Saturday, May 21, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result

Nkhanza zanyanya

by Martha Chirambo
29/11/2020
in Uncategorized
4 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Bambo wina wa zaka 31, walaula dziko pomwe akumunazira kugwiririra khanda lalikazi la miyezi 5. Pakadali pano Muderanji Kanjira ali m’manja mwa apolisi.

Nkhaniyitu idatuluka Lachitatu pa 25 November pomwe anthu adali pa kalikiliki ndi zochitika zoyamba  masiku 16 olimbana ndi nkhanza za m’banja.

Malinga ndi mneneri wa polisi ya Zomba Patricia Sipiliano, Kanjira adapempha makolo a khandalo kuti akacheze nalo chifukwa ngoyandikana nyumba.

Mbuyomu, atolankhani aakazi adachita zionetsero zokwiya ndi kugwiririra

“Patadutsa ola limodzi adakalibwenza khandalo koma likulira kwambiri ndipo mayi ake pomusintha adaona magazi pa zovala zake komanso mabala kumalo ake obisika,” adalongosola Sipiliano.

Iye adati ngakhale zotsatira zochokera kuchipatala chachikulu cha Zomba zatsimikiza kuti khandalo lidagwiriridwa.

Kanjira amachokera m’mudzi mwa Mtiya,  kwa T/A Mlumbe m’boma la Zomba.

Ndipo kumapeto a sabata yatha, kudatuluka uthenga wa mwana wina ku Chigumula amene adatepa bamboo ake pomwe amamunyengerera kuti akagone nawo. Bamboyo amakakamira mwanayo kuti akagone naye posinthanitsa ndi fizi.

Malinga ndi zomwe mwanayu watumiza m’masamba a mchezo, bamboyo yemwe sakudziwika bwino dzina lake akumveka akumuuza mwanayo kuti akavulire zonse pabalaza ndipo akalowe kuchipinda kwa bamboyo ali maliseche ngati chibalo chokana kugona naye mmbuyomu.

“Ndidaganiza zowajambula palamya akukamba zawozo chifukwa nthawi zambiri n’kamadandaula anthu amandinena kuti ndine wabodza,” adatero mtsikanayo.

Izi zili apo, m’boma la Dowa, apolisi atsekera mnyamata wina wa zaka 21 yemwe adagwiririra ana amuna anayi a zaka kuyambira 10 mpaka 17 ndi kuwapatsanso matenda opatsirana pogonana.

Malinga ndi mneneri wa apolisi m’boma la Dowa, Gladson M’bumpha, Innocent Poita akuganiziridwa kuti wakhala akugwiririra anawa kuchoka m’chaka cha 2016 kufika pa 19 November chaka chino m’mudzi wina ku Dowako.

“Anyamatawa amapita kunyumba kwake kukaonera kanema pa lamya yake ya m’manja.  Ndipo pa 19, atamaliza kuonera kanemayo, mmodzi mwa anyamatawo adatsalira kunyumbako zomwe zidapangitsa anzakewo kukaulula kwa makolo ake kuti Poita amawagona akakhala kunyumba kwake,” adalongosola M’bumpha.

Poti amachokera m’mudzi mwa Ndalama kwa T/A Chiwere, m’boma la Dowa.

N’zodandaulitsa kuti pomwe mbali zina zili pa likiliki kuyesetsa kuthana ndi mchitidwe wogwiririra zinthu zikunka zikipiratu.

M’chaka cha 2018, apolisi adapeza kuti ana 1 539 ndiwo adagwiriridwa, pomwe m’chaka cha 2019 anthu 1 766 adagwiriridwa ndipo kuchoka January chaka chino kufika mwezi wa September ana 1 501 adagwiriridwa.

Izi zikutanthauza kuti  pofika mwezi wa mawa wa December chiwerengerochi chikhala chitadutsa chiwerengero cha chaka chatha cha 1 766.

Komatu si ana okha omwe akukumana ndi nkhanza m’dziko muno chifukwa ngakhale nawo atsikana komanso amayi akukumana nazo.

Pomwe Msangulutso udacheza ndi amayi ena omwe amagwira ntchito yoyendayenda mumzinda wa Mzuzu, zidaululikanso kuti amayiwa amagwiriridwa makamaka ndi abambo ogwira ntchito za chitetezo monga apolisi ndi asilikali.

Mmodzi mwa amayiwa yemwe sitimutchula dzina pomuteteza adati ambiri mwa abambo azachitetezowa amawagona ulele powaopseza komanso akamaliza pamenepo amawamenya.

“Sabata yomwe ino, bambo wina wa chitetezo adandigona mondikakamiza komanso sadagwiritse ntchito chitetezo. Atatha pamenepo adandimenya komanso kunditengera zakudya ndi zakumwa zomwe ndidali nazo,” iye adalongosola.

Polankhulapo pa nkhanza zomwe zikuchitikira amayi, atsikana ndi ana a m’dziko muno, Jessie Ching’oma wochokera ku bungwe lomwe si laboma la NGO Gender Coordinating Network (NGO-GCN) adati anthuwa akufunika zilango zokhwimitsitsa, zoopsa kuti ena atengerepo phunziro.

“Anthuwa akufunika zilango zomwe sizidalembedwe, zilango zoopsa kuti mwina mchitidwewo uchepeko,” adalongosola Ching’oma.

Pomwe Amos Nyaka yemwe amamenyeranso ufulu adauza msonkhano wa achinyamata mumzinda wa Mzuzu kuti mpofunika kuunikanso zina mwa zikhalidwe zathu chifukwa ndi zomwe zikupititsa patsogolo mchitidwewu.

Previous Post

FDH supports FIMDA Lakeshore Conference

Next Post

Tidakumana ku BICC

Related Posts

Left economy in tatters: Muluzi
Front Page

Malawi’s public debt now at K5.8 tn

May 21, 2022
Signed the statement: Namiwa
Front Page

Cdedi demands govt action on forex

May 21, 2022
Chakaka-Nyirenda: I recommend termination of the contracts
Front Page

AG urges cancellation of Movesa no. plate deal

May 21, 2022
Next Post

Tidakumana ku BICC

Opinions and Columns

Layman's Reflection

New IMF programme pivotal moment for Tonse Alliance

May 21, 2022
Family Table Talk

Historical lessons on the value of forgetting

May 21, 2022
My Diary

Politics of ‘kutola chikwama’

May 21, 2022
Bottom Up

Ukraine war: Sanctions backfire?

May 21, 2022

Trending Stories

  • Left economy in tatters: Muluzi

    Malawi’s public debt now at K5.8 tn

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • CAF accepts FAM’s request on Flames fixture shift

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Gaba comes up with two options

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Onesimus leaves Major One Records

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • UN bets K66bn on LMC’s plan

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.