala ndi owathandiza bwezi akupirira ndi jombo. Koma bambo awo angomwalira dzulodzuloli ndiye sitingayembekezere kuti angalimbe pa jombo.

Mwinatu asilikaliwa thandizo la boma lomwe amapeza ndilo likuwachititsa kuti azisangalala poponda anzawo. Timaganiza kuti ku Lilongwe aneba athu kumeneko ayimitsana ndi jombo polingalira kuti iwo ndi eni ndalama koma madzi enieni.

Ayi ife tipepese anebawa pa ngozi yachitika. Tamva kuti maso anu muponyeza pa Standard Bank ndi ligi komabe ndi momwe jomboyi ikufikira ife tilibe chikhulupiriro.

Previous Post

Malawi cost of living up on maize account

Next Post

Of patriotism and Escom

Related Posts

Nkhani

Agwidwa ndi yunifomu za polisi

May 22, 2022
Nkhani

Dollar yasowa

May 21, 2022
Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
Next Post

Of patriotism and Escom

Opinions and Columns

Business Unpacked

Tame egos, take risks to grow economy

May 26, 2022
People’s Tribunal

What was that press briefing all about?

May 22, 2022
Big Man Wamkulu

Wife, in-law plotting my downfall

May 22, 2022
My Thought

Tonse Alliance died on arrival

May 22, 2022

Trending Stories

  • Mutharika on the campaign trail in 2019

    APM under pressure

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Musician Martse in hospital after fire accident

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Kalindo earmarked for diplomatic post

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Nyasa Mobile Limited partners Vodafone

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Blantyre-based artists see off Martse

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.