Monday, March 1, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

‘Miyoyo ya Amalawi ili pachiopsezo’

by Nation Online
10/10/2015
in Chichewa
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 

Mkulu wa bungwe loona za umoyo la Malawi Health Equity Network (MHEN) Martha Kwataine wati nzomvetsa chisoni kuti dziko la Malawi lasemphanitsa zoyenera kuika patsogolo. Iye wati izi zaika miyoyo ya Amalawi ambiri pachiospezo.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

Amwalira atathawa m’chipatala

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Kwataine adanena izi kaamba ka ganizo la boma losiya kulemba ntchito madokotala 51 omwe amaliza maphunziro awo kusukulu ya ukachenjede ya College of Medicine ati popeza bomalo silikulembanso anthu ntchito.

Koma unduna wa zaumoyo wati wasintha maganizo ake ndipo tsopano ulemba ntchito madokotalawa ngakhale kumene kuchokere ndalama zowalipira sikukudziwika.

kwataine_martha

Polankhulana ndi Tamvani mkati mwa sabatayi, Kwataine adati n’zachisoni kuti boma lafika pokanika kulemba ntchito adotolo panthawi yomwe dziko lino likulira chifukwa chakuchepa kwa madotolo m’zipatala.

Iye adati n’zodabwitsa kuti boma lomwe lakhala likudandaula kuti madokotala akuthawa m’dziko muno kutsatira ntchino zonona kunja, pano likukana kuwalemba ntchito.

“Nanga akatithawa, kapena anthu akasiya kupita kusukulu ya udotolo, titani?” adadabwa Kwataine.

Iye adati n’zachisoni kuti ganizo la boma posalemba ntchito madotokotalawa kuika miyoyo ya Amalawi ambiri pachiospezo chifukwa madokotala alipo kale ochepa.

“Ndikulankhula pano zinthu sizili bwino m’zipatala zambiri momwe anthu akumwalira ndi matenda ochizika kaamba kakuchepa kwa madotolo,” Kwataine adatero.

Ndipo m’sabatayi madokotala onse m’dziko muno adaopseza kuti anyanyala ntchito ngati boma sililemba ntchito anzawowo pakutha pa sabata ziwiri.

Koma pozindikira kuti zinthu sizikhala bwino madokotalawo akanyanyala ntchito, unduna wa zaumoyo ndi a kuunduna wa zachuma adakhala pansi n’kugwirizana kuti madokotalawo alembedwe ntchito zisanafike poipa.

Mneneri wa unduna wa zaumoyo Adrian Chikumbe adatsimikiza za nkhaniyi Lachinayi polankhula ndi mtolankhani wa The Nation, koma adati undunawo sukudziwa kuti ndalama zolipira madokotala atsopanowo zichokera kuti.

Naye mneneri wa unduna wa zachuma Nations Msowoya adati ngakhale adagwirizana zoti madokotalawo ndi anamwino alembedwe ntchito, sakudziwa kuti malipiro awo azitenga kuti.

Malinga ndi kalata yomwe adatulutsa a bungwe la Medical Doctors Union of Malawi mogwirizana ndi bungwe la Society of Medical Doctors, kulemba ntchito adotolowa kuthandiza kuchepetsa kuperewera kwawo m’zipatala.

Kalatayo idati boma la Malawi liganizire za umoyo wa anthu m’dziko muno womwe ukufunika kuikidwa patsogolo ndipo zina zonse zibwere pambuyo.n

Mkulu wa bungwe loona za umoyo la Malawi Health Equity Network (MHEN) Martha Kwataine wati nzomvetsa chisoni kuti dziko la Malawi lasemphanitsa zoyenera kuika patsogolo. Iye wati izi zaika miyoyo ya Amalawi ambiri pachiospezo.

Kwataine adanena izi kaamba ka ganizo la boma losiya kulemba ntchito madokotala 51 omwe amaliza maphunziro awo kusukulu ya ukachenjede ya College of Medicine ati popeza bomalo silikulembanso anthu ntchito.

Koma unduna wa zaumoyo wati wasintha maganizo ake ndipo tsopano ulemba ntchito madokotalawa ngakhale kumene kuchokere ndalama zowalipira sikukudziwika.

Polankhulana ndi Tamvani mkati mwa sabatayi, Kwataine adati n’zachisoni kuti boma lafika pokanika kulemba ntchito adotolo panthawi yomwe dziko lino likulira chifukwa chakuchepa kwa madotolo m’zipatala.

Iye adati n’zodabwitsa kuti boma lomwe lakhala likudandaula kuti madokotala akuthawa m’dziko muno kutsatira ntchino zonona kunja, pano likukana kuwalemba ntchito.

“Nanga akatithawa, kapena anthu akasiya kupita kusukulu ya udotolo, titani?” adadabwa Kwataine.

Iye adati n’zachisoni kuti ganizo la boma posalemba ntchito madotokotalawa kuika miyoyo ya Amalawi ambiri pachiospezo chifukwa madokotala alipo kale ochepa.

“Ndikulankhula pano zinthu sizili bwino m’zipatala zambiri momwe anthu akumwalira ndi matenda ochizika kaamba kakuchepa kwa madotolo,” Kwataine adatero.

Ndipo m’sabatayi madokotala onse m’dziko muno adaopseza kuti anyanyala ntchito ngati boma sililemba ntchito anzawowo pakutha pa sabata ziwiri.

Koma pozindikira kuti zinthu sizikhala bwino madokotalawo akanyanyala ntchito, unduna wa zaumoyo ndi a kuunduna wa zachuma adakhala pansi n’kugwirizana kuti madokotalawo alembedwe ntchito zisanafike poipa.

Mneneri wa unduna wa zaumoyo Adrian Chikumbe adatsimikiza za nkhaniyi Lachinayi polankhula ndi mtolankhani wa The Nation, koma adati undunawo sukudziwa kuti ndalama zolipira madokotala atsopanowo zichokera kuti.

Naye mneneri wa unduna wa zachuma Nations Msowoya adati ngakhale adagwirizana zoti madokotalawo ndi anamwino alembedwe ntchito, sakudziwa kuti malipiro awo azitenga kuti.

Malinga ndi kalata yomwe adatulutsa a bungwe la Medical Doctors Union of Malawi mogwirizana ndi bungwe la Society of Medical Doctors, kulemba ntchito adotolowa kuthandiza kuchepetsa kuperewera kwawo m’zipatala.

Kalatayo idati boma la Malawi liganizire za umoyo wa anthu m’dziko muno womwe ukufunika kuikidwa patsogolo ndipo zina zonse zibwere pambuyo.n

Previous Post

Ntchito yasowa, wayamba ulimi wa kabichi

Next Post

Ulangizi wabala mwana ku Mulanje

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
death e1465557792659 | The Nation Online
Chichewa

Amwalira atathawa m’chipatala

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Next Post
farming1 | The Nation Online

Ulangizi wabala mwana ku Mulanje

Opinions and Columns

People’s Tribunal

Burglary at the hill

February 28, 2021
Search Within

Perseverance landed, is alive and well

February 28, 2021
Emily Mkamanga

Tasting your own salt in politics

February 28, 2021
People’s Tribunal

When blood of citizens is on head of leaders

February 28, 2021

Trending Stories

  • chisale1 | The Nation Online

    Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Grace Chinga makes posthumous return

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MIN coy on K18bn MZ youth centre

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • TUM insists strike continues

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Admarc secures K430bn to revamp operations

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.