Friday, January 22, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Kupewa moto mu Dzalanyama kuteteza madzi

by Johnny Kasalika
25/10/2019
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Anthu ozungulira nkhalango ya Dzalanyama m’maboma a Lilongwe ndi Mchinji awapempha kuti apewe kuyambitsa moto mwachisawawa kuti ateteze ndi kusamalira zachilengedwe m’deralo.

Kudzera m’ndondomeko ya Conservation and Sustainable Management of Dzalanyama Forest Reserve (Cosma–DFR), nthambi ya za nkhalango yalimbikitsa ntchito yoteteza nkhalango ya Dzalanyama kuti zachilengedwe zibwezeredwenso m’nkhalangoyo zimene zithandizenso kuti kapezekedwe ka madzi kakhale kodalilika.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

deforestation | The Nation Online
Dzalanyama Forest

Kuchulukana kwa anthu okhala mozungulira nkhalango ya Dzalanyama komanso mumzinda wa Lilongwe, kukula kwa ntchito za mafakitale kuphatikizapo kusadalilika pa kagwedwe ka mvula ndi zina mwa zifukwa zimene zikuika pachipyezo nkhalangoyi komanso  kapezekedwe ka madzi mu mzindawu kotero mabungwe ndi nthambi zosiyanasiyana za boma zikuyenera kugwirana manja kupeza njira zochepetsera vutoli.

Kafukufuku waposachedwapa anapeza kuti chilengedwe m’madera ambiri ku  nkhalango ya Dzalanyama, chinaonongeka podula mitengo zimene zapangitsa kuti nthaka yambiri ikokolokere mumtsinje ndi kukakwilira damu la Malingunde. Zinyalala zikupitilira kutaidwa mwa chisawawa komanso anthu ambiri atsekula minda mphepete mwa nkhalangoyi zimene zathandizira pa kuonongeka kwa chilengedwe.

Pamwambo wozindikiritsa anthu kuopsa kwa moto ku chilengedwe umene unachitikira m’mudzi mwa Mkokoto ku Lilongwe, Moses Njiwawo amene amayendetsa ntchito za pulojekitiyo anadandaula ndi kuchuluka kwa moto umene ukuononga chilengedwe m’nkhalango ya Dzalanyama kuphatikizaponso kukwiririka ndi kuchepa kwa madzi m’damu la Malingunde.

Pulojekitiyo ikuyembekezekanso kupindulira kampani ya Lilongwe Water Board limene limapopa madzi kuchokera a m’madamu a Kamuzu 1 ndi 2 ku Malingunde. Kaamba ka matope ochuluka amene akudza chifukwa cha kukokoloka kwa nthaka, zapangitsa kuti madzi akhale ochepa komanso kulitengera bungweli ndalama zochuluka pa mankhwala amene limagwiritsa ntchito potsukira ndi kusefa madziwa zimene zapangitsa madzi azigulitsidwa pa mtengo okwera.

Mkulu wofalitsa nkhani ndi kuphunzitsa anthu m’pulojekitiyo, Charles Gondwe, adati posachedwapa pachitika kafufuku wotsimikiza kukula kwa malo amene anakhudzidwa ndi moto m’nkhalangoyi chifukwa zithunzi za mlengalenga kudzera pa makina a nternert zikuonetsa  kuti malo ambiri a nkhalango ya Dzalanyama munatenthedwa.

Mfumu Masumbankhunda idayamikira boma la Japan kaamba ka thandizo limene likupita ku nthambi ya za nkhalango pa chilinganizo cha Cosma—DFR zimene zotsatira zake zipindulira anthu okhala mozungulira nkhalangoyi.

Previous Post

Mangochi embarks on cervical cancer screening

Next Post

Mvula yayandikira, makuponi kulibe

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
fisp | The Nation Online

Mvula yayandikira, makuponi kulibe

Trending Stories

  • Escaped South African bail: Bushiris

    Bushiri says not seeking political intervention

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi closes in on hefty US deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Vendors back on streets amid Covid-19 surge

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi loses 5% of GDP on donor withdrawal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

These Freedoms

Where is God in the Malawi Vision 2063?

January 22, 2021
Business Unpacked

Towards Malawi2063, lessons from Vision 2020

January 20, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 20, 2021
In pursuit of development

India’s vaccine drive

January 20, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.