Saturday, March 6, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Nanawa: Mlowam’malo wa kupitakufa

by Bobby Kabango
10/10/2015
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 

Matenda a HIV/Edzi asokoneza miyambo ina monga mwambo wa kupitakufa, womwe umapereka mphamvu kwa ‘fisi’ kuti akakonze maliro pocheza ndi namfedwa kwa sabata ziwiri ndipo machezawo amachitika katatu patsiku. Chifukwa cha matendawa, kwabwera njira ya nanawa yomwe yazilalitsa mwambo wa kupitakufawu. BOBBY KABANGO adali m’boma la Nsanje komwe adacheza ndi mlembi wa nyakwawa Masanzo kwa T/A Mlolo.

RelatedHeadlines

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

Mtsutso pa zoika a Covid-19

Kodi amfumu tawapeza?

Ayi, iwowa adzukirira kudimba. Akuyembekezereka kubwerako madzulo chifukwa ntchito yakula kumeneko.

 

Tidalire kuti inu mutithandiza pa vuto lathu?

Musakaikenso, ndine mlembi wa amfumuwo ndiye palibe chomwe sindikuchidziwa chokhudza mudzi uno ndi miyambo yomwe timatsata.

Mkaka: Mwambo wa nanawa timangomwa  mankhwala othamangitsa imfa
Mkaka: Mwambo wa nanawa timangomwa
mankhwala othamangitsa imfa

Kodi mwambo wa kupitakufa ukuchitikabe kuno?

Zikuchitika koma mobisa chifukwa momwe matenda a Edzi aopseramu sungayerekeze kumachitabe mwambowu. Amabungwe akhala akufika kumemeza anthu kuti miyambo yoipa, monga umenewu, itheretu ndipo zipatso zake zikuonekadi pano.

 

Ndiye mukutani kuti imfa ithawe pakhomo?

Timagwiritsa mankhwala a ‘nanawa’ amene amathamangitsa imfa pakhomo. Kuno anthu ambiri tikutsata zimenezi.

 

Nanawa n’chiyani?

Ndi mankhwala amene sing’anga amachita pakhomo pamene pagwa maliro. Anthu, maka achibale, amamwa mankhwalawo molandirana ndipo pakhomopo pamakhala bwino.

 

Zimachitika nthawi yanji?

Maliro akachitika monga lero, mawa timakaika ndiye timasweretsa tsiku limodzi pamene timasonkhana kudzasesa. Nthawi yosesa mpamene mwambo wa nanawa umachitika. Mungathe kuchita mwambowu nthawi iliyonse kaya ndi masana kapena madzulo.

 

Kodi mankhwalawa mumatemera kapena mumadya?

Mankhwalawa ali pawiri. Ena amakhala a madzi. Amawaika m’kapu ndiye aliyense wachibale amalandirana mankhwalawo kumamwa pang’ono mpaka nonse achibale akukwaneni. Pamene mankhwala ena amawaika kudenga kwa nyumba yomwe mumagona malemuwo. Mumawasomeka kudenga mbali yomwe kuli khomo kuti anthu akamalowa m’nyumbamo azigwira mankhwalawo.

 

Mukutanthauza wachibale aliyense amayenera amwe mankhwalawo?

Zimatero kumene. Nonse mumalandirana, kumwa pang’ono basi, aliyense kamodzi komanso momapatsirana.

Nanga achibale amene sadafike pamwambowo mumawatani?

Achibale amene nthawi ya malirowo kapena tsiku la kusesalo palibepo, timawasungira mankhwalawo. Mankhwala ake ndi amene tawasomeka kudenga aja. Tsiku lomwe akonza zodzafika pakhomopo, timawalandira ndi kuwatengera kunyumba yomwe kudachitika malirowo. Ndiye pamene tikulowa m’nyumbayo, timawapatsa mankhwala aja kuti agwire. Akangotero basi amabwezeretsa mankhwalawo kudengako.

 

Amachitanso china chiti?

Palibe, ngati agwira mankhwalawo ndiye kuti nawonso akonzedwa ku imfa yomwe idakangogwa pakhomopo.

 

Nthawi yomwe munkatsata mwambo wa kupitakufa zinkakhala bwanji?

Maliro akachitika chonchi, timapeza fisi kuti apite kunyumba yomwe kwachitika malirowo akacheze ndi namfedwayo. Katatu patsiku kapena zikavuta atha kumacheza nawo kawiri patsiku kwa sabata ziwiri. Fisiyu ntchito yake idali yoti achotse mzimu wa imfa womwe wakuta pakhomopo.

 

Mpaka katatu? Ndiye zidalikolikotu…

Hahaha! Eeh, amasangalala kwambiri koma pano zimenezi zidatha.

 

Nanga akamwalira wamkazi, afisi aakazinso amapezeka?

Ayi, zikatere ndiye tinkapanga mankhwalawa kapena apo ayi mupemphe banja lina kuti likupitireni kufako.

Previous Post

Commercial farming is way to go

Next Post

Then there was Vision 2020

Related Posts

Blantyre’s ‘best building’: St Michael and All Angels Church
Nkhani

Mipingo yakonzeka zophunzitsa anthu za katemera wa Covid 19

March 6, 2021
People queue to buy maize at Admarc market
Nkhani

Boma ligulitsa chimanga pamtengo wa sabuside

March 6, 2021
covid death | The Nation Online
Nkhani

Mtsutso pa zoika a Covid-19

February 28, 2021
Next Post
Named in the report: Muluzi

Then there was Vision 2020

Opinions and Columns

My Diary

Musowa voice missing yet needed

March 6, 2021
Off the Shelf

Off the Shelf 5 years on

March 6, 2021
Back Bencher

Let the teachers have their Covid-19 risk allowances

March 6, 2021
Guest Spot

Ensuring quality education for Malawian girls

March 6, 2021

Trending Stories

  • Lowe: We are trying to find potential markets

    Ministry plans to export 1m tonnes surplus maize

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt to finance 15 major projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • SKC ‘intervenes’ on youths’ demos

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Exclusive: RBM’s Mzuzu branch payment mess exposed

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 vaccine in today

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.