Wednesday, January 27, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

MCP, UTM, PP ayamba kutsatsa manifesito

by Steven Pembamoyo
15/02/2019
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kupereka makalata ofuna kudzaimira m’chisankho chikudzachi ndiye kwatha, maso tsopano ali pazomwe zipani zasanja kufuna kutukula dziko lino.

Kuunguza kwa Tamvani kwapeza kuti mfundo zomwe zipani zasanja sizikusiyana kwambiri. Zipani za UTM, MCP ndi PP atsindika nkhani ya ntchito, ulimi, maphunziro ndi magetsi.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

mcp mec12 | The Nation Online
MCP akuti yamaliza kusanja manifesito ake

Chipani cholamula cha DPP chakana kuulula manifesito ake ati chifukwa nthawi ya kampeni sidakwane. Pamene olankhulira UDF nambala zawo sizimapezeka.

Mneneri wa MCP, Maurice Munthali adati manifesito a chipani chawo atuluka koma adakana kuti tiyione ponena kuti kukhala mwambo wobweretsa poyera manifesitoyo.

Komabe iye adati manifesito yawo alongedza mfundo monga zotukula ulimi ndi kukonza misika yodalirika ya mbewu, kuthetsa vuto la magetsi, kutukula maphunziro ndi kutsitsa chiwongola dzanja pa ngongole zomwe anthu amatenga ku banki.

“Mwachitsanzo, manifesto ikuti m’miyezi 6 yoyambirira, vuto lamagetsi lidzakhala litantha. Pakutha pa chaka, banja lilironse lizidzadya katatu patsiku,” adatero Munthali.

Mneneri wa chipani cha PP Ackson Kalaile Banda adati chipanicho chasanja zodzapeleka magetsi aulere m’midzi, kuwonjezera chiwerengero cha wogwira ntchito m’boma, kukhazikitsa sabuside yopindulira aliyense komanso kuwonjezera nyengo yomwe oyendetsa magalimoto amatenga kuti akakonzeso chiphaso chawo.

“Padakali pano, ogwira ntchito m’boma alipo 25 000 koma ife takonza zoti adzafike 40 000 kuti anthu ambiri makamaka achinyamata adzapeze ntchito. Zaka zisanu zomwe munthu amatenga kuti akakonzenso chiphaso choyendetsera galimoto zimachepaa koma ife tidzawonjezera.

“M’midzimu, tidzayikamo magetsi aulere kuti anthu akumudzi moyo wawo udzasinthe ndipo sabuside tidzathetsa zosankha anthu kuti aliyense yemwe akufuna kulima azidzapeza mwayi wa sabuside,” adatero Kalaile Banda.

Mneneri wa UTM Joseph Chidanti Malunga adati manifesito yachipani idatha kale koma chipani chikadasokerera mwina pomva maganizo a anthu ena ndipo chikuyika mlingo wa nthawi yodzakwaniritsira malonjezo ake.

Mwa mfundo zina, Malunga adati chipani cha UTM chizidzawonetsetsa kuti chikulemba ntchito achinyamata 1 miliyoni pa chak.

Chidzakonza nkhani za malimidwe ndi zamaphunziro pochotsa njira yosankhira ophunzira opita ku sukulu za ukachenjede.

“Ndipo zomwe tasanja m’manifesito athu zidzachitika, mboni adzakhala Amalawi,” adatero Malunga.

Koma kadaulo pa ndale Nandin Patel wati ngakhale zipani zili ndi ufulu obenthula za m’manifesito kapena ayi, ndibwino kufulumira kuuza anthu zomwe awakonzera chifukwa zimapereka mpata kwa anthu kuti afunse momwe sakumvetsa.

“Nthawi zambiri, manifesito imangonena zomwe chipani chidzachite chikadzapambana koma poti manifesito amatuluka mochedwa, anthu sakhala ndi mpata ofunsa momwe zipanizo zidzakwaniritsire mfundozo,” adatero Patel.

Iye waunikiranso kuti manifesito abwino amayenera kufotokoza nthawi yomwe mfundo zomwe zalonjezedwazo zidzakwaniritsidwe kuti anthu azidzatha kukwenya nthawi ikakwana koma mfundo osawoneka tsogolo lake.

Mneneri wa chipani cha DPP Nicholas Dausi adati chipani chake ndichosakonzeka kudziwitsa Amalawi zomwe chidzawachitire akapatsidwanso zaka zina zisanu.

Previous Post

Kamuzu Barrage upgrade complete

Next Post

Nyumba ya Malamulo yakhutira ndi MEC

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Alfandika: It will be submitted

Nyumba ya Malamulo yakhutira ndi MEC

Trending Stories

  • Mlusu presents the budget in this file photo

    Budget off rails

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • SA returnees in forced quarantine

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • New mashup draws mixed reactions

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Spread hope not fear

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Donors up game in Covid-19 fight

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

My Turn

When schools become inaccessible, a glimmer of hope in a coding boot-camp

January 27, 2021
My Turn

Behaviour change key in Covid-19 fight

January 25, 2021
Emily Mkamanga

Citizens power brings change

January 24, 2021
Search Within

The rural farmer needs to take centre stage

January 24, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.