Sunday, January 24, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Kulandira mwana ndi ‘nkanulo’

by Steven Pembamoyo
13/08/2016
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Zikhulupiriro zina ukamva, mutu wake weniweni sowe. Pali zambiri zomwe makolo amakhulupilira paumoyo wa munthu kuyambira kubadwa mpaka kumwalira. Anthu ena akuti amakhulupirira kuti mwana akabadwa, pamafunika mwambo wa ‘nkanulo’ ati kusonyeza kuti mwanayo walandiridwadi pakati pa abale. STEVEN PEMBAMOYO adacheza ndi mayi Miriam Chongwe a kwa mfumu yaikulu (T/A) Maganga m’boma la Salima yemwe akufotokoza zambiri za mwambowu.

Mayi Chongwe (kumanja) kulongosola za mwambo wa nkanulo
Mayi Chongwe (kumanja) kulongosola za mwambo wa nkanulo

Mayi, ndati ndicheze nanu pa mwambo wa ‘nkanulo’. Mwambowu ndi wotani?

RelatedHeadlines

Amapita kukagula zomwera tiyi

Anatchezera

Odzipha akuchuluka

Uwu ndi mwambo womwe umatsatidwa mwana akabadwa kusonyeza kuti abale ndi anthu pamudzipo amulandira ndipo ndi mmodzi wa iwo. Izi zimatanthauza kuti ndi mfulu kukhala ndi malo monga muja zikhalira ndi malo a banja chifukwa munthu wongobwera amavutika kupeza malo chifukwa palibe mizu yake yomwe angalondoloze.

Mwambowu umayenda bwanji?

Sikuti anthu amachita kusonkhana ngati momwe miyambo ina imakhalira, ayi. Chomwe chimachitika nchakuti mwana akabadwa, chinthu choyambirira n’kudziwitsa abale, makamaka amalume ake kapena azakhali, omwe amakanena kwa amfumu kenako anthu amamasuka kupita kukaona mwanayo ndi kumupititsira mphatso ngati ali nazo.

Mukati chinthu choyambirira mukutanthauzanji poti azaumoyo amati mwana akangobadwa, pompo ayamwe?

Zimenezo n’zoona koma apa tikukamba za mwambo. Umu ndimo makolo kalelo ankakhulupirira zinthu zisadayambe kusintha. Masiku ano miyambo yambiri ikutha pang’onopang’ono chifukwa cha maphunziro, anthu adayamba kuzindikira kuti miyambo ina imaononga mmalo mokonza zinthu.

Tsopano mukati ‘nkanulo’ timadziwa tanthauzo lokanula koma apapa pali mgwirizano wanji ndi mwambo?

Eya, ndimayembekezera funso limenelo. Kumbukani kuti ndati chimakhala chinthu choyambirira mwana akangobadwa ndiye kukanulako n’kutsegula mwanayo kukamwa kuti akhoza kuyamwa chifukwa walandiridwa pakati pa mudzi ndi banja lomwe wabadwiralo.

Inu mudachitapo mwambo umenewu?

M’zaka za mmbuyomo nditangokwatiwa kumene koma kenako ndidazindikira kuti n’kulakwa chifukwa chimakhala chilango kwa mwana. Mwachitsanzo, kumatheka kuti panthawi yomwe mwana wabadwa, palibe mayendedwe achangu malingana nkuti nthawiyo mauthenga amachita kukaperekedwa pakamwa kapena pakalata, foni kudalibe nthawi imeneyo ndiye mudikire munthu ayende kukapereka uthenga kuno mwana ali ndi njala.

Koma madotolo ndi anamwino amadziwa kuti izi zikuchitika?

Sindikudziwa koma zimachitika kwambiri chifukwa chochirira kwa azamba m’midzi. Mwina ndinene kuti kukhwefula ntchito za azamba am’midzi kudathandiza nawo kuchepetsa mwambo umenewu. Sindikukhulupirira kuti dotolo kapena namwino angalekerere izi zikuchitika.

Pano zinthu zili motani?

Panopa zinthu zili bwino chifukwa ndi maphunziro a zauchembere wabwino, anthu tidatsekuka m’maso. Mwina pena ndi pena zikhoza kumachitikabe poti uthenga umafika mosiyanasiyana koma nkhani yaikulu ndi yoti anthu ambiri adatsekuka m’maso chifukwa olo zokachirira kwa azamba am’midzi zidachepa.

Langizo lanu kwa amayi pankhani yokhudza mwambowu n’lotani?

Kwanga n’kuwalimbikitsa kuti miyambo inayi njofunika kuiganizira bwino. Uchembere si chinthu chamasewera, ayi, ngowawa. Ndiye munthu wanzeru sangalole kuti aziona mwana wake akulira chifukwa cha njala chifukwa choti akudikira kuti uthenga ukafike kumudzi kuti kuli mwana. Mwana wobereka wekha sungaponyere munthu wina ameneyo, ndi wako ndithu basi. Chofunika n’kutsatira malangizo a zaumoyo pa zakayamwitsidwe koyenera. n

Previous Post

Chonona chifumira kudzira

Next Post

ECA launches index to measure progress on integration

Related Posts

marriage | The Nation Online
Chichewa

Amapita kukagula zomwera tiyi

January 3, 2021
Chichewa

Anatchezera

January 3, 2021
An illustration of court proceedings
Chichewa

Odzipha akuchuluka

January 3, 2021
Next Post
Karingi: Progress has been uneven

ECA launches index to measure progress on integration

Trending Stories

  • Not yet given retirement benefits: Mutharika

    Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Wasteful Chakwera

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera has to instill unity

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • SA returnees in forced quarantine

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • AG disowns K750m compensation signature

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Emily Mkamanga

Citizens power brings change

January 24, 2021
Search Within

The rural farmer needs to take centre stage

January 24, 2021
My Thought

Spread hope not fear

January 24, 2021
Big Man Wamkulu

Hot babe wants to trap me, should I ran?

January 24, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.