Friday, March 5, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Limbani Simenti: Kukangalika pa zoimba

by Chimwemwe Sefasi
13/09/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Ku Malawi kuno kuli oimba zauzimu ochuluka. Mmodzi mwa iwo ndi Limbani Simenti yemwe akudziwika bwino. Iyetu amadziwika kwambiri ndi nyimbo ya Ndikuoneni. CHIMWEMWE SEFASI adamupeza mnyamata wa ku Ndirandeyu ndipo adacheza naye motere:

Ndikudziwe….

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

Amwalira atathawa m’chipatala

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Dzina langa ndine Limbani Simenti, ndimachokera chigawo cha kumwera, m’boma la Thyolo, T/A Nsabwe, m’mudzi wa Matekenya.

Adaimba ‘Ndikuoneni Baba’: Simenti
Adaimba ‘Ndikuoneni Baba’: Simenti

Kodi zoimbaimbazi mudayamba liti?

Inetu zoimbaimba ndidayamba pa kanthawi, pamene ndidali sitandade 4, koma chidwi chidayamba kundipeza pomwe ndidayamba kuimba kwaya ya Mount Sinai mu 1999. Mu 2010 pomwe ndidayamba kuimba mu Praise Team ya mpingo wa All for Jesus. Mu 2011 mpomwe ndidatulutsa chimbale changa cha Lungisani Mpiro kutanthauza kuti konzani moyo wanga.

 

Kodi nkhani zamaimbidwe umaziona bwanji pa Malawi pano?

Nkhani za maimbidwe zili bwino pa Malawi. Kungoti ubwino weniweni umaoneka munthu ukakhala ndi chidwi komanso ukaikapo mtima wako wonse, ndi kudziwa chomwe ukufuna pamoyo wako chifukwa zomwe umabzala ndi zomwe umakolola.

 

Kodi nyimbo yako ya Ndikuoneni imatiphunzitsanji?

Ndikuoneni Baba ndi nyimbo yomwe mumapezeka mphamvu. Iyi ndi nyimbo yomwe imatifupikiritsa chifupi ndi Mulungu. Mwachitsanzo, ndikamati Baba ndifuna ndikuoneni imakhala ikusonyeza ife tili paubale weniweni ndi Mulungu, ndi nyimbo yomwe ine uthenga ndimati ndikaumva ndimaona kuti Mlengi ndi amene adandipatsa uthengawo kuti ndilakhule kudzera m’nyimbo posonyeza kuti nkhawa zathu timatula kwa Yehova ndi kuonetsa ubale weniweni ndi Mulungu. Nyimbo imeneyi imapezeka m’chimbale chotchedwa Lungisani Mpiro chomwe mudali nyimbo 12 monga Uligwindi, Njoka Yokalamba, Yesu Salemphera ndi zina, pamene DVD idatuluka ndi dzina loti Ndikuoneni.

 

Kodi chaka chino Amalawi ayembekezere zotani kuchoka kwa iwe?

Ndikuwalonjeza Amalawi kuti tisanafike kumapeto a chaka chino cha 2015 ndiwapatsira chimbale chomwe chili ndi nyimbo 12, zomwe panopa ndamaliza kujambula.

Previous Post

Catholics launch Bible Month, study lessons

Next Post

FAM ignores revenue impact in Standard Bank

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
death e1465557792659 | The Nation Online
Chichewa

Amwalira atathawa m’chipatala

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Next Post
Big Bullets

FAM ignores revenue impact in Standard Bank

Opinions and Columns

In pursuit of development

The future of aid

March 4, 2021
Business Unpacked

Take time to know your pension’s worth

March 4, 2021
Rise and Shine

How do successful people think?

March 4, 2021
My Turn

Unmasking Covid-19 vaccine

March 3, 2021

Trending Stories

  • Under probe: The Reserve Bank building in Mzuzu

    Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Minister wants Msundwe police officers prosecuted

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Charcoal traffickers fined K800 000, vehicle forfeited

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Macra to introduce fees for phone numbers

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawian boxer risks life ban

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.