Thursday, January 21, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result

Nkhanza zanyanya

by Martha Chirambo
29/11/2020
in Uncategorized
4 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Bambo wina wa zaka 31, walaula dziko pomwe akumunazira kugwiririra khanda lalikazi la miyezi 5. Pakadali pano Muderanji Kanjira ali m’manja mwa apolisi.

Nkhaniyitu idatuluka Lachitatu pa 25 November pomwe anthu adali pa kalikiliki ndi zochitika zoyamba  masiku 16 olimbana ndi nkhanza za m’banja.

RelatedHeadlines

Food imports doubled in 20 years—report

Malawi loses 5% of GDP on donor withdrawal

Inequality within and poverty reduction

Malinga ndi mneneri wa polisi ya Zomba Patricia Sipiliano, Kanjira adapempha makolo a khandalo kuti akacheze nalo chifukwa ngoyandikana nyumba.

chichewa | The Nation Online
Mbuyomu, atolankhani aakazi adachita zionetsero zokwiya ndi kugwiririra

“Patadutsa ola limodzi adakalibwenza khandalo koma likulira kwambiri ndipo mayi ake pomusintha adaona magazi pa zovala zake komanso mabala kumalo ake obisika,” adalongosola Sipiliano.

Iye adati ngakhale zotsatira zochokera kuchipatala chachikulu cha Zomba zatsimikiza kuti khandalo lidagwiriridwa.

Kanjira amachokera m’mudzi mwa Mtiya,  kwa T/A Mlumbe m’boma la Zomba.

Ndipo kumapeto a sabata yatha, kudatuluka uthenga wa mwana wina ku Chigumula amene adatepa bamboo ake pomwe amamunyengerera kuti akagone nawo. Bamboyo amakakamira mwanayo kuti akagone naye posinthanitsa ndi fizi.

Malinga ndi zomwe mwanayu watumiza m’masamba a mchezo, bamboyo yemwe sakudziwika bwino dzina lake akumveka akumuuza mwanayo kuti akavulire zonse pabalaza ndipo akalowe kuchipinda kwa bamboyo ali maliseche ngati chibalo chokana kugona naye mmbuyomu.

“Ndidaganiza zowajambula palamya akukamba zawozo chifukwa nthawi zambiri n’kamadandaula anthu amandinena kuti ndine wabodza,” adatero mtsikanayo.

Izi zili apo, m’boma la Dowa, apolisi atsekera mnyamata wina wa zaka 21 yemwe adagwiririra ana amuna anayi a zaka kuyambira 10 mpaka 17 ndi kuwapatsanso matenda opatsirana pogonana.

Malinga ndi mneneri wa apolisi m’boma la Dowa, Gladson M’bumpha, Innocent Poita akuganiziridwa kuti wakhala akugwiririra anawa kuchoka m’chaka cha 2016 kufika pa 19 November chaka chino m’mudzi wina ku Dowako.

“Anyamatawa amapita kunyumba kwake kukaonera kanema pa lamya yake ya m’manja.  Ndipo pa 19, atamaliza kuonera kanemayo, mmodzi mwa anyamatawo adatsalira kunyumbako zomwe zidapangitsa anzakewo kukaulula kwa makolo ake kuti Poita amawagona akakhala kunyumba kwake,” adalongosola M’bumpha.

Poti amachokera m’mudzi mwa Ndalama kwa T/A Chiwere, m’boma la Dowa.

N’zodandaulitsa kuti pomwe mbali zina zili pa likiliki kuyesetsa kuthana ndi mchitidwe wogwiririra zinthu zikunka zikipiratu.

M’chaka cha 2018, apolisi adapeza kuti ana 1 539 ndiwo adagwiriridwa, pomwe m’chaka cha 2019 anthu 1 766 adagwiriridwa ndipo kuchoka January chaka chino kufika mwezi wa September ana 1 501 adagwiriridwa.

Izi zikutanthauza kuti  pofika mwezi wa mawa wa December chiwerengerochi chikhala chitadutsa chiwerengero cha chaka chatha cha 1 766.

Komatu si ana okha omwe akukumana ndi nkhanza m’dziko muno chifukwa ngakhale nawo atsikana komanso amayi akukumana nazo.

Pomwe Msangulutso udacheza ndi amayi ena omwe amagwira ntchito yoyendayenda mumzinda wa Mzuzu, zidaululikanso kuti amayiwa amagwiriridwa makamaka ndi abambo ogwira ntchito za chitetezo monga apolisi ndi asilikali.

Mmodzi mwa amayiwa yemwe sitimutchula dzina pomuteteza adati ambiri mwa abambo azachitetezowa amawagona ulele powaopseza komanso akamaliza pamenepo amawamenya.

“Sabata yomwe ino, bambo wina wa chitetezo adandigona mondikakamiza komanso sadagwiritse ntchito chitetezo. Atatha pamenepo adandimenya komanso kunditengera zakudya ndi zakumwa zomwe ndidali nazo,” iye adalongosola.

Polankhulapo pa nkhanza zomwe zikuchitikira amayi, atsikana ndi ana a m’dziko muno, Jessie Ching’oma wochokera ku bungwe lomwe si laboma la NGO Gender Coordinating Network (NGO-GCN) adati anthuwa akufunika zilango zokhwimitsitsa, zoopsa kuti ena atengerepo phunziro.

“Anthuwa akufunika zilango zomwe sizidalembedwe, zilango zoopsa kuti mwina mchitidwewo uchepeko,” adalongosola Ching’oma.

Pomwe Amos Nyaka yemwe amamenyeranso ufulu adauza msonkhano wa achinyamata mumzinda wa Mzuzu kuti mpofunika kuunikanso zina mwa zikhalidwe zathu chifukwa ndi zomwe zikupititsa patsogolo mchitidwewu.

Previous Post

FDH supports FIMDA Lakeshore Conference

Next Post

Tidakumana ku BICC

Related Posts

Malawi has been importing maize over the years largely due to floods that have impacted output
Business News

Food imports doubled in 20 years—report

January 21, 2021
Mlusu: The budget is skewed
Business News

Malawi loses 5% of GDP on donor withdrawal

January 21, 2021
Poverty levels in Malawi remain high
Business News

Inequality within and poverty reduction

January 21, 2021
Next Post
Mwale ndi Kadzakumanja lero ndi banja | The Nation Online

Tidakumana ku BICC

Discussion about this post

Trending Stories

  • Escaped South African bail: Bushiris

    Bushiri says not seeking political intervention

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi closes in on hefty US deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Vendors back on streets amid Covid-19 surge

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 initiative raises K18.3m in 2 days

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Business Unpacked

Towards Malawi2063, lessons from Vision 2020

January 20, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 20, 2021
In pursuit of development

India’s vaccine drive

January 20, 2021
My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.