Monday, March 8, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Kutumiza ana kundende si yankho—Jaji

by Steven Pembamoyo
11/10/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 

Jaji wa kubwalo lalikulu (High Court) Justice Annabel Mtalimanja wati kuthamangira kugamula ana achichepere kukagwira ukaidi kundende ndi njira imodzi yopititsira uchigawenga patsogolo.

RelatedHeadlines

Akana ndalama za Covid-19

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

Mtalimanja adalakhula izi posachedwapa poyamikira ntchito yomwe likugwira bungwe losamala ana ndi kuwaphunzitsa zachikhalidwe chabwino la Chisomo Children’s Club.

Mtalimanja: Ana asapite kundende  za akulu
Mtalimanja: Ana asapite kundende
za akulu

Mtalimanja adati ana achichepere akapita kundende amakakumanako ndi anamandwa pazauchigawenga omwe amawagawira nzeru zolakwika ndipo akatuluka amakayeserera zomwe adaphunzirazo moyo wauchigawenga n’kupitirira.

“N’koyenera kwake kuti munthu yemwe walakwira lamulo alandire chilango koma mpofunika kuunika bwino kuti kodi chilango chomwe chikuperekedwacho zotsatira zake zikhala zotani chifukwa cholinga cha chilango n’kuwongola, koma nthawi zina kumatheka kukhotetserakhotetsera.

“Chomwe ndikutanthauza apa n’chakuti chilango chomwe chikuperekedwa chizifanana ndi msinkhu wa munthu wolangidwayo. Ana achichepere, mwachitsanzo, akhoza kuongoka polandira maphunziro achikhalidwe chabwino,” adatero Mtalimanja.

Bungwe la Chisomo Children’s Club lidayambitsa pologalamu ya Mwayi Wosinthika yomwe amaphunzitsa achinyamata opezeka olakwa za mmene angasinthire moyo wawo ndi kukhala achinyamata odalirika.

Mkulu wa bungweli Charles Gwengwe adati pakalipano bungweli laphunzitsapo achinyamata ochuluka ndipo pano ena adasinthiratu moti akugwira ntchito, ena akuchita bizinesi ndipo ena adabwerera kusukulu.

“Sitiphunzitsa zakusukulu, ayi koma mmene munthu angakhalire ngati munthu pakati pa anzake. Ambiri mwa ana omwe timaphunzitsa amakhala ndi milandu ing’onoing’ono monga kupezeka malo olakwika ngati omwera mowa, kuchita mchitidwe woyendayenda ndi kuba pakhomo pa makolo awo.

“Timayenda m’malo oweruzira milandu, m’ndende, ndi kupolisi kusakasaka ana a milanduyi ndipo tikawapeza timapanga dongosolo lowatenga kuti tikawaongole,” adatero Gwengwe.

Pologalamuyi imayenda ndi thandizo lochokera ku Ireland kudzera mu nthambi yolimbikitsa njira zina za kaweruzidwe ka milandu yomwe imatchedwa kuti mpatutso (Diversion Program).

Tags: Justice Annabel Mtalimanja
Previous Post

Kwaterera kwa ntenje

Next Post

Mzuzu’s missionary of hope

Related Posts

covid relief | The Nation Online
Nkhani

Akana ndalama za Covid-19

March 6, 2021
Blantyre’s ‘best building’: St Michael and All Angels Church
Nkhani

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

March 6, 2021
People queue to buy maize at Admarc market
Nkhani

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

March 6, 2021
Next Post
mzuni. | The Nation Online

Mzuzu’s missionary of hope

Opinions and Columns

Search Within

Cut out the religious dogma from Covid-19 vaccines

March 7, 2021
Big Man Wamkulu

Won’t libido-boosting pills kill him?

March 7, 2021
Political Uncensored

Pulling rank…

March 7, 2021
People’s Tribunal

Ombudsman has challenged us all

March 7, 2021

Trending Stories

  • Protesting pay cut: Mathanga

    Court blocks RBM deputy governor salary cut

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • RBM sues Mulli, 4 others

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Police, DPP, ‘ignore’ court order

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt to finance 15 major projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Ministry plans to export 1m tonnes surplus maize

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.