Sunday, February 28, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Ntchito ilipo

by Solomon manda bobby kabango
10/10/2015
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

 

Zilikoliko mawa lino kubwalo la masewero la Kamuzu Stadium kumene mphunzitsi wa timu ya dziko lino Ernest Mtawali akuyembekezeka kutsogolera anyamata ake kuchita chamuna chogonjensa Tanzania ndi kudzigulira malo mumpikisano wa 2018 World Cup.

RelatedHeadlines

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

Sukulu zitsegulidwanso

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

Kuti ipitirire m’ndime ina ya mpikisanowu, timu ya Malawi ikuyenera kuchinya zigoli zosachepera ziwiri pambali polepheretsa alendo a kumpoto kwa dziko linowa kukoleka mpira muukonde.

Mtawali akuti mawa Flames idya monona
Mtawali akuti mawa Flames idya monona

Izi zili chonchi potsatira kugonja kwa Flames 2-0 pabwalo la Benjamin Mkapa ku Tanzania Lachitatu. Malawi itapambana 3-1 m’masewero achiwiri mawa, idzafanana zigoli ndi alendowa koma siidzakhalabe ndi mwayi wodumphira mu ndime ina ya mpikisanowu chifukwa malamulo amati zikatere, yemwe adapeza chigoli pabwalo la ena ndiwo akatswiri.

Koma mpira ukathera 2-0 mokomera Amalawi, tikhala kuti tafanana mphamvu ndipo pakayenera kulowa m’ndime ya kapherachoka wa mapenote kuti papezeke oyalula mphasa ndi kulowa m’ndime yachiwiri yodzakumana ndi timu ya dziko la Algeria.

“Nzotheka kupambana ndi zigoli zochuluka Lamulungu likudzali. Tinaluza ku Tanzania chifukwa chochinyitsa zigoli zopepera. Koma pano mavuto onse takonza ndipo tili okonzeka kuchotsa chitonzo chomwe tili nacho pakalipano,” adatero Mtawali m’sabatayi.

Komadi timumvere mphunzitsiyu zoti chilipo chipambano chokwanira mawa? Sitigwiritsidwanso fuwa la moto?

“Zitengera ndi mmene alowetsere osewera komanso momwe osewerawo adzadziperekere. Nkofunika tidzalimbikire kuthira nkhondo kutsogolo kwathu mowirikiza. Komanso tisadzawapatse adani mpata wobwerabwera kugolo lathu. Mwayi ulipo,” adatero kadaulo woona za masewero a mpira Charles Nyirenda.

Nyirenda, yemwe adakhalapo mkulu wa bungwe la masewero a mpira mdziko muno la FAM, adaonjezera kuti ochemerera mpira asadzafooke polimbikitsa osewera a dziko lino ndi mingoli yopereka chikhulupiliro.

Pamene Malawi imakomana ndi Tanzania Lachitatu, Mtawali adali atachotsa komanso kuonjezera osewera ena amene adapatsidwa mpata m’masewero okumana ndi Swaziland kwawo mumpikisano wa Africa Cup of Nations omwe adathera 2-2.

Iye adachotsa John Lanjesi kumbuyo ndi kuseweretsapo Miracle Gabeya ndipo adachotsanso Richard Chipuwa pagolo ndi kuikapo Simplex Nthala. Kutsogolo, adaikako Chawanangwa Kaonga mmalo mwa Chiukepo Msowoya yemwe adavulala.

Previous Post

Can Flames overturn the tables?

Next Post

Mtima pansi, mayeso A jce alipo chaka chino

Related Posts

HRDC pursuing this matter further: Trapence
Nkhani

‘Osakondera odya nawo K6.2 biliyoni’

February 27, 2021
Teachers KK | The Nation Online
Nkhani

Sukulu zitsegulidwanso

February 27, 2021
Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols
Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

February 19, 2021
Next Post
jce students | The Nation Online

Mtima pansi, mayeso A jce alipo chaka chino

Opinions and Columns

My Diary

Light that came with Covid-19

February 27, 2021
Guest Spot

Resurgence of albino killings deplorable

February 27, 2021
Back Bencher

Is violence a boomerang effect in DPP?

February 27, 2021
Off the Shelf

Sacrificial lambs of a dysfunctional system

February 27, 2021

Trending Stories

  • Court has declared Escom a private firm

    Court declares Escom private company

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • K1.7bn Chisale assets seized

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside Chisale’s seized property

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • What the hell is APM doing with BJ?

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • HRDC alleges threats, intimidation from investor

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.