Friday, January 22, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Odzipha akuchuluka

by Wisdom Chirombo
03/01/2021
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

M’chaka cha 2020 chiwerengero cha anthu odzipha chidakwera poyerekeza ndi cha m’chaka cha 2019.

Kafukufuku wa apolisi akuonetsa ku chiwerengerochi chidachoka pa 166 miyezi ya January mpaka August chaka cha 2019 kukafika pa 182 miyezi ngati yomweyi m’chaka cha 2020.

RelatedHeadlines

Amapita kukagula zomwera tiyi

Anatchezera

Mbuzi ndi zosavuta Kusamalira, kudyetsa

Wachiwiri kwa mneneri wa apolisi m’dziko muno, Peter Kalaya, ndiye adapereka chiwerengerochi.

Iye adati ambiri mwa anthuwa adali amuna a zaka zapakati pa 15 ndi 40.

court room | The Nation Online
An illustration of court proceedings

Kalaya adati ambiri amadzipha kaamba ka mavuto a za m’banja, komanso nkhani zachuma.

Iye adati apolisi akupepha Amalawi kuti akakumana ndi mavuto azipita ku victim support unit yomwe ali nayo pafupi kukalandira uphungu.

“Kudzipha si yankho chifukwa pali njira zina zabwino zothesera mavuto,” adatero mkuluyu.

Ngale Massa, katswiri wa za kaganizidwe ka munthu, adapempha anthu kuti afunsa uphungu kwa anzawo akakumana ndi mavuto.

Malingana ndi zotsatira zakafukufuku yemwe bungwe la St John of God lidatulutsa mwezi wa November 2020, mwa anthu 100 aliwonse omwe amadzipha 80 ndi amakhala abambo.

Kafukufukuyu akusonyeza kuti 57 mwa 100 anthu aliwonse adadzipha podzimangirira pamene 30 mwa 100 aliwonse adagwiritsa ntchito chiphe.

Kafukufukuyu akuti mchitidwewu ukuchuluka chifukwa chosowa ukadaulo pa kaganizidwe koyenera.

Katswiri wina pa nkhani ya kaganizidwe wa pa sukulu ya College of Medicine, Chiwoza Bandawe, adati n’zokhumudwitsa kuti chiwerengero cha ana odzipha chikukweranso.

“Anthu ambiri safuna kufa, koma kuchotsa ululu womwe akukomana nawo.

“Amaganiza kuti akadzipha ndiye kuti athana ndi mavuto omwe akukumana nawo,” adatero Chiwoza.

Iye adati chiwerengero cha anthu odzipha chitha kutsika Amalawi ambiri ataphunzira kaganizidwe koyenera, komanso njira zothetsera mavuto awo.

Previous Post

Mangochi CCAP charity shelters late pastor’s wife

Next Post

Anatchezera

Related Posts

marriage | The Nation Online
Chichewa

Amapita kukagula zomwera tiyi

January 3, 2021
Chichewa

Anatchezera

January 3, 2021
goats | The Nation Online
Chichewa

Mbuzi ndi zosavuta Kusamalira, kudyetsa

January 2, 2021
Next Post

Anatchezera

Discussion about this post

Trending Stories

  • Escaped South African bail: Bushiris

    Bushiri says not seeking political intervention

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi closes in on hefty US deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Vendors back on streets amid Covid-19 surge

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi loses 5% of GDP on donor withdrawal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

Business Unpacked

Towards Malawi2063, lessons from Vision 2020

January 20, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 20, 2021
In pursuit of development

India’s vaccine drive

January 20, 2021
My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.