Friday, March 5, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Mutharika apempha bata

by Kondwani Kamiyala
31/05/2019
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Peter Mutharika, yemwe adapambana pa chisankho cha pa 21 May, dzulo adapempha Amalawi kuti apite patsogolo ndi kukhala wogwirizana ndi a mtendere potukula dziko lino.

Polankhula dzulo ku Kamuzu Stadium mumzinda wa Blantyre pamwambo wolandira ulemerero wa dziko lino kuchokera kwa asilikali, Mutharika adati Amalawi ayenera kuyanjana potukula dziko lino.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

MUTHARIKA | The Nation Online
Mutharika kuonetsa lupanga la ulemerero pamwambowo

“Tonse tiyenera kudekha ndi kuthana ndi umphawi. Amalawi alankhula ndipo zofuna zawo zikwaniritsidwe. Icho chitiluzanitsa chiposa icho chitisemphanitsa. Ndine mtsogoleri wa Amalawi onse, kaya adandivotera kaya sanandivotere,” adatero Mutharika pamwambo umene padafika khwimbi la anthu.

Iye adapempha a mipingo ngakhalenso ogwira ntchito m’boma kuti apewe kulowerera pandale.

Ndipo polankhulapo za zipolowe zimene zidadza ndi otsatira chipani cha MCP ena amene adakwiya ndi kusankhidwa kwa Mutharika, mtsogoleri wa dziko linoyo adapempha otsatira chipani chake cha DPP kuti asabwenzere.

“N’zachisoni kuti amayi ena otsatira DPP amenyedwa ndi kuvulidwa koma palibe mabungwe a za amayi amene alankhulapo kanthu chifukwa amayiwo ndi a DPP. Chonde osabwenzera choipa,” adatero Mutharika.

Pamwambowo, padafika nduna yaikulu ya dziko la Tanzania, Kassim Majaliwa, komanso nduna zoimirira maiko a Zambia, Zimbabwe ndi Mozambique  komanso oimira bungwe la mgwirizano wa maiko la African Union.

Mtsogoleri wakale wa dziko lino Bakili Muluzi, yemwe adali nawo pamwambowo komanso pomwe Mutharika amamulumbiritsa Lachiwiri, adati Amalawi ayenera kuyanjana.

“Ndikuwafunira zabwino a Mutharika. Tonse tiyenera kusangalala komanso kugwirizana potukula dziko lathu,” adatero Muluzi.

Mutharika  ndi womutsatira Everton Chimulirenji adapeza ma voti oposa 1.9 miliyoni pomwe omutsatira wake, Lazarus Chakwera wa MCP ndi womutsatrira wake Sidik Mia adapeza mavoti 1.7 miliyoni.

Iyi ndi ndime yachiwiri komanso yomaliza ya Mutharika kulamulira dziko lino.

Previous Post

Committee urges institutions to champion integrity

Next Post

Atibera—Chakwera

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Next Post
Chakwera: Tikupita kukhoti

Atibera—Chakwera

Opinions and Columns

In pursuit of development

The future of aid

March 4, 2021
Business Unpacked

Take time to know your pension’s worth

March 4, 2021
Rise and Shine

How do successful people think?

March 4, 2021
My Turn

Unmasking Covid-19 vaccine

March 3, 2021

Trending Stories

  • Under probe: The Reserve Bank building in Mzuzu

    Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Minister wants Msundwe police officers prosecuted

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Charcoal traffickers fined K800 000, vehicle forfeited

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt to finance 15 major projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Macra to introduce fees for phone numbers

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.