Sunday, February 28, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

‘Kunyalanyaza kudzetsa ngozi’

by Temwa Mhone - Correspondent
17/06/2017
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Sabata yangothayi ngozi zidakuta dziko lino pomwe anthu 17 adafa.

Pamene anthu amati akhazikitse mitima pansi, anthu 8 atafa pa ngozi ya basi pamlatho wa Rivirivi ku Ntcheu komanso anthu 4 adamwalira ku Bunda ku Lilongwe ndi 4 kwa Magalasi mumzinda wa Blantyre, Lachisanu kudalinso ngozi ina mumzinda wa Blantyre pomwe munthu mmodzi adamwalira. Ndipo kudalinso ngozi zina ku Zomba, Mzimba ndi Mulanje.accident 5 | The Nation Online

RelatedHeadlines

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

Mneneri wa apolisi James Kadadzera adati ngozi zikuchuluka chifukwa chothamanga kwa madalaivala mosatsata malamulo.

Kadadzera adati madalaivala amakanika kuwongolera galimoto yothamanga kwambiri akadodometsedwa kapena kudzidzimutsidwa pamsewu.

“Mwa zina, ngozi ya galimoto yomwe idanyamula simenti ku Blantyre ndi chifukwa chokanika kumanga mabuleki koma nkhani ndi kuthamanganso kosatsata malamulo. Ukalondoloza zikwangwani za pamsewu, ngozi ikachitika sikhala yoopsa chifukwa munthu amatha kuwongolera komanso kupeweka. Vuto anthu akufuna kukafika msanga atanyamuka mochedwa zomwe zikusokoneza kayendedwe pamsewu,” adatero Kadadzera.

Iye adapempha okwera mabasi kuletsa madalaivala akamayendetsa galimoto mopanda dongosolo.

“Oledzera asaloledwe  kuyendetsa galimoto. Akamathamanga kwambiri chonde dziwitsani apolisi mungakumane nawo kuti adzudzule dalaivalayo. Tili tcheru kuonetsetsa kuti malamulo atsatidwe pamsewu popewa ngozi,” adatero Kadadzera.

Kaamba ka ngozizo, bungwe la akatswiri a zomangamanga la Malawi Institute of Engineers (MIE) ladzipereka kuthandiza apolisi ndi nthambi zonse za boma zoona za pamsewu kuthana ndi ngozi.

Chikalata chosainidwa ndi mkulu wa MIE Martin Chizalema chidati: “Pakuyenera kukhala kafukufuku wozama opeza gwero la kuchuluka kwa ngozi pamsewu. Tiyike mwachangu njira zothana ndi ngozi zoopsazi zomwe zikubwezera chitukuko cha dziko lino m’mbuyo.”

Chizalema adatinso anthu atenge umwini oteteza miyoyo yawo pa msewu komanso eni galimoto azionetsetsa kuti zili bwino komanso kupewa kuimba lamya akuyendetsa. 

Previous Post

Afufuza za mkalabongo

Next Post

Maliam Mdoko: Malawi Institute of Architects president

Related Posts

HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols
Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

February 19, 2021
Next Post
Maliam Mdoko—First female architects’ president

Maliam Mdoko: Malawi Institute of Architects president

Opinions and Columns

My Diary

Light that came with Covid-19

February 27, 2021
Guest Spot

Resurgence of albino killings deplorable

February 27, 2021
Back Bencher

Is violence a boomerang effect in DPP?

February 27, 2021
Off the Shelf

Sacrificial lambs of a dysfunctional system

February 27, 2021

Trending Stories

  • Court has declared Escom a private firm

    Court declares Escom private company

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K1.7bn Chisale assets seized

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • What the hell is APM doing with BJ?

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • HRDC alleges threats, intimidation from investor

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.