Monday, March 1, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Kudali Ku Karonga

by Dailes Banda
13/09/2015
in Chichewa
1 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 

Pamene ena amati chikondi sichiona chikhalidwe kapena mtundu wa khungu la munthu, banja la Manaseh Chisiza, mkulu wa bungwe la azisudzo ndi mkazi wake Andrea Beyerlein likuchitira umboni mawuwa.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

Amwalira atathawa m’chipatala

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Manaseh, mkulu wa National Theatre Association of Malawi, adakumana ndi njole yake ku Karonga komwe Andrea adabwera ndi makolo ake kuyendera ntchito zachifundo zomwe iwo adali kugwira mogwirizana ndi bungwe lina la ku Mzuzu.

Manaseh ndi Andrea tsiku la ukwati wawo
Manaseh ndi Andrea tsiku la ukwati wawo

“Atabwera nthawiyo adapezeka kuti adafikanso ku Lusubilo Orphan Care Project komwe ndidamuona koyamba,” adatero Manaseh, yemwenso ndi mkulu wa gulu la zoimb la Lusubilo Band.

Awiriwa adapatsana nambala za telefoni ndipo ankachezerana kufikira pomwe adakumananso ku Germany chaka chathachi.

Kukumana kwawo ali ku Germany kudali chiyambi cha chikondi chomwe chidakula ndipo chikukulirakulirabe mpaka adamanga woyera mwezi watha ku Germany komweko.

Manaseh adati Andrea yemwe ndi woimba komanso wochita mafilimu amalemekeza chikhalidwe chake Chimalawi ndipo banja lawo limaganizira zikhalidwe zonse za Chizungu komanso chikhalidwe cha Chimalawi.

“Andrea amakonda kukonza m’nyumba pomwe ine ndimakonda kuphika osati chifukwa cha chikhalidwe cha kwawo koma chifukwa ndimakonda kuphika basi kuyambira kalekale ndipo ndimaphika bwino kwambiri,” adatero Manaseh.

Manaseh ndi wochokera m’mudzi mwa Khwawa T/A Mwasambo m’boma la Karonga ndipo adabadwa m’banja la ana 8 momwe ndi wachisanu ndi chimodzi kubadwa. Andrea adabadwa yekha m’banja la kwawo.

Previous Post

The father and his daughters

Next Post

Mlandu wa Savala ukupendekeka

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
death e1465557792659 | The Nation Online
Chichewa

Amwalira atathawa m’chipatala

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Next Post
Savala (L) with a well-wisher at the court yesterday

Mlandu wa Savala ukupendekeka

Opinions and Columns

People’s Tribunal

Burglary at the hill

February 28, 2021
Search Within

Perseverance landed, is alive and well

February 28, 2021
Emily Mkamanga

Tasting your own salt in politics

February 28, 2021
People’s Tribunal

When blood of citizens is on head of leaders

February 28, 2021

Trending Stories

  • chisale1 | The Nation Online

    Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Grace Chinga makes posthumous return

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Admarc secures K430bn to revamp operations

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MIN coy on K18bn MZ youth centre

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • TUM insists strike continues

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.