Friday, April 23, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Njovu ziwiri zitengetsana pa 19 May

by Steven Pembamoyo
13/03/2020
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Zadziwika tsopano kuti njovu ziwiri zomwe ndi mgwirizano wa Democratic Progressive Party (DPP) ndi United Democratic Front (UDF) komanso Malawi Congress Party (MCP) ndi UTM Party ndizo zidzalimbane pachisankho cha pa 19 May.

Izi, zidatsimikizika Lachitatu zipani za MCP ndi UTM zitabwera poyera n’kunena kuti m’gwirizano wawo womwe wakhala mphekesera chabe kwa nthawi yaitali tsopano watheka.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

chilima bingu | The Nation Online

Izi zikutanthauza kuti tsopano zipani zinayi zomwe zidali zikuluzikulu pachisankho cha pa 21 May chaka chatha tsopano zapanga mbali ziwiri zomwe zidzapikisane pachisankho chomwe chikubwerachi.

Zipani za DPP ndi UDF zidalengeza mgwirizano wawo pa 25 February pomwe MCP ndi UTM ati mgwirizano wawo wangopsa kumene ndipo adzasainira pa 19 March ku Bingu International Convention Centre (BICC) ku Lilongwe.

Polengeza mgwirizano wawo, DPP ndi UDF onse adati adaona kuti mfundo zawo zachitukuko ndi zolinga zawo n’zofanana ndipo MCP ndi UTM nawo akunena zomwezo.

Migwirizanoyi yapangidwa pokonzekera chisankho cha mtsogoleri wa dziko lino chobwereza potsatira chigamulo cha Constitutional Court choti chisankho cha pa 21 May sichidayende bwino ndipo chibwerezedwe.

Khothilo lidagamula kuti chisankhocho chichitike m’masiku 150 kuchokera pa 3 February 2020 pomwe lidapereka chigamulo chake chomwe chidakomera Lazarus Chakwera wa MCP ndi Saulos Chilima wa UTM Party.

Awiriwa adakamang’ala kukhoti kuti bungwe loyendetsa chisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) lidapotoza zotsatira zachisankhocho chomwe lidapambanitsa Peter Mutharika wa DPP.

Koma zokonzekera chisankhocho ziyembekeza kuti mtsogoleri wa dziko lino Peter Mutharika asainire mabilo a zachisankho amene aphungu a Nyumba ya Malamulo adapereka kwa iye.

Mwa zina, mabilowo akuti chisankho cha aphungu ndi makhansala chotsatira chidzachitike mu 2025 kuti chidzalingane ndi cha mtsogoleri wa dziko lino.

Aphunguwo adapemphanso Mutharika kuti achotse makomishona a MEC amene bwalo lidawapeza kuti sadayendetse bwino chisankho cha pa 21 May chaka chatha.

Oimira ufulu wa anthu Timothy Mtambo, Gift Trapence ndi MacDonald Sembereka adamangidwa pokonza zionetsero zokakamiza Mutharika kuchotsa makomishonawo.

Wotambasula za ndale Humphreys Mvula wati polingalira za nthawi yomwe yatsala kuti chisankho chichitike, n’koyenera kuti Pulezidenti asadikire masiku 21 kuti asayinire mabiluwo. “N’zoona malamulowo akutero koma apapa tikuyang’ana nthawi yomwe ilipo kuti chisankho chichitike,” adatero iye.

Avatar
Steven Pembamoyo
Previous Post

Chisankho chipitirire—bwalo

Next Post

Activism in Malawi

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post

Activism in Malawi

Opinions and Columns

My Turn

They couldn’t breathe

April 23, 2021
My Turn

Controlling bladder cancer

April 23, 2021
Business Unpacked

Tobacco indeed a dying industry, but

April 22, 2021
Rise and Shine

What bosses hate the most

April 22, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • chilima 3 | The Nation Online

    Tonse cracks widen

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MLS dares judges

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • DPP loses fifth parliamentary seat

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Rwandan exiles pen govt

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Sumbuleta faces 6 counts

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.