Tuesday, January 26, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Kusanthula ntchito ya fisi

by Steven Pembamoyo
29/07/2016
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Miyambo ya makolo ndi yambiri ndipo ina akuti siyofunika kupitirira chifukwa ikuthandizira kufalitsa kachilombo koyambitsa matenda a Edzi. Sabata yathayi, mafumu adali ndi msonkhano mumzinda wa Lilongwe wokambirana za miyambo. Umodzi mwa miyambo yomwe ikukanidwa ndi mwambo wa fisi omwe ambiri amausokoneza ndi mwambo wa kusasafumbi. STEVEN PEMBAMOYO adacheza ndi Senior Chief Lukwa wa ku Kasungu pa zamwambowu. Adacheza motere:

Lukwa: Mafumu tikuthana ndi miyamboyi
Lukwa: Mafumu tikuthana ndi miyamboyi

Gogo tandimasuleni eti mwambo wa fisi ndi mwambo wanji?

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Pamwambowu munthu amalembedwa ganyu yobereka ana m’nyumba ya munthu yemwe zikumukanika. Imakhala ganyu ngati kuti munthu wagula galimoto koma satha kuyendetsa ndiye amalemba munthu yemwe amatha kuyendetsa kuti azimuyendetsera nkumulipira.

Basi? Nanga Fisi uja amalowa m’nyumba yoti mwini wake wamwalira kapena asungwana akuchoka kutsimba ndi uti?

Choyamba ndikonze kuti amene uja si fisi. Umene uja ndi mwambo wa kuchotsafumbi. Fisi ndi pokhapokha ngati wina akulephera kubereka ana m’nyumba ndiye pofuna kuti asachite manyazi m’mudzi, amalemba fisi kuti amuberekere mwana kapena ana koma zimakhala zachinsinsi zongodziwa bambo, mayi ndi fisiyo basi.

Nanga kusasafumbi nkutani? Ndikufunatu ndimvetsetse. Kusasafumbi kuli pangapo. Nthawi zina mwamuna akamwalira, m’nyumbamo mumabwera mwamuna wina kudzagona ndi mai osiyidwayo akuti kugoneka mzimu wa malemuyo. Nthawi zina mkazi akachotsa pakati kapena anamwali akamachoka kutsimba, amatenga mwamuna woti agonane nawo pokhulupirira kuti kutero ndiye kuti ayendetsa mwambo momwe uyenera kukhalira.

Malipiro ake amakhala chiyani?

Zimatengera pangano la awiriwo, ena amatha kulipirana mbuzi kapena nkhuku mwinanso ndalama. Apa palibe dipo lenileni lokhazikika chifukwa nzachinsinsi moti ozidziwa amakhala okhawo okhudzidwa.

Nanga pambuyo pake fisi atatembenuka kuti akufuna ana ake zingathe bwa?

Ichi nchibwana chachikulu chifukwa potengera momwe mwambowu umayendera, iye akagwira ntchito pathupi nkuoneka, akangolandira zake basi kwatha zammbuyo muno nza eni nyumbayo. Kuchita masewera, akuluakulu akhoza kugwirapo ntchito chifukwa woteroyo waphwanya mwambo wachinsinsi omwe adavomereza yekha.

Boma ndi mabungwe amati miyambo yotereyi ndi yoipa makamaka nkubwera kwa kachilombo koyambitsa matenda a Edzi, muti bwanji?

Zimenezo nzoona zokhazokha moti mafumu kuyambira ku Chitipa mpaka ku Nsanje, Nkhotakota mpaka Mchinji tidagwirizana chimodzi kuti m’madera mwathu miyamboyi isamachitike. Tidachita izi dala

chifukwa omwe amazunzika kwambiri ndi amai ndi asungwana chifukwa kumatheka bambo mmodzi kusasafumbi asungwana kapena amai angapo choncho matenda a Edzi sangathe ayi.

Nanga poti mwambo ndi mwambo, mungathe kuwaletseratu anthu?

Mfumu siyilephera makamaka pomwe ikutsogolera anthu ake pachinthu chabwino. Monga ndanena kale, mafumu tidamanga fundo imodzi moti kumupeza wina akuchita khalidweli, timamulanga potengera malamulo omwe tidamanga komanso timaonetsetsa kuti onse okhudzidwawo akayesedwe kuchipatala ngati sadavulazane ndi matenda.

Malangizo anu ndiwotani kwa anthu omwe satha kubereka koma amafunitsitsa kukhala pa banja?

Malangizo ndi wosavuta: kuli bwino asakwatire kapena kukwatiwa apo biii, alimbe mtima kudzasekedwa osada nkhawa ayi. Chomwe ife tikunena ngati mafumu nchakuti asakwatilire dala akudziwa kuti zimawavuta kenako azidzalowetsa fisi m’nyumba. n

Previous Post

Nkhanza zapolisi zanyanya

Next Post

‘Malawi is a stable democracy’

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Haugen: We are committed

‘Malawi is a stable democracy’

Trending Stories

  • covid 2 | The Nation Online

    SA returnees in forced quarantine

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Health workers not spared by Covid-19

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Smuggling of flour, cooking oil rising, say traders

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • court rebuffs apm on frozen account

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

My Turn

Behaviour change key in Covid-19 fight

January 25, 2021
Emily Mkamanga

Citizens power brings change

January 24, 2021
Search Within

The rural farmer needs to take centre stage

January 24, 2021
My Thought

Spread hope not fear

January 24, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.