Saturday, January 23, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

MEC igwira njakata pa zisankho zapadera

by Bobby Kabango
02/09/2016
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Zinthu sizikuyenda kubungwe loyendetsa zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) komwe tsogolo la zisankho zapadera silikudziwika.

Lachitatu lapitali, mkulu wa nthambi yoona za chuma kubungweli, Linda Kunje, adauza Tamvani kuti zisankho zachibwereza zichitikabe mtsogolo muno koma tsiku lenileni silikudziwika.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Mathanga: Tikudikirabe ndalama kuchokera kuboma
Mathanga: Tikudikirabe ndalama kuchokera kuboma

Posachedwa bungwe la MEC lidatulutsa chikalata chodziwitsa onse okhudzidwa ndi zisankhozi kuti ayamba aziimitsa kaye kaamba koti boma silidapereke ndalama zoyendetsera zisankhozi, zomwe zikuyembekezeka kuchitika ku Mchinji West Constituency, Kaliyeka Ward ku Lilongwe City South East Constituency, Sadzi Ward ku Zomba Central constituency, Bunda Ward ku Kasungu Central Constituency ndi Bembeke Ward ku Dedza South Constituency.

Mmodzi mwa makomishona kubungweli, Jean Mathanga, akuti pakufunika zosachepera K499 miliyoni zoyendetsera zisankhozi.

Mathanga adati boma silidawapatse ndalamazo koma adatsimikiza kuti zisankhozi zichitikabe mtsogolo muno.

Koma mneneri wa nthambi yoona za chuma kuboma, Nations Msowoya, watsindika kuti boma silipereka ndalama ku MEC pokhapokha lipoti lofotokoza za kusokonezeka kwa ndalama kubungweli litatulutsidwa.

Msowoya: Boma silipereka  msanga  ndalama
Msowoya: Boma silipereka
msanga ndalama

“Ife tidapempha kuti pakhale kafukufuku pa momwe ndalama zidayendera ndipo chomwe tikudikira ndi lipoti. Akatipatsa lipotilo, ndipo tikakhutitsidwa nalo tikhala okonzeka kupereka ndalamazo,” adatero Msowoya.

M’chaka cha 2012 mpaka 2014, kubungweli kudasowa ndalama zoposa K15 miliyoni. Kusowa kwa ndalamazi kudachititsa kuti akuluakulu ena kubungweli akakamizidwe kuti akapume kaye ndi cholinga choti afufuze bwino za mmene ndalama zosowazo zidayendera.

Pa 24 August chaka chino, MEC idatumiza akuluakuluwo, omwe ndi mkulu wa zisankho Willie Kalonga, komanso Harris Potani, George Khaki, Khumbo Phiri, Edington Chilapondwa, Chimwemwe Kamala, ndi Sydney Ndembe kuti abapuma kaye pomwe zofufuzazo zili mkati.

Zitachitika izi, mu August momwemo, boma lidalemba anamnadwa atatu, Rex Harawa, Stevenson Kamphasa ndi Duncan Tambala kuti achite kafukufuku pa kusokonekera kwa ndalamazo.

Koma izi zili chonchi, Kunje akuti zisankho zikhalapobe posakhalitsapa.

“Mitima ya anthu ikhale mmalo. Ngakhale sitingalonjeze tsiku lenileni lomwe zisankhozi zidzachitike, zichitika ndithu posakhalitsa,” adatero iye.

Si izi zokha, kumwaliranso kwa wapampando wa MEC, Maxon Mbendera, ndi komwe kukukayikitsa ngati bungweli lingapangitse zisankho posakhalitsa. Koma malinga ndi Kunje, ili si vuto.

Iye adati: “Palibe chovuta, kupanda iwo ndiye kuti ine ndidzaima kulengeza momwe chisankho chayendera.” n

Previous Post

Who will protect an ordinary Malawian?

Next Post

Akwiya ndi bungwe la MEC

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post

Akwiya ndi bungwe la MEC

Trending Stories

  • Not yet given retirement benefits: Mutharika

    Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • FAM ex-co approves women’s national league

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 initiative raises K18.3m in 2 days

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • India’s vaccine drive

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Legendary Patani Mwase remembered

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Bottom Up

Thanks Team Onjezani Kenani; our turn now

January 23, 2021
My Thought

Cloud hangs on Mtambo’s head

January 23, 2021
Off the Shelf

Goodbye Trump, you were a joke

January 23, 2021
Back Bencher

Chakwera’s ‘politics’ rant was in bad taste

January 23, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.