Tuesday, March 2, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Kwaterera ku DPP

by Steven Pembamoyo
29/08/2020
in Chichewa
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Madzi achita katondo kuchipani cha Democratic Progressive Party (DPP) chomwe chidali m’boma kwa zaka 6 zapitazo ndipo chidagwetsedwa ndi m’gwirizano wa Tonse Alliance pachisankho chobwereza cha pa 23 June 2020.

Lachinayi lapitali anthu adadzidzimuka ndi kuchotsedwa kwa mlembi wamkulu wachipanicho Greselder Jeffrey yemwe mtsogoleri wa DPP Peter Mutharika adamuchotsa popanda msonkhano waukulu wachipani.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

Amwalira atathawa m’chipatala

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Jeffrey adachotsedwa pampandowo atauza nyuzipepala ya The Nation kuti chipanicho chikufunika msonkhano waukulu wokasankha atsogoleri ena makamaka pulezidenti, chifukwa Mutharika wapangako mbali yake.

apm | The Nation Online
Mmbuyomu zinthu zikuyenda: Mutharika kupatsana moni ndi Greselder

Mutharika adatsogolera DPP pachisankho cha 2014 chomwe DPP idachotsa People’s Party (PP) m’boma, Mutharika yemweyo adaimira DPP pachisankho cha 2019 chomwe chidakanidwa atapambana kenako adagwetsa chipanicho pachisankho chobwereza cha 2020.

Pazisankho zonse ziwiri cha 2019 ndi 2020, Jeffrey ndiye adali mlembi wamkulu wachipanicho.

Polankhula ndi The Nation Lachitatu, Jeffrey yemwe adakana kuti sachoka pampandowo adati iye aonetsetsa kuti msonkhano waukulu wachipani uchitike.

“Anthu m’chipani akufuna msonkhano waukulu chifukwa akuona kuti ndi njira yokhayo yokonzera chipani. Sindichoka ndikhala m’chipani ngati mlembi wamkulu sindikupita kulikonse,” adatero iye.

Akadaulo pa ndale ayikira kumbuyo Jeffrey kuti akutsata ndondomeko yoyenera ya demokalase pofuna kuti adindo azisankhidwa ndi anthu a m’chipani osati munthu mmodzi chifukwa chotenga chipani ngati chake.

Rafiq Hajat wati chipani cha DPP chikufunika msonkhano waukulu kuti chibwezeretse chikhulupiriro mwa Amalawi.

“Vuto lomwe lilipo ndi loti zipani za m’Malawi muno zimakhala ngati chuma cha munthu kapena banja ndiye za demokalase sawerengera amafuna mwini wakeyo ndiye azinena zochita. Ichi n’chifukwa chake zipani zambiri zimafa mosadziwika,” watero Hajat.

George Phiri wa kusukulu ya ukachenjede ya  University of Livingstonia wati popanda msonkhano waukulu, chipani cha DPP chikhoza kudzibaya chokha kumsana chifukwa chikupereka uthenga wolakwika kwa Amalawi.

“Uthenga omwe akupereka ndi woti safuna kumva za anthu. Ngati sadakonzeke za msonkhano waukulu akadangonena mmalo mochita kuonetsa kuti sakufuna msonkhano omwe uli m’malamulo a chipani chawo,” watero Phiri.

Naye Ernest Thindwa wa ku Chancellor College wati pafikapa, Mutharika akadangovomereza kuti wakula ndipo akuyenera kusiya chipani m’manja mwa omwe ali ndi mphamvu zoyendetsera.

“Mutharika amayenera kudziwa kuti mbiri ya chipani idaipa pautsogoleri wake ndiye zokakamiza izi siziwapindulira ayi,” watero Thindwa.

Lachinayi lapitali, komiti yaikulu ya DPP imakumana kunyumba kwa Mutharika ku Mangochi koma Jeffrey adati Mutharika adamuletsa kukakhala nawo pamsonkhanowo ngakhale udindo wake umamuyenereza kukhala m’komitiyo.

Aka si koyamba kuti chipani cha DPP chisemphane ndi akuluakulu ena chifukwa chodzudzula Mutharika kuti wakula ndipo asiyire ena mpando kuti apitirize. 

Previous Post

The hounds surround APM even more

Next Post

Malingaliro pa malonjezo a Tonse

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
death e1465557792659 | The Nation Online
Chichewa

Amwalira atathawa m’chipatala

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Next Post
Namiwa: An investigation is needed

Malingaliro pa malonjezo a Tonse

Opinions and Columns

My Turn

Tackling global slowdowns

March 1, 2021
People’s Tribunal

Burglary at the hill

February 28, 2021
Search Within

Perseverance landed, is alive and well

February 28, 2021
Emily Mkamanga

Tasting your own salt in politics

February 28, 2021

Trending Stories

  • Olela: We are excited

    K5bn Sunbird Waterfront hotel opens May

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • We won’t give Up—Chakwera

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Court declares Escom private company

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.