Wednesday, April 21, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Okhala kumalire ku Phalombe akulira

by Bobby Kabango
04/10/2014
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email
Ena mwa amayi adafika kumsonkhanowo
Ena mwa amayi adafika kumsonkhanowo

Anthu ena ku Phalombe adandaula ndi nkhanza zimene amachitiridwa akapita m’dziko la Mozambique ndiponso ndi chiwerengero cha ana obedwa m’bomalo.

Mchitidwe woba ndi kuzembetsa ana wanyanya ndipo ku Phalombe zankitsa chifukwa chaka chino chokha ana 14 abedwa kale, pomwe chaka chatha ana asanu ndiwo adasowetsedwa.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

Izi ndi malinga ndi lipoti la polisi m’bomalo lomwenso lasonyeza kuti ku Zomba ana anayi okha ndiwo abedwa pomwe Maboma a Mangochi, Machinga, Chiradzulu ndi Mulanje palibe amene wasowetsedwa.

Anawatu ndi a zaka zosaposa 18 ndipo ambiri akumanamizidwa kuti akukawalemba ntchito koma akafika m’dzikolo akumagwiritsidwa ntchito yogulitsa matupi awo kapena kugwira ntchito zosalingana ndi misinkhu yawo.

Si kusowetsedwa kwa ana kokha komwe kwanyanya m’boma la Phalombe, nzika za dziko lino akuti zikalowa ku Mozambique zikumalipitsidwa kapena kumenyedwa pamene nzika za ku Mozambique zikalowa m’dziko muno savutitsidwa.

Nawo achitetezo a m’dziko la Mozambique akuti akumalowa m’dziko muno ndi mfuti pomwe ena atavala zovala zapolisi.

Izi zidachititsa kuti anthu a magulupu a Chinani, Nthambula, Nambazo, Mpinda komanso Mtemanyama kwa T/A Nazombe ndi Senior Chief Chiwalo asonkhane pamsika wa Mphwisi kuti apereke madandaulo kwa mkulu wa apolisi kuchigawo chakummwera.

Gogo Lone Tawanga wa m’mudzi mwa Chinani adati chifukwa cha njala amapita ku Mozambique komwe amakalimitsa chinangwa kuti adzadye ndi ana ake koma chaka chatha atapitako adagwidwa ndi asilikali a m’dzikolo.

“Adandimenya ndipo adati ndilipire K1 500 ngati ndikufuna ndidzipulumutse. Nditanenerera ndidapereka K600. Timadabwa kuti tikalowa m’dziko lawo timazunzidwa koma iwo amalowa m’dziko muno popanda vuto,” adadandaula Tawanga.

Nyakwawa Mandawala ya mwa Senior Chief Chiwalo idati nayonso idagwidwa pamene imakagula ufa wophikira mandasi ndipo idalipitsidwa. Koma kudabwa kwa mfumuyi ndikoti zikutheka bwanji anthu a m’dziko la Mozambique savutitsidwa akalowa m’dziko muno.

“Tikudabwa kwambiri, chifukwa chiyani boma lathu likulekerera kuti tizizunzidwa motere? Ana athu akutengedwa nthawi iliyonse,” idatero mfumuyo yomwe idalankhula mokwiya kwambiri.

Mandawala adaonjeza kuti ndi bwino boma likhwimitse chitetezo kuti anthu a m’dzikolo asamangolowa m’dziko muno mwa chisawawa ndipo akagwidwa azilangidwa, ganizo lomwe lidavomerezedwa mokweza mawu ndi anthu oposa 300 amene adasonkhana panthawiyo.

Nkhumano omwe udalipo Lachiwiri m’sabatayi udakonzedwa ndi bungwe la mpingo wa Katolika loona za chitukuko la Catholic Development Commission (Cadecom) ndi thandizo lochokera ku Caritas Austraria. Bungweli lidakhazikitsa magulu omvera wailesi m’bomali amene amathandiza kuulutsa nkhani zomwe zimachitika m’midzi.

Peter Pangani wa bungwe la Cadecom adati kaamba ka mavuto amene anthu akhala akukumana nawo m’bomali nchifukwa chake adapanga nkhumanowo kuti adindo ndi mafumu adzimvere mavuto amene anthu m’bomalo akukumananawo.

“Tidapempha a bungwe la Develpment Communications Trust (DCT) amene ndi akadaulo pa zofalitsa nkhani kuti agwire ntchito ndi amagulu omvera wailesiyi kuti tikhale ndi tsiku lomwe anthu angapereke nkhawa zawo. Ife tasangalala kuti adindo adzimvera okha za mavuto amene akukumana nawo ndipo mayankho eya ayamba kale kuperekedwa,” adatero Pangani.

Koma mkulu wa apolisi kuchigawo chakummwera, Wilson Matinga adatsimikizira anthuwa kuti pakhala kusintha. Iye adati chitetezo sichingakhale ngati apolisi alipo ochepa komanso ngati palibe galimoto zoyendera. Polisi ya Phalombe ili ndi galimoto imodzi yomwe siifikira m’madera onse.

“Tamva anthu alankhula, ndipo akunena zoona. Koma tikuwatsimikizira kuti pakhala kusintha, ndikamba ndi anzanga a dziko la Mozambique kuti mavutowa athe.

“Wapolisi wa dziko lawo saloledwa kulowa m’dziko muno atavala zachitetezo kapena kunyamula mfuti. Tikutumizanso asilikali ena kuti mwina akwane 7 ndi amene alipo kale kudera lino cholinga chitetezo chikhwime,” adatero Matinga.

DC wa bomalo Paul Kalilombe adauza apolisi kuti akatenge njinga yamoto kuofesi kwake kuti ithandize apolisi kukhwimitsa chitetezocho. Naye Senior Chief Chiwalo adagwirizana kwathunthu ndi zomwe anthu ake adadandaulira akuluakuluwa.

Njira yaulere yomwe anthu amaimbira foni mwa ulere kupereka madandaulo awo ya Child Help Line 828 (CHL 828) ikuwonetsa kuti pofika mmwezi wa June chaka chino, ana 684 ndiwo adataidwa, ana 14 adabedwa, 195 ndiwo amagwiritsidwa ntchito zoposa msinkhu wawo, 53 ndiwo adakakamizidwa kukalowa banja, 259 ndiwo adachitidwa nkhaza monga kumenyedwa komanso ana 25 amene adagwiriridwa m’dziko muno.

Avatar
Bobby Kabango
Previous Post

Njikho tops Simama League score chart

Next Post

Leading from the front in malaria fight

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
Shire RIver

Leading from the front in malaria fight

Opinions and Columns

My Turn

Honour Malewezi posthumously

April 21, 2021
Big Man Wamkulu

Hot babe wants to trap me, should I ran?

April 18, 2021
Political Uncensored

Mighty mess!

April 18, 2021
My Thought

Chakwera’s indecisiveness will be his downfall

April 18, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • FB IMG 1618917210807 | The Nation Online

    ‘Tobacco is dying crop’

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Suspension without pay sparks debate

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • NGOs hail Chakwera, urge caution

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MEC is back

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Refugees ask govt to review relocation order

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.