Sunday, January 17, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Makhansala aderera alawansi

by Steven Nhlane and Rebecca Chimjeka
05/12/2020
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kucha kwa Lolemba lapitali Amalawi adadzuka ndi nkhani yododometsa kuona adindo (makhansala) akulalata poyera kudelera alawansi ya K20 000 ndipo akunena modzithemba kuti iwo amayembekezera kuti alawansiyo ikhala K200 000 khansala aliyense.

Koma mongokumbutsira, K20 000 yomwe makhansalawo amadelera ndi yokwanira kugula matumba anayi afetereza otsika mtengo yemwe alimi ambiri kumudzi akusowa ndi chenje chokwanira K2 000 pamwamba pake.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Athotha a kabaza opanda mapepala

Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Chakwera adakumananso ndi makhansala a ku Mzuzu koma izi sizidaphulike

Kanema ya makhansala a mumzinda wa Blantyre yomwe Tamvani ikusunga mpaka lero ikuwonetsa makhansalawo akulalata kuti zomwe akuwona (polandira K20 000 ngati alawansi) sizikugwirizana ndi Kanani yemwe amayembekezera.

“Kodi Kenaniyo ndi ameneyu? Kumalandira K20 000 pomwe kale anzathu akakumana ndi Pulezidenti ankalandira K200 000. Ayi sizoona ndiye bolanso kalelo,” akutero makhansala mukanemayo.

Lamulungu lapitalo, makhansala a mumzinda wa Blantyre adakakumana ndi mtsogoleri wa dziko lino Lazarus Chakwera kunyumba ya boma ya Sanjika ndipo utatha mkumano wawo adapatsidwa K20 000 aliyense ngati alawansi yokhalira pamkumanowo.

Koma mkulu woyendetsa mapologalamu kubungwe lowona zoti zinthu zikuyenda m’chilungamo ndi mtendere la Catholic Commission for Justice and Peace (CCJP) Boniface Chibwana wati izi zikuonetseratu poyera kuti adindo m’dziko muno sazindikira chomwe adakhalira pampando.

“Zikungoonetsa kuti tikadali ndi maganizidwe a kalekale woti pampando mpodyera kuiwala kuti kukhala pampando ndi mpata wotsogolera anthu. China chomwe adindowa akuiwala n’choti chomwe ana akuona lero chikukhazikika mwa iwo choncho adzapanga zomwezo nthawi yawo yokhala pampando ikadzafika,” adatero Chibwana.

Iye adati potengera zomwe zili mkanemayo, zikuwonetseratu kuti makhansalawo adalibe ntchito ndi zokambirana zomwe adali nazo ndi Pulezidenti koma kuti mitima yawo idali pa ndalama basi.

“Mpata okumana ndi Pulezidenti ndi wosowa kwambiri moti makhansalawo akadakhala ena akadagwiritsa ntchito mpatawo kukambirana ndi Pulezidenti nkhani zachitukuko m’madera mwawo,” adatero Chibwana.

Koma mkulu oyendetsa ntchito za likulu la makhansala la Malawi Local Government Association (MALGA) Charles Chunga wati anthu akutengera zomwe zili mukanemayo pamgong’o.

Iye adati makhansalawo amangoseleula pa zomwe amachita ndi kunenazo koma osati kuti adali ndi mtima woderera alawansiyo.

“Palibe lamulo kapena ndondomeko yomwe imanena kuti alawansi ya makhansala ndizingati. Iwo amakumana ndikukambirana ndi aliyense yemwe wawafuna ndipo zimatengera owayitanayo kuti awapatsa alawansi yochuluka bwanji ndiye sikuti aphunguwo amadelera,” watero Chunga.

Iye adati likululo lilibe ndondomeko yeniyeni yokhazikitsira mwambo pakati pa makhansala ndipo limagwiritsa ntchito makhansala omwewo kudzudzula ndi kuwongola anzawo omwe awonetsa khalidwe losokonekera koma pakali pano palibe khansala yemwe wafika pofunika mwambo.

“Anthu akukokomeza kwambiri nkhaniyi chifukwa munthu olalata saonetsa nkhope yoseka ngati momwe makhansala aja akuwonekera mukanemayo,” adatero Chunga.

Woyang’anira zofalitsa nkhani kunyumba za boma Sean Kampondeni adauza atolankhani Lolemba kuti boma la Tonse Alliance silidabwere kudzadzadza matumba a anthu ndi ndalama.

“Boma ili lidabwera kudzakonza zinthu ndi kubweretsa chitukuko osati kudzagawa ndalama ayi ndiye sitingasinthe chikonzero chathu chokonza dziko kuti tiyambe kugawa ndalama nkumawoneka abwino,” adatero Kampondeni.

Ndipo Chibwana adati njira yokhayo yothana ndi nthenda yongofuna kulandira n’kukhazikitsa lamulo loona za zipani za ndale momwe mfundo ina ndi kuonetsetsa momwe zipani zimapezera ndi kugwiritsira ntchito ndalama.

Anthu osiyanasiyana pamchezo wa pa Intaneti apereka ndemanga zodzudzula zomwe makhansalawo adachita.

Previous Post

Malawi’s bundle of contradictions

Next Post

Fertilising further poverty through AIP mess

Related Posts

Malango: Covid-19 ikadalipo
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Njinga za kabaza zawanda kwambiri m’Malawi
Nkhani

Athotha a kabaza opanda mapepala

December 4, 2020
Next Post
Potential beneficiaries desperate to redeem their farm inputs

Fertilising further poverty through AIP mess

Discussion about this post

Trending Stories

  • covid death | The Nation Online

    Tonse owes ‘ife tonse’ an apology

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Nocma in race against time

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Imbibers defy Covid-19 guidelines

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 mars cabinet review

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Locked with hubby’s brother

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Bottom Up

For 20 Pounds John Chilembwe was betrayed

January 16, 2021
My Diary

Tonse owes ‘ife tonse’ an apology

January 16, 2021
Off the Shelf

Accomplices in genocide

January 16, 2021
Back Bencher

On verge of collapse due to Covid-19

January 16, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

WhatsApp us

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.