Friday, February 26, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Kulumana pa ofunika kulandira chakudya

by Bobby Kabango
05/10/2018
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kusankha ovutikitsitsa kuti alandire thandizo la chakudya kuchokera ku boma kwavuta m’midzi ina pamene anthu ndi mafumu ayamba kulumana.

Izitu zadza pamene boma kudzera m’nthambi yoona za ngozi zogwa mwadzidzidzi ya Department of Disaster Management Affairs (Dodma) yayamba kugawa chakudya kwa anthu amene sadakolole chakudya chokwanira chifukwa cha ntchemberezandonda ndi ng’amba.

RelatedHeadlines

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

Aphungu akumana lolemba

Mtsutso pa zotsegulira sukulu lolemba

chimangade | The Nation Online
Kugawa chimanga kuli mkati m’maboma ena

Nthambi ya Dodma idapempha alangizi a zamalimidwe komanso ofesi ya DC m’boma lililonse kuti itolere maina a anthu amene athiphwa ndi njala.

Pa ntchitoyo, Dodma idatolera mabanja oposa 400 000 malinga ndi amene akuyendetsa ntchitoyi ku Dodma, Paul Kalilombe.

“Awatu ndi anthu oposa 2 miliyoni amene tikuyenera tiwapatse thandizo. Iyi ndi nambala yomwe tigwiritse ntchito dziko lonse,” adatero Kalilombe.

Koma nambalayi yakhumudwitsa mafumu ena amene akuti m’madera awo asiya anthu ambiri amene akhudzidwa ndi njala.

Gulupu Cheghama wa m’boma la Karonga kwa Paramount Kyungu adati m’dera lake anthu a mwa nyakwawa 5 ndi amene akhudzidwa ndi njala ndipo ayenera thandizo madzi asadafike m’khosi.

Cheghama adati anthu pafupifupi 300 ndi amene akuphupha ndi njala mwa mfumu Ngingekemo, Mwangwabila, Kazguli, Kazguli 2 ndi Mwaphoka.

“Chomwe tadabwa ife n’chakuti ngakhale tidapereka mainawo kuti boma liwathandize, iwo avomereza anthu 75 okha kuti ndiwo alandire chakudya,” adatero Cheghama.

Gulupu Mpochera ya kwa mfumu yaikulu Tsikulamowa m’boma la Ntcheu yati idapereka maina a anthu 250 amene adakhudzidwa ndi njala m’dera lake.

Poyamba akuti adadziwitsidwa kuti nambala ija ayidula ndipo anthu 115 ndi amene alandire thandize.

“Sabata yatha adaitananso mafumu onse, titapita akatiuza kuti nambala ija ayidulanso ndipo anthu 45 okha ndi amene alandire thandizo,” adatero Mpochera.

“Anthu 250 tonse takambirana kuti chimanga chikabwera, tonse tikhala pansi ndipo tigawana. Kaya aliyense adzatenga chimanga chodzadza mbale yokha bolani akaphike kaphala ndi kumwa,” adaonjeza.

Mfumuyo idati dera lake kapuchi ndi ng’amba ndi zimene zidasokoneza moti palibe amene adapeza ngakhale thumba limodzi la chimanga.

“Kunoko kuli moto, ineyo ndimakolola matumba oposa 10 koma chaka chino ndidapeza ndowa imodzi basi,” adatero iye.

Koma Kalilombe akuti nthambi yawo ikuyang’ana anthu okhawo amene alibe pogwira ngakhale ‘nkhuku yeniyeniyi’ alibe.

“Zoti chiwerengero chabwera chochepa bwanji ife zimenezo sitikudziwa chifukwa tidadalira ena kuti afufuze amene akufunika thandizo ndipo nambalayo tidapatsidwa.

“Komanso zoti chimangacho azigawana gulu ife sitikondwera chifukwa ndiye kuti akupha cholinga chathu kuti anthu asafe ndi njala. Anthu ena angovomereza basi kuti si onse amene angalandire thandizo,” adatero Kalilombe.

Iye adati pa banja la anthu pafupifupi asanu likulandira thumba limodzi la chimanga lolemera ndi makilogalamu 50.

Lipoti la Malawi Vulnerability Assessment Committee (Mvac) lomwe lidatuluka mwezi watha lidati anthu 3.3 miliyoni atuwa ndi njala chaka chino chifukwa choti anthu sadakolole chakudya chokwanira.

Kodi anthu enawo athawira kuti? Kalilombe akuti akamaliza gawo ayambalo, akhala pansi kuti aunguze za anthu 3.3 miliyoni amene Mvac yafunthula.

“Amene tikuwagaira pano sitidagwiritsire ntchito zomwe yatulutsa Mvac, koma tikamaliza gawoli ndiye kuti tikhala pansi kuti tigawirenso anthu 3.3 miliyoni amene Mvac yatulutsa,” adatero Kalilombe Lachitatu pamene amagawa chimanga m’maboma a Dowa ndi Mchinji.

Pofotokoza mmene ndondomekoyo ikuyendera, Kalilombe adati ntchitoyo yayamba sabata yatha m’maboma a Phalombe ndi Chikwawa.

Iye adati ndondomekoyi yachedwerako chifukwa mndandanda wa oyenera kulandira umachedwa kuperekedwa ku nthambi yawo.

Malinga ndi Kalilombe, sabata ino amayenera kugawa m’boma la Blantyre koma ofesi ya DC yachedwa kupereka mndandanda wa amene akuyenera kulandira.

“Tikufunitsitsa kuti pofika pa 14 mwezi uno tikhale titamaliza. Sitikupereka kwa mafumu koma kwa amene adalembedwayo,” adatero.

Previous Post

Expert urges govt to look to coal, uranium to ease blackouts

Next Post

Angwanjula osalembetsa

Related Posts

Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols
Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

February 19, 2021
Parliament in session
Nkhani

Aphungu akumana lolemba

February 19, 2021
Ophunzira azidziteteza ku Covid
Nkhani

Mtsutso pa zotsegulira sukulu lolemba

February 5, 2021
Next Post
Anthu akulembetsa manambala awo a foni

Angwanjula osalembetsa

Opinions and Columns

My Turn

On Covid vaccine liability

February 25, 2021
In pursuit of development

The Chinese approach to network-building

February 25, 2021
Business Unpacked

Back to the drawing board on budget

February 25, 2021
Rise and Shine

How do successful people think?

February 25, 2021

Trending Stories

  • Vokhiwa | The Nation Online

    Censorship Board acts on ‘Aunt Nellie’ videos

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside k6.2bn

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K780M Dodma Covid-19 feast

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Student’s rape case attracts CSOs attention

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Admarc secures K430bn to revamp operations

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.