Tuesday, April 20, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

‘Mafumu adyera’

by Bobby Kabango
08/12/2017
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Akatswiri pandale komanso mafumu adzudzula zomwe adachita mafumu ena poyenda ndawala ulendo ku Nyumba ya Malamulo komwe amakatsutsa mabilo a zisankho.

Lachitatu sabata yatha mafumuwo motsogozedwa ndi mfumu Ngolongoliwa, Lundu, Kyungu mwa ena adakasiya kalata kunyumbayo.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

Chiefs | The Nation Online
Akudana ndi 50+1: mafumuwo ku Nyumba ya Malamulo

Iwo adati sakugwirizana ndi mabilowo omwe mwa zina akufuna kuti mtsogoleri wadziko azisankhidwa ndi anthu oposa 50 pa 100 aliyonse.

Mafumu ena monga Kabunduli wa m’boma la Nkhata Bay wati mafumu amene akupanga izi ndi adyera ndipo akungogwiritsidwa ntchito ndi boma.

“Ili ndi dyera, ufumu ausambula,” adatero Kabunduli. “Mafumu timaimira banja, kodi zonena za banja langa ndingamanene kuti dziko lonse likugwirizana nazo?

“M’ndani adawauza kuti Amalawi akukana 50+1? Ife anatifunsa mafumuwo?” Atafunsidwa ngati iye adaitanidwa kukakhala nawo pa zochitikazo, Kabunduli adati.

“Sangandiuze [za chibwanazo]. Zimenezo amatuma mafumu andale, komanso adyera.”

Mphunzitsi wa za ndale wa ku Chancellor College (Chanco), Happy Kayuni, adati iyi si ntchito yomwe mafumu amayenera kugwira ndipo uku ndi kududuka.

“Timawadziwa mafumu kuti amakhudzidwa ndi nkhani za chikhalidwe, komanso chitukuko. Koma tikuona panozi ndi zosiyana,” adatero Kayuni.

“Andale ndiwo akugwiritsira ntchito molakwika mafumuwa. Ukutu ndi kuphwanya chikhulupiriro chomwe anthu ali nacho mwa mafumuwa.”

Malinga ndi Kayuni, ntchito za mafumuwa zasokonekera kaamba koti akulowerera nkhani zosawakhudza.

“Palibe angaike chikhulupiriro mwa mafumuwa potengera ndi zomwe akuchita. Sizikusiyana ndi andale,” adatero.

Pothirirapo ndemanga pa za kusuluka kwa mphamvu zawo, Kabunduli adati iye wakhala akupita ku Mozambique ndi Zambia komwe anthu amamupatsa ulemu monga mfumu zomwe m’dziko muno sizikuchitika.

“Pano tasanduka andale chifukwa nkhani zomwe si zanthu tayamba kulowerera nawo,” iye adatero.

Mafumu ena a m’maboma a Ntcheu, Mwanza, Mangochi, Mzimba ndi Dedza omwe adakana kutchulidwa adati zomwe anachita mafumuzo ndi maganizo awo osati a anthu kapena mafumu onse.

Pa 29 July 2010, dziko lino lidasintha mbendera yake. Mafumu ndiwo adali patsogolo kuthandizira boma lolamula la DPP kuti mbenderayo isinthe.

Koma pa May 28 2012 yemwe adali mtsogoleri wa dziko lino, Joyce Banda, adabwezeretsa mbenderayo.

Joseph Chunga, mphunzitsi wina wa ndale wa ku Chanco, adati mafumuwo adachita izi pofuna kunyengerera boma kuti boma liwakweza udindo.

Ngolongoliwa adati sangalankhule pafoni koma pamaso. Pamene Lundu adati ndiwotangwanika ndipo aimbabe akakhala ndi mpata.

Avatar
Bobby Kabango
Previous Post

‘Delilah’ singer no saint

Next Post

Kuli zionetsero pa 13 December

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
To lead the delegation: Chilima

Kuli zionetsero pa 13 December

Opinions and Columns

Big Man Wamkulu

Hot babe wants to trap me, should I ran?

April 18, 2021
Political Uncensored

Mighty mess!

April 18, 2021
My Thought

Chakwera’s indecisiveness will be his downfall

April 18, 2021
People’s Tribunal

Cut the crap, act on abuse forthwith

April 17, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Minister of Labour Ken Kandodo

    Ministry defends ‘borrowing’ of Covid-19 funds

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera bites

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chilima in public projects inspection

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • OPC frustrates roads projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malewezi’s career, political profile

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.