Saturday, April 17, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Mthirira usathere panjira

by ESMIE KOMWA
27/06/2020
in Chichewa
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kaitane Shuga wa m’mudzi mwa a Gavi ku Chileka m’boma la Blantyre ndi mmodzi mwa alimi amene amachita ulimi wothirira koma kusiyana ndi chaka chatha, iye akuti padakalipano zitsime zimene amapezapo madzi zayamba kuphwa.

Iye ali ndi nkhawa kuti mbewu zimene wabzala kachiwiri zikhonza kupserera zisadache kaamba kakusowa kwa madzi.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

“Padakalipano ndafukula kale zitsime zanga ndipo ndikumachita kudikirira kuti madzi abwerepo ndiyambe kuthirira pamene chaka chatha ndidalima kokwana katatu osakumana ndi vuto limeli kufikira madziwa adafika ndi nyengo ya mvula,” adadandaula motero.

Naye Eneless Timothy wa m’boma la Chikwawa akuti mtsinje umene iye pamodzi ndi alimi anzake a m’deralo amapatutsako madzi ndi kumathirira mbewu zawo achepa.

Irrigation on onions | The Nation Online
Sungani madzi othirira mbewu kuti mupindule ndi mthirira

Zotsatira zake, sakubwera ndi mphamvu choncho mbewu zimene zili kumtundako pang’ono sizikupeza madzi.

“Timagwiritsa ntchito makhwawa ndipo madzi akachepa amayenda mofooka. Izi zikupereka chiopsezo choti akhoza kuphwereratu,” iye adatero.

Malingana ndi katswiri wa zaulimi wothirira ku nthambi ya zakafukufuku wa za ulimi m’dziko muno Isaac Fandika, mvula ikagwa yocheperapo, malo osungira madzi amene amadziwika kuti water table m’Chingerezi amatsika.

Zotsatira zake, anthu makamaka alimi amene amachita ulimi wothirira amakanika kufikira madziwa koma iye adafotokoza kuti alimi akhoza kuchepetsa vutoli pochepetsa kagwiritsidwe ntchito kamadzi pothirira mbewu.

Katswiriyu adafotokoza kuti alimi akhoza kuchepetsa kagwiritsidwe ntchito ka madzi pophimbira mbewu, kuthirira mbewu madzi ocheperapo kapena kugwiritsa ntchito mthirira wosunga madzi wongodonthetsera pa mbewu umene umadziwika kuti drip irrigation pa chizungu.

“Mlimi akaphimbira mbewu ndi mapesi pamene akuchita ulimi wothirira, amathandiza kuti madzi asamauluke kuchoka m’nthaka kupita m’mwamba mwansanga. Zotsatira zake, amakhalitsa m’nthaka kwa nthawi yaitali choncho mlimi sathirira pafupipafupi.

“Izi zimathandiza kuti malo amene mlimi akupeza madzi othiririra mbewu zake mwachitsanzo pachitsime, padamu kapena mumtsinje akhalitse chifukwa amakhala ngati wasungako ena,” iye adatero.

Fandika adafotokoza kuti kuchepetsa madzi othirira mbewu ndi njira imene mlimi amadumpha makhwawa ena osawathirira ndipo ulendo wina n’kudzawathirira kwinako akudumpha makhwawa amene adathirira mmbuyomo koma osachepetsa zokolola.

Iye adati njirayi imathandiza kupulumutsa kapena kusunga madzi amene adakathiriridwa m’makhwawa kapena kuti m’makanalo enawo choncho zimamupatsa mlimi mwayi wogwiritsa ntchito madziwa kwa nthawi yaitali.

Fandika adati mthirira wongodonthetsera madzi pa mbewu ndiwodalirirka kwambiri pa nkhani yoteteza kutayika kwa madzi ku ulimiwu.

Malinganana ndi wachiwiri kwa mkulu woona za ulimi wothirira m’dziko muno Geoffrey Mwepa, mthirira wa mtunduwu umachepetsa kutaika kwa madzi ndi pafupifupi magawo 80 mwa 100 aliwonse.

“Izi zili chomwechi chifukwa mthirirawu umadonthetsera madzi okhawo ofunikira pa mbewu mosapyola muyeso komanso popanda kuthira malo osafunikira mwachitsanzo munda wonse,” adafotokoza motero.

Mphunzitsi wa ku nthambi ya zaulangizi ku Lilongwe University of Agriculture and Natural Resources (Luanar) Paul Fatch adaonjeza kuti kubzala mitengo kuzungulira malo amene mlimi amapezako madzi othiririra mbewu kumathandiza kuti malowa asaphwe msanga.

Iye adati izi zili chomwechi chifukwa imateteza madzi kuti asamauluke kwambiri kupita m’mwamba.

Avatar
ESMIE KOMWA
Previous Post

Covid-19 cases reach 1 005

Next Post

Council on Nam’s neck

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
queens | The Nation Online

Council on Nam’s neck

Opinions and Columns

Cut the Chaff

Tonse administration has bigger fish to fly

April 17, 2021
Off the Shelf

More fire on draining the swamp

April 17, 2021
Layman's Reflection

Govt should tighten financial management systems

April 17, 2021
Waiting for Godot

The country under State capture!

April 17, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Has over 25 cases to handle: Silungwe

    Chakwera, AG meet over MEC

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Heartless plunder

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt plans to relocate all refugees

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Made See needs help—Namadingo

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MPs in funds abuse go free

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.