Thursday, January 21, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Kalembera wafika kummwera

by Steven Pembamoyo
17/08/2018
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kalembera wa mkaundula wachisankho cha chaka cha mawa wafika m’chigawo cha kummwera tsopano ntchitoyi itakumana ndi zokhoma zosiyanasiyana m’maboma a mchigawo chapakati pomwe idayambirira.

Boma la Ntcheu ndi boma lomaliza la mchigawo chapakati komwe kwafika kalemberayu mgawo lachinayi ndipo mgawo lomweli muli maboma a mchigawo cha kummwera monga a Blantyre, Mwanza ndi Chikwawa.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Voters registration | The Nation Online
Ntchito ya kalembera

Kalemberayo adayamba Lachinayi ndipo adzatha pa 29 August.

Malingana ndi mkulu woyang’anira zisankho ku Malawi Electoral Commission (MEC), Sam Alfandika, pali chiyembekezo choti pamene ntchitoyi ikupitirira, mavuto omwe amaoneka m’magawo atatu oyambirira achepa kwambiri chifukwa anthu aphunzira mokwanira za kalemberayu.

“Kumayambiriro kuja tidali ndi vuto loti anthu ambiri adali asadadziwitsitse za kalemberayu koma pano ndi mauthenga omwe akhala akuperekedwa, anthu ambiri akudziwa ndipo chiyembekezo n’chachikulu kuti ziyenda bwino,” adatero Alfandika.

Iye adapempha kuti zipani zitengepo mbali yaikulu yomema anthu kuti akalembetse chifukwa anthu omwewo ndiwo mavoti awo.

Mkulu wa bungwe lophunzitsa anthu la National Initiative for Civic Education (Nice) Trust, Ollen Mwalubunju wati bungwelo lipitiriza kuphunzitsa anthu m’madera momwe mukulowera kalemberayu kuti cholinga chenicheni cha demokalase chidzawoneke pachisankho cha chaka chamawa.

“Zimakhala zofoola nkhongono kuona kuti anthu ochepa ndiwo avota kusankha atsogoleri chifukwa zimakhala ngati ena aja angokakamizidwa kutsogoleredwa ndi anthu omwe sadawafune, ndiye tikufuna ulendo uno, aliyense yemwe ndi woyenera kuvota akavote. Chiyambi cha zonse ndi kulembetsa,” adatero Mwalubunju.

Iye adati ndi wokondwa ndi momwe kalembera adayendera m’gawo lachitatu lomwe limachitika ku Lilongwe ndipo adati izi zidatheka chifukwa bungwelo ndi mabungwe ena komanso mipingo ndi zipani adagwirana manja kumema anthu.

Poyamba kalemberayu m’maboma a Kasungu, Salima ndi Dedza, padali mavuto aakulu okhudza kufaifa kwa zipangizo mpakana anthu ambiri sadalembetse. Mavutowa adapitirira mgawo lachiwiri ku Mchinji, Dowa, Ntchisi ndi Nkhotakota moti chipani cha Malawi Congress (MCP) ndi mabungwe ena monga la Centre for Human Rights and Rehabilitation (CHRR) adapempha MEC kuti idzabwereze kalembera mmabomawa.

Mavutowa adadzachepa m’gawo lachitatu lidatha sabata yatha koma padapezeka mavuto ena monga anthu kulandidwa ziphaso komanso miyambo yamakolo yomwe imabwezera kalembera mmbuyo.

Previous Post

Kuli ziii! za mapulaimale

Next Post

Hellen Chabunya — Chigoneka Ward aspiring councillor

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Hellen Chabunya | The Nation Online

Hellen Chabunya — Chigoneka Ward aspiring councillor

Trending Stories

  • Not yet given retirement benefits: Mutharika

    Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 initiative raises K18.3m in 2 days

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi closes in on hefty us deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Fake injury claims soar

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Fired Vale staff claim K4.6bn compensation

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Business Unpacked

Towards Malawi2063, lessons from Vision 2020

January 20, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 20, 2021
In pursuit of development

India’s vaccine drive

January 20, 2021
My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.