Monday, January 18, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Msonda: Tsamba loyoyoka mu PP?

by Frank Namangale
17/09/2016
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Nthawi yomwe anthu akuchoka m’chipani cha Peoples Party (PP) chitangogwa m’boma, mneneri wa chipanichi, Ken Msonda, yemwe ali ndi lilime lakuthwa komanso amayankhula mokhadzula, amawayerekeza anzawowo ngati masamba ouma amenene akuyoyoka m’mitengo nthawi ya chilimwe.

Lero zagwa pamphuno.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Wachoka mu PP: Msonda
Wachoka mu PP: Msonda

Kodi pano Msonda nditsamba louma limene lathothoka m’chipani chakale cholamula kuti zichitire ubwino chipanichi?

Wogwirizira utsogoleri wa PP, Uladi Mussa akuti Msonda, ngati wina aliyense, ali ndi ufulu wochoka mu chipanichi.

Msonda akunenetsa kuti iye ndi katakwe pandale ndipo kuchoka kwake m’chipanichi sikutanthauza kuti ukatakwe wake pandale watha, ayi, koma akumvera zimene Mulungu wake akumuyankhula.

Iye dzana Lachinayi adalonjedza kuti auza mtundu wa Malawi zifukwa zochokera m’chipanichi ndi zomwe akulingalira kuchita pamoyo wake mtsogolomu pamsonkhano wa atolankhani mumzinda wa Blantyre, koma dzulo, iye adasintha thabwa ndi kuuza atolankhani kuti msonkhanowu walepheleka atamvera malangizo a mbusa wake.

“Abusa anga andiuza kuti ndisapangitse msonkhano wa atolankhaniwu. Akuti ndidekhe kaye mpakana nthawi yoyenerera yokhazikitsidwa ndi Mulungu itakwana.

“Ndikupempha anthu kuti andimvetsetse. Monga mmene ndanenera kale, ndikufuna kuzamisa moyo wanga wa uzimu komanso kukhala ndi nthawi yokwanira ndi banja langa,” Msonda adatero.

Mkuluyu adati adayankhulana ndi mtsogoleri wa chipani cha PP, Joyce Banda—amene ali kunja kwa dziko lino komwe akhala chigonjereni pazisankho za mu 2014—za kuchoka kwake.

Msonda adati Banda adamupempha kuti asachoke msanga kufikira iyo atabwerera ku Malawi, koma idati izi sizikadagwirizana ndi chikonzero chake chopempha Mulungu kuti amutsogolere pa za tsogolo lake mundale komanso muuzimu.

Iye adati zomwe amayankhulira anzake powayerekeza ngati masamba ouma amene akuthothoka mumtengo nthawi ya chilimwe zidali gawo la ntchito yake potumikira chipani.

“Ngati mmeneri wa chipani, ndimayenera kuyankhulira chipani komanso kupereka chithunzithunzi chabwino cha chipanichi kumtundu wa Malawi. Koma izi sizikusonyeza kuti ine ndi tsamba louma lomwe latha ntchito.

“Poti ndanena kuti ndikufuna ndizame muuzimu kaye, za ine akambe ndi anthu. Ndale ndazisiya kale apo, koma mtsogolomu mundiona ndikuzapanga nawo mpikisano pachisankho cha aphungu a ku Nyumba ya Malamulo mu 2019,” Msonda adatero.

Mkuluyu, yemwe wakhala akusintha zipani komaso amadziwika kwambiri ndi dzina loti ‘Foot Soldier’, akuti panthawi yoyenera adzauza anthu dongosolo limene akupempha Mulungu kuti amukonzere.

Msonda, yemwe lilime lake lamuikako m’mavuto potengeredwa kukhoti atamemeza anthu kuti azipha anthu amene amagonana amuna okhaokha kapena akazi okhaokha, adalowa mu chipani cha PP mu January 2012, chipanichi chisanalowe mboma koma mayi Banda ali wachiwiri kwa mtsogoleri wa dziko lino malemu Bingu Wa Mutharika.

Iye adasankhidwa kukhala mneneri wa PP ndipo udindowu udapitirira chipani cha PP chitalowa m’boma potsatira imfa ya Bingu wa Mutharika.

Msonda, yemwe adakhalakonso wothandizira mmeneri m’chipani cha UDF asadalowe PP, wakhala akusowetsa mmtendere chipani cholamula ndi kuyankhula kwake kokhadzula, ndipo kumayambiriro a chaka chino, adauzapo mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika kuti atule pansi udindo wake kaamba koti alephera kukonza vuto la zachuma ndi zina.

Izi anayankhula kumsonkhano wa anthu onse okhuzidwa wa Public Affairs Committee (PAC)mu mzinda wa Blantyre, ndipo kuyankhula uku kudakwiyitsa nduna zambiri zomwe zinkatenga nawo gawo kumsonkhanowu.

Chipani cha PP chakhala chikutaya atsogoleri ake ofunikira kwambiri kuphatizapo Sidik Mia, yemwe adatula pansi udindo wake ngati pulezidenti wothandizira m’chigawo cha kummwera chisankho za 2014 chitatsala pang’ono.

Ndipo chipanichi chitagwa pa zisankho za 2014, akuluakulu ena amene achoka m’chipanichi ndi Caeser Fatch, Stephen Mwenye, Tony Ngalande, Moses Kunkuyu ndi ena ambiri. n

Previous Post

Siteshoni ya Nkaya ifewetsa maulendo

Next Post

Gulewamkulu ndi mankhwala

Related Posts

Malango: Covid-19 ikadalipo
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Cultural dances such as these can provide a huge tourism attraction

Gulewamkulu ndi mankhwala

Trending Stories

  • Spending more: Chakwera

    Wasteful Chakwera

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Nocma in race against time

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Rot at Neef over loans

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Neef bosses, board fight in court

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse owes ‘ife tonse’ an apology

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
Political Uncensored

Maddening chaotic virus

January 17, 2021
Emily Mkamanga

Chakwera has to instill unity

January 17, 2021
People’s Tribunal

Perilous times and the need for accountability

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

WhatsApp us

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.