Friday, March 5, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

‘Mundibwezere voti yanga’, amalawi athafulira APM pazionetsero

by Bobby Kabango
27/04/2018
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Amalawi athera Chichewa mtsogoleri wa dziko lino komanso nduna zake pa zionetsero zomwe zidachitika Lachisau.

Zionetserozo zidatsogoleredwa ndi amipingo, amabungwe komanso azipani amene amakakamiza boma kuti liyankhepo pa mavuto amene dziko lino likudutsamo.Demos Malawi6 | The Nation Online

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Mwa zina ndi kuuza mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika kuti athothe nduna ya zachuma Goodall Gondwe komanso ya maboma ang’ono Kondwani Nankhumwa pokhudzidwa ndi nkhani ya K4 biliyoni yomwe imagawidwa kwa aphungu 83 zisadasinthe kuti ziperekedwa kwa aphungu onse.

Amabungwewa akuda kukhosi ndi boma pankhani ya kuzimazima kwa magetsi chikhalirecho boma lidagula majeneleta kuti athane ndi kuzimazima kwa magetsiwo.Demos Malawi3 | The Nation Online

Patsikulo, mizinda ya Blantyre, Lilongwe, Zomba ndi Mzuzu komanso maboma monga Rumphi kudawirira pamene anthu adayenda kukapereka madandaulo awo kwa akuluakulu a boma.

Mwa zina, anthu adagwiritsa ntchito nyimbo popereka uthenga ku boma. Mwa nyimbo zina ndi monga: Tichotse nkhalamba ndi mtima umodzi. Bewu—bewula Peter, bewula Chaponda, bewula Goodall. Mukamva hi! Ho! agogo athawa, M’manja mwako mlamu tachokamo, undibwezere mavoti anga mlamu mwazina.

Ku Mzuzu, nyimbo idazunguza idali yolimbana ndi nduna zomwe zatopa ndi ukalamba m’boma.

“Mukutani m’boma, pitani muzikacheza ndi adzukulu kumudzi,” idatero.Demos Malawi1 | The Nation Online

Kupatula nyimbo, anthuwo adagwiritsiranso ntchito zikwangwani zomwe mudalembedwa mauthenga osiyanasiyana.

Mwa mauthengawo adali monga; Ngolongoliwa, Kyungu, Lukwa ndi Lundu si mafumu koma ogwira ntchito a chipani cha DPP.

Uthenga wina udalunga ku wailesi ya boma ya MBC. “Sumbuleta ndi Phillip Business, MBC si nyumba ya abambo anu.”

Uthenga wina umanena Gondwe: “Adada Goodall taweya mwachekula, lutani kukaya mukachezgenge nawazukulu [bambo Goodall mwakula, pitani kumudzi mudzikacheza ndi zidzukulu].”

Zina zimafunsa nkhani ya K4 biliyoni. “Kulubwalubwa ndi K4 biliyoni yathu?”

Mmodzi mwa akuluakulu amabungwe amene amatsogolera zionetserozi Gift Trapence wa bungwe la Centre for the Development of people (Cedep) adati zionetserozo zidachitika bwino.

“Ganizo lathu lakwaniritsidwa, tapereza madandaulo athu ku boma ndipo tikuwapatsa masiku 30 kuti atiyankhe ndipo akalephera kupitanso ku msewu,” adatero Trapence.  

Steven Pembamoyo, Martha Chirambo adathandizira pa nkhaniyi

Previous Post

Electricity back at Bingu Stadium after 7 months

Next Post

Amalawi alankhula: Masiku 30, boma liyankhe—Gift Trapence

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Next Post
Demos Malawi6 | The Nation Online

Amalawi alankhula: Masiku 30, boma liyankhe—Gift Trapence

Opinions and Columns

In pursuit of development

The future of aid

March 4, 2021
Business Unpacked

Take time to know your pension’s worth

March 4, 2021
Rise and Shine

How do successful people think?

March 4, 2021
My Turn

Unmasking Covid-19 vaccine

March 3, 2021

Trending Stories

  • Under probe: The Reserve Bank building in Mzuzu

    Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Minister wants Msundwe police officers prosecuted

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Charcoal traffickers fined K800 000, vehicle forfeited

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt to finance 15 major projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Macra to introduce fees for phone numbers

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.