Monday, April 19, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Mukufuna kulima chamba?

by Steven Pembamoyo
27/03/2021
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kwa nthawi yaitali, chamba chakhala chikulimidwa m’dziko muno mozembera malamulo. Komatu makono kwadza chamba chosazunguza bongo chimene akuchitama kuti chikhonza kutembenuza chuma cha dziko lino. Komatu ofuna kulima chamba cha mafakitalechi akonzeke kutulutsa kaye K7.6 miliyoni kuti apeze layisensi.

Unduna wa zamalimidwe wati makampani ndi magulu aalimi omwe akonzeka ndipo adula chiphaso cholimira mbewu ya chamba akhoza kuyamba kulima chaka chino.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

Industrial Hemp | The Nation Online
Mbewu ya chamba adaiyesera ku Chitedze Research Station

Koma mkulu wa bungwe la alimi la Farmers Union of Malawi (FUM) Frighton Njolomole wati K7.6 miliyoni n’chiletso kuti alimi aang’ono asachite nawo ulimiwu.

Iye adati alimiwo azingolionera phindulo likudutsa umooo! “N’zokomera makampani ndi makopaletivi okhazikika bwino chifukwa ndalamazo zizidutsa K7.6 miliyoni akaphatikiza zofunika zonse kuti alime n’kufika pogulitsa. Si ntchito ya masewera pakufunika mpamba,” watero Njolomole.

Nduna ya zamalimidwe Lobin Lowe idalengeza pa 20 November 2020 kuti nthambi yoyendetsa ulimiwu itaunika bwino idaona kuti chiphaso cholimira chamba chikhale K7.6 miliyoni ($10 000).

Koma malingana ndi ndondomeko za nthambi yoyendetsa ulimiwo, chiphaso chiziperekedwa kwa makampani ndi makopaletivi okhazikika okhaokha.

“Tizifuna umboni woti ndi kampani kapena kopaletivi yodziwika, ali ndi mpamba wokwanira, ali ndi malo okwanira komanso apeza kale msika,” ikutero ndondomekoyo.

Mneneri waunduna wa zamalimidwe Gracian Lungu wati undunawo udavonereza kale zoti ulimiwo uyambe chifukwa kafukufuku wake adatha ndipo ubwino wa mbewuyo udapezeka.

“Ubwino waulimiwu ndi woti boma lizipezapo msonkho, alimi azipha makwacha, anthu apeza ntchito mminda ndi mmakampani okhudza za chamba,” watero Lungu.

Iye watinso pali ndondomeko zomwe zakhazikitsidwa kuti anthu asapezelepo danga lolima chamba chozunguza bongo pobisalira m’chamba chovomerezekachi.

Ndipo alimi eni ake ati boma likadaganizira zokhwefula ndondomeko ya zofunika paulimiwo kuti nawonso apindule nawo paulimiwo.

“Akadakhwefula mtengo kuti nafe tizilima n’kumagulitsa ku makampani omwe azikagulitsa kunja ngati momwe momwe timapachitira ndi bale, kampopi ndi chikopa,” adatero Maliko Dziyende mlimi wa fodya kwa Nkhwazi ku Mchinji.

Wolakhulapo pa zochitika m’dziko Stanley Onjezani Kenani adaikira kumbuyo alimi kuti mtengo wachiphaso omwe boma lakhazikitsa n’chiletso kwa iwo.

“Nkhani ya ulimiwu ndi yabwino koma zomwe boma lapanga pamtengo wachiphaso zili ngati kupereka ndi dzanja ili n’kulandanso ndi dzanja linali chifukwa apapa alimi ang’onoang’ono palibe chawo,” adatero Kenani.

Malingana ndi unduna wazamalimidwe, makampani ndi makopaletivi oposa 100 adapereka kale kalata zokhumba kuchita nawo ulimiwu ndipo nthambi yoyendetsa ulimiwo ikuwaunika.

Lamulo lovomereza ulimi wa chamba lidakhazikitsidwa mdziko muno mmwezi wa February 2020 ndipo lidasainidwa ndi Pulezidenti Peter Muntharika (mu May 2020 yomweyo.

Nthambi ya zakafukufuku waulimi ya Chitedze Research Station idafufuza mbewuyi ulendo mvula zitatu nkuvomereza kuti ndiulimi wotheka komanso wofunika ku Malawi.

Avatar
Steven Pembamoyo
Previous Post

Justice in thin air

Next Post

Kaunda drops autobiography

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
Kaunda: It is my life story

Kaunda drops autobiography

Discussion about this post

Opinions and Columns

Big Man Wamkulu

Hot babe wants to trap me, should I ran?

April 18, 2021
Political Uncensored

Mighty mess!

April 18, 2021
My Thought

Chakwera’s indecisiveness will be his downfall

April 18, 2021
People’s Tribunal

Cut the crap, act on abuse forthwith

April 17, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Lilongwe Road | The Nation Online

    OPC frustrates roads projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Ministry defends ‘borrowing’ of Covid-19 funds

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chakwera bites

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Caroline Kautsire: English Professor at Bay State College in Boston

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chilima in public projects inspection

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.