Wednesday, May 25, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

by Steven Pembamoyo
06/03/2021
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Thunthu loyamba la katemera wa Covid 19 lidafika mziko muno sabata ikuthayi ndipo malingana ndi mtsogoleri wa dziko lino Lazarus Chakwera, magulu oyambilira akhala akulandira katemerayo posachedwa.

Muuthenga wake Lamulungu lapitali, Chakwera adati majekeseni opelekera katemerayo adali kale m’dziko muno ndipo katemera weniweniyo amayembekezeka dzulo Lachisanu cha m’ma 4 koloko.

Mneneri wa unduna wa zaumoyo Joshua Malango Lachinayi adatsimikiza kuti katemerayo afika Lachisanu

Chakwera adati boma likuyesetsa kulimbana ndi matenda a Covid 19 kuti chiwerengero cha anthu opezeka ndi matendawo chiitsike kufika pa anthu 5 mwa 100 aliwonse kapenanso kutsikirapo.

Mkulu wa mgwirizano wa mabungwe a zaumoyo la Malawi Health Equity Network (Mhen) George Jobe adayamikira ganizo la katemerayo koma adati mpofunika kuchilimika kuphunzitsa anthu kuti adziwe zoona za katemerayo.

“N’zofunika kumakhala tcheru chonchi,  tathanako ndi miliri ina mmbuyomu ndi katemera koma chofunika n’kuphunzitsa anthu kuti amvetsetse za katemerayo apo ayi akhoza kuvuta kaperekedwe kake,” adatero Jobe.

Malingana ndi kalata yochokera kuunduna wa zaumoyo, ogwira ntchito zachipatala ndi magulu ena omwe ali ndi mavuto a zaumoyo m’matupi mwawo ndiwo adzayambe kulandira katemerayo.

“Monga tikudziwa zachiopsezo chomwe anzathu a zaumoyo ali nacho, katemera oyambilira adzalandira ndi iwowo limodzi ndi anthu omwe ali ndi mavuto azaumoyo mmatupi mwawo kuti atetezedwe,” idatero kalata yaundunawo.

Pakatipo kwakhala kukumveka manong’onong’o okhudza katemerayo koma unduna wazaumoyo udatsutsa manong’onong’owo ndi kupempha magulu osiyanasiyana monga mipingo kuti ithandize pophunzitsa anthu zaubwino wa katemerayo.

Kudzera m’mabungwe monga Malawi Interfaith Aids Association (MIAA) atsogoleri a mipingo akhala akukumana ndi kukambirana za gawo lomwe angatengepo pa nkhondo yolimbana ndi corona.

Wapampando wa bungwe la MIAA Gilford Matonga adati atsogoleri a mipingo ndi okonzeka tsopano kuphunzitsa anthu za katemerayo koma adati mpofunika kuti atsogoleri onse akhale ndi uthenga umodzi.

“Sizingaphule kanthu kuti mpingo uliwonse ukhale ndi uthenga wake wake  ayi, tikufunika tonse tinyamule uthenga umodzi ndi kuuza anthu zoona ndipo takonzeka kutero,” adatero Matonga.

Jobe adati mpofunika kusiyira ntchito yopanga mauthengawo akadaulo enieni odziwa za mankhwala kuti uthenga omwe uzipita kwa anthu ukhaledi ochokera pa nzeru zaukadaulo.

“Nkhaniyi kuti ithe bwino, boma lisiyile akadaulo odziwa za mankhwala mu unduna wa zaumoyo kuti ndiwo apange mauthenga ndi kufalitsa malingana ndi ukadaulo wawo. Boma lionetsetse kuti magulu ena ngati andale asakhale patsogolo ndi nkhaniyi,” adatero Jobe.

Iye adati Amalawi akuyenera kutenga katemerayu ngati momwe amatengera katemera wina aliyense akafika ndi kutsogoza chikhulupiliro kuti zonse ziyende bwino.

“Katemera sasiyana kwambiri ndi mankhwala. Mkati mothandizika, ena amatha kukumanabe ndi zovuta zina koma zimakhala zopepuka kusiyana ndi vuto lomwe athana nalolo. Tikufuna zimenezi anthu auzidwiretu ngati zilipo,” adatero Jobe.

Iye adati si bwino kulekelera munthu afe ndi nthenda yoti ili ndi katemera kotero nkofunika uthenga okwanira kuti anthu amvetsetse zowona zake za katemerayu ndi kumulandira ndi manja awiri.

Ngakhale izi zikuchitika, mayiko ena makamaka olemera akangalika kugula katemerayo kusonyeza kuti mmayikomo amuvomereza.

Posachedwapa, Pulezidenti wa dziko la South Africa Cyril Ramaphosa komanso nthumwi ya maiko aazungu (EU) Ivo Hoefkens adadzudzula maiko olemera omwe akugula mankhwala oposa omwe akufuna m’dziko mwawo ponena kuti apereka chiopsezo ku maiko osauka.

Previous Post

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

Next Post

Tabitha quits Chinese club

Related Posts

Nkhani

Agwidwa ndi yunifomu za polisi

May 22, 2022
Nkhani

Dollar yasowa

May 21, 2022
Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
Next Post
Tabitha (in yellow) in a previous match

Tabitha quits Chinese club

Opinions and Columns

People’s Tribunal

What was that press briefing all about?

May 22, 2022
Big Man Wamkulu

Wife, in-law plotting my downfall

May 22, 2022
My Thought

Tonse Alliance died on arrival

May 22, 2022
Layman's Reflection

New IMF programme pivotal moment for Tonse Alliance

May 21, 2022

Trending Stories

  • Kalindo: I am hearing it from you

    Kalindo earmarked for diplomatic post

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Musician Martse in hospital after fire accident

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Musicians, fans mourn Martse

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • APM under pressure

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Cooking oil project impresses Chilima

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.