Tuesday, April 20, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Malawi ali mu mdima

by Bobby Kabango
01/12/2017
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Zasokonekera! Malawi ali pamoto wosaneneka ndi kuzimazima kwa magetsi. Anthu akumudzi akugona kuchigayo kudikira magetsi pamene alimi a ng’ombe zamkaka akutaya mkaka.

Ndi Loweruka usiku cha m’ma 10 koloko pamene timafika pachigayo cha Muhiriri m’dera la mfumu Kasisi m’boma la Chikwawa.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

Blackouts 1 | The Nation Online
Si zidaonekenso: Amayi kugona m’chigayo podikira kugayisa chimanga

Anthu 16, atatu mwa iwo abambo, ali pachigayopa kudikira magetsi. Anayi okha ndiwo ali maso pamene onse agona.

Matumba a chimanga komanso mapira andandana kuti magetsi akayaka agayise. Magetsiwatu akuti adazima Lachisanu mmawa.

Pafupi nane pali mayi wachikulire, ndi wothodwa. “Sindikudziwa kuti ayaka nthawi yanji, koma ndabwera pano mmawa cha m’ma 7,” adatero mayiyu, Ezelesi Stanton wa zaka 60.

Ngakhale atayaka, Stanton sangabwerere kumudzi chifukwa wayenda mtunda wa makilomita 8.

POWER BY BOBBY | The Nation Online
Awa ndiye ndi mavuto adzaoneni: Anthu akudikira magetsi ayake pa chigayo cha ku Chikwawa

“Kunyumba kulibe ufa, ndasiya ana ndi bambo. Kuti ndibwerere ndiye sitikadya chifukwa ufa udatheratu,” adatero mayiyu.

Awa ndiwo mavuto amene akungana kumudzi pamene bungwe lopanga magetsi la Electricity Generation Company of Malawi (Egenco) likungopanga pafupifupi theka la magetsi amene dziko lino likufuna.

Izi zikupangitsa kuti anthu ena, monga aku Chikwawa, azitha masiku awiri osaona magetsi.

Eleni Kalavina wa m’mudzi mwa Chikalumpha akuti mwezi wa November wokha wagona kuchigayo kanayi, kudikira magetsi kuti agayise.

Pamene timafike pa chigayopa, Kalavina adali m’tulo. Iye adadzidzimuka pemene mwana wake wa miyezi 7 amalira. Iye adadzuka ndi kumuyamitsa.

Pachigayopatu pali ana oyamwa anayi amene agona kumimba kwa amayi awo.

“Ambuye adzatitenge, dziko lino latopetsano,” Kalavina adatero. “Mwina n’kukaona zina kumwambako.”

“Kodi Ambuye abwera liti? Tatopa abale.” Iye adati kuzimazima kwa magetsi kukuzuza moyo wawo komanso mabanja awo.

“Nthawi zina amunanga amandikaniza kuti ndisadzagone kuno poganizira kuti mwina ndikukayenda ndi amuna ena pamene si choncho,” adatero.

Pamene nthawi imathamangira 12 koloko usiku, bambo wina adafika pamalopo mokuwa. “Kodi kuli akazanga kumeneko?”

Bamboyu, Davie Kachiza wa zaka 49, amachokera m’mudzi mwa Josamu m’dera la mfumu Katunga-mtunda wa makilomita 7-kudzasaka mkazi wake.

“Ndakhala ndikumudikira koma mpaka pano sakubwera. Ndanyamuka cha m’ma 9 koloko usiku kuti ndisake chigayo chomwe ali,” adatero mkuluyu.

Kunyumba wasiya mwana wa zaka 14 ndi wina wa zaka 9. Koma pachigayopo padalibe mkazi wake ndipo adatsetserekera ku chigayo china komwe adakamupeza.

Kachiza adapempha atsogoleri kuti athetse mavuto amene akunga Malawi. “Tivomereze zinthu sizili bwino m’dziko muno. Malawi waipa,” adatero Kachiza.

Nyakwawa Zakaliya idati anthuwa alibe kothawira chifukwa amayenera ayende mtunda wa makilomita 17 kuti akapeze chigayo cha dizilo.

Iye adati ali ndi mantha ndi anthu ake. “Kugona kuchigayo komanso kumayenda ndi usiku kusaka magetsi, ndi zachisoni, anthuwa atha kuchitidwa chipongwe komanso kunyumba kwawo akumasiya ana pamene makolo ali kuchigayo,” adatero Zakaliya.

Pamene timachoka pa chigayopo m’mama wa Lamulungu n’kuti magetsi asadayakebe ndipo akuti adayaka cha m’ma 5 madzulo a Lamulungu.

Mavutowa sadasiye malo, ku Ntcheu, Thyolo ndi Nkhata Bay, anthu akuti ayamba kumasinja pamanja pamene ena akuyenda mitunda yotalika kusaka chigayo cha dizilo.

“Tayamba kusinja pamanja kuno,” adatero mfumu Kabunduli ya m’boma la Nkhata Bay.

“Boma lisagawe pakati Escom. Izi ndi zomwe zikubweretsa mavutowa. Aleke Escom izipanga ndi kugulitsa yokha magetsi,” idaonjeza choncho mfumuyo.

Samuel Mugwa, mlimi wa ng’ombe za mkaka wa kwa Goliati m’boma la Thyolo, akuti akusowa kogulitsa mkaka chifukwa makampani ogula mkaka ayimika kaye chifukwa cha kuzimazima kwa magetsi.

“Poyamba ndimapanga K75 000 pa mwezi, patsiku ndimagulitsa malita 18. Pano bizinesi yasokonekera chifukwa asiya kutigula. Mkaka ukuwonongeka chifukwa cha magetsi,” adatero mkuluyu.  n

 

Avatar
Bobby Kabango
Previous Post

House of political prostitutes

Next Post

Making strides in child HIV prevention

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
Msiska: Our challenge remains dealing with the five percent

Making strides in child HIV prevention

Opinions and Columns

Big Man Wamkulu

Hot babe wants to trap me, should I ran?

April 18, 2021
Political Uncensored

Mighty mess!

April 18, 2021
My Thought

Chakwera’s indecisiveness will be his downfall

April 18, 2021
People’s Tribunal

Cut the crap, act on abuse forthwith

April 17, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Minister of Labour Ken Kandodo

    Ministry defends ‘borrowing’ of Covid-19 funds

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera bites

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chilima in public projects inspection

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • OPC frustrates roads projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Suspension without pay sparks debate

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.