Friday, January 22, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Kusamvana pa zochotsa fizi

by Bobby Kabango
28/09/2018
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Ganizo la boma lochotsa fizi pa maphunziro m’sukulu za sekondale ladzetsa chisokonezo m’sukulu zaboma zina pomwe ophunzira ena akukana kulipira fizi ponena kuti boma lachotsa fizi.

Sabata zitatu zapitazo, boma lidalangiza mahedimasitala kuti asatolere ndalama za sukulu fizi, yomwe ndi K500. Ndipo Lachwiri, Unduna wa Maphunziro udalengeza kuti ophunzira asamalipire fizi komanso K500 yochitira zitukuko zosiyanasiyana pasukulu—General Purpose Fund. Koma undunawo udati ophunzira apitiriza kulipira ndalama za malo ogonera pasukulu.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Secondary school students | The Nation Online
Ophunzira m’sukulu za sekondale sazilipira fizi

Izi zadzetsa chisokonezo pakati pa makolo ndi ophunzira ena omwe akukana kulipira kalikonse kusukulu. Pofuna kumasula thumba la tambe, sukulu zina zikuchititsa misonkhano ya ophunzira ndi makolo kuti athetse mpungwepungwe womwe wabadwa.

Mphunzitsi wamkulu ku Mdeka m’boma la Blantyre, Leo Munyopowa akuti sabata ikudzayi akonza msonkhano wa makolo kuti awafotokozere chimene boma lachotsa.

“Makolo ena akukana kupereka ndalama ponena kuti boma lachotsa fizi, ndiye tangoitanitsa msonkhano wa makolo kuti tiwafotokozere tokha,” adatero Munyopowa.

Chimangeni Gaso wa m’boma la Dedza ndipo amalipirira ophunzira 7, adati kumenekonso padali kusamvana kuti makolo asunge ndalama kenaka boma lidzaitanitsenso.

“Koyambirira zidavuta, ana amadabwa pamene amabwezedwa. Chifukwa cha ichi, tidapita kusukuluko kuti akatifotokozere chenicheni chimene boma lachotsa,” adatero.

Koma nduna ya zamaphunziro Bright Msaka yati kutsatira thandizo lomwe boma lalandira la K6.7 biliyoni kuchokera ku America, ilo laganiza zochotseratu fizi.

Msaka adati kuyambira pa 1 January chaka chamawa, sukulu zauzidwa kuti zisadzatolerenso ndalama yamabuku (textbook revolving fund) yomwe ndi K250, ndalamayi imaperekedwa pa chaka kamodzi.

Izi zikutanthauza kuti kuyambira January chaka chamawa, ophunzira adzilipira ndalama yogonera ngati akugonera pasukulupo ndi zina zoyendetsera sukulu.

Nduna ya zachuma, Goodall Gindwe adati K6.7 biliyoni ndi ndalama yambiri kuposa yomwe boma limalandira m’sukulu ophunzira akalipira zimene lachotsazo.

“Kuchotsa kwa ndalamako sizikhudza boma chifukwa ndalama talandirayo ndi yambiri komanso igwiritsidwa ntchito kumanga sukulu zina,” adatero Gondwe.

Koma mkulu wa bungwe loona zamaphunziro la Civil Society Education Coalition (Csec), Benedicto Kondowe ganizoli ladza modzidzimutsa zomwe zingabweretse mpungwepungwe.

“Ili ndi ganizo la ndale lomwe silingatipatse chilimbikitso. Taona mavuto ochuluka ndi sukulu za pulaimale zaulele zomwe boma lidakhazikitsa, apapa amayenera ayambe aunguza bwino asadabwere ndi ganizoli,” adatero Kondowe.

Komabe anthu ena ndi okondwa ndi ganizoli. Masida Mhango wa m’mudzi mwa Wiskematumbo kwa mfumu Mwahenga m’boma la Rumphi adati chaka chatha, adalephera kuphunzitsa mwana wake chifukwa adalibe ndalama.

“Chaka chatha mwana wanga wa Folomu 3 pasukulu ya Ng’onga adatha chaka chonse wosapita kusukulu chifukwa chosowa ndalama. Izitu zidachitika chifukwa ulimi sudayendenso. Apa ndiye kuti boma laganiza,” adatero. Steven Pembamoyo ndi Martha Chirambo athandizira.

Previous Post

Akana kulemba UTM

Next Post

Patricia Kaliati: Mulanje West MP

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Kaliati (L) at previous UTM rally

Patricia Kaliati: Mulanje West MP

Trending Stories

  • Escaped South African bail: Bushiris

    Bushiri says not seeking political intervention

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi closes in on hefty US deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Vendors back on streets amid Covid-19 surge

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi loses 5% of GDP on donor withdrawal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Business Unpacked

Towards Malawi2063, lessons from Vision 2020

January 20, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 20, 2021
In pursuit of development

India’s vaccine drive

January 20, 2021
My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.