Monday, March 1, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Mwambo woika maliro a khanda lozizira

by Bobby Kabango
11/09/2015
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Amalawi ngakhale ali ndi miyambo yosiyanasiyana malinga ndi mitundu yawo monga Achewa, Angoni, Atumbuka, Alhomwe, Amang’anga, Asena kaya ndi Ayao, koma pamwambo woika khanda lopitirira zochitika zimakhala zofanana. DAILES BANDA adacheza ndi mayi Catherine Ligowe kuti afotokoze mmene mwambo woika khanda lozizira umayendera. Adacheza motere:Grave_commonwealth

Ndikudziweni mayi wanga.

RelatedHeadlines

Mtsutso pa zoika a Covid-19

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Ndine Catherine Ligowe. Ndidabadwa zaka zambiri zapitazo. Ndimachokera ku Ntcheu m’mudzi mwa Chikadya, T/A Ganya. Ndili ndi ana asanu ndi awiri. Ndinenso namkungwi kumudzi kwathu komanso ndidali mzamba.

 

Kuno ku Mzuzu mukupezekako bwanji?

Mavuto mwanawe. Kuyeseyesa kuti tipezeko koponyako mkamwamu.

 

Ku Mzuzu kunonso ndinu namkungwi?

Ayi, ku Mzuzu kuno unamkungwi wanga umakhala wa m’makwalalamu koma kumudzi ndi komwe ndimagwira ntchitoyi kuchinamwali, tere chaka chomwechi ndidali komweko.

 

Mutiuzeko pang’ono za maliro akhanda lopitirira

Inu mufuna mudziwe chani?

Tiyambe ndi mwambo wa maliro mmene umakhalira.

Khanda lopitirira limatchedwa kuti khanda lozizira chifukwa mayi a khanda lija amakhala kuti sadakhale kaye pamodzi ndi mwamuna.

 

Mukutanthauza kuti khanda litamwalira pamiyezi iwiri makolo ake asadakhalire malo amodzi mwambo wake umakhala ngati wa khanda lopitilira?

Eya, chifukwa timakhulupirira kuti mwanayo sadatenthetsedwe ndi bambo ake.

 

Zimayenda bwanji?

Mwana uja akamwalira amakaikidwa ndi azimayi okhaokha koma azimayi aja saloledwa kulira malirowo chifukwa kulira kuja kumachititsa kuti mayi uja asadzaberekenso. Manda a malirowa sakhala akuya ngati a maliro a munthu wamkulu.

Chifukwa chiyani sakhala akuya?

Kalekalelo makolo athu ankakhulupirira kuti manda a khanda lozizira akakhala akuya kwambiri mayi wa khandalo sadzaberekanso.

Ndiye maliro a mapasa mumachita bwanji?

Akamwalira mmodzi mwa ana amapasa azimayi akalira malirowa timakhulupirira kuti mwana wotsala uja amamwaliranso, komanso tikamaika malirowa timaika khanda lomwaliralo ndi mvunguti pambali pake kuti mzimu wake uziona ngati akadali ndi mnzake uja.

Nanga wotsalayo mumatani naye?

Ameneyo timamusambitsa mumankhwala kuti mzimu wa mnzake uja usamamubwerere.

 

Tsopano inu mumati mudali mzamba, mudabadwitsako mwana wopitirira?

Ayi, palibe mwana wopitirira amene ndidabadwitsako.

 

Mudasiyiranji ntchitoyi?

Boma lidaletsa komanso anthu amene amabereketsa azimayi amafa maso n’chifukwa chake anamwino ambiri ochiritsa azimayi kuchipatala amakhala ovala magalasi. Kalekalelo mzamba asadayambe kugwira ntchito amayamba kaye wasamba mankhwala kuti adziteteze ku ukhungu.

 

Chimachititsa kufa masoko ndi chiyani?

Chimachitika ndi chakuti azimayi akamabereka amachita zinthu zodabwitsa zambiri ndiye ukaona zinthu zimenezo kwanthawi yaitali maso aja amafa, umangoona zinthu mwa mbuu.

 

Zikomo kwambiri chifukwa cha nthawi yanu.

Zikomo.

Previous Post

Panazale samakololapo!

Next Post

Government calls for investment in solar powered irrigation

Related Posts

covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Next Post
Irrigation ntchisi | The Nation Online

Government calls for investment in solar powered irrigation

Opinions and Columns

People’s Tribunal

Burglary at the hill

February 28, 2021
Search Within

Perseverance landed, is alive and well

February 28, 2021
Emily Mkamanga

Tasting your own salt in politics

February 28, 2021
People’s Tribunal

When blood of citizens is on head of leaders

February 28, 2021

Trending Stories

  • chisale1 | The Nation Online

    Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Grace Chinga makes posthumous return

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MIN coy on K18bn MZ youth centre

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • TUM insists strike continues

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Admarc secures K430bn to revamp operations

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.