Sunday, April 18, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Mapemphero a mvula aliko lero

by Staff Writer
09/01/2016
in Nkhani
1 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Pamene ng’amba yadzetsa chikaiko choti Amalawi akhoza kukolola zochepa chaka chino, mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika lero akhala nawo pa mapemphero a mvula amene achitike mumzinda wa Lilongwe.

Malinga ndi mlangizi wa Mutharika pa za chipembedzo Timothy Khoviwa, mapempherowo akhalanso othokoza Mulungu pa zochitika za chaka chatha.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

Mutharika led Malawians in prayer
Mutharika led Malawians in prayer

Mapempherowo akachitikira ku Bingu International Conference Centre (BICC) pansi pa mfundo yaikulu yakuti ‘Kudzipereka kwa Mulungu posinkhasinkha mtendere ndi chitukuko cha dziko’.

“Tikakhalanso tikupempha Mulungu kuti atipatse zokolola zokwanira mu 2016. Kuli atsogoleri a mipingo yosiyanasiyana. Iyinso ndi nthawi yakuti a zipembedzo zosiyanasiyana akhalire pamodzi,” adatero Khoviwa.

Mapempherowa akudza pomwe nthambi yoona za nyengo idati kudula kwa mvula kwa sabata ziwiri kwadzetsa chikaiko pakati pa alimi ndi Amalawi ena onse.

Mneneri wa nthambiyo Ellina Kululanga adati kudulaku kwadza chifukwa cha nyengo ya El Nino imene ikuchititsa kuti madera a m’chigawo cha kumwera mugwe ng’amba pomwe kumpoto ndi pakati chiyembekezo chilipo kuti mvulayi igwa bwino.

Malinga ndi kafukufuku wa nyuzipepala ya The Nation, madera ambiri mvula siyikugwa bwino zimene zingachititse kuti zokolola zichepe. Izi zikudza pomwe m’chaka cha 2015 zokolola zidatsika ndi makilogalamu 30 pa makilogalamu 100 alionse chifukwa cha vuto la madzi osefukira amene adakokolola mbewu zambiri.

Avatar
Staff Writer
Previous Post

The day I faced my spouse in the face to talk money

Next Post

Are our leaders clueless?

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post

Are our leaders clueless?

Opinions and Columns

Big Man Wamkulu

Hot babe wants to trap me, should I ran?

April 18, 2021
Political Uncensored

Mighty mess!

April 18, 2021
My Thought

Chakwera’s indecisiveness will be his downfall

April 18, 2021
People’s Tribunal

Cut the crap, act on abuse forthwith

April 17, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Lilongwe Road | The Nation Online

    OPC frustrates roads projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera, AG meet over MEC

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MPs in funds abuse go free

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Heartless plunder

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Traders fall short of Maize export demand

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.