Thursday, May 26, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Opanda masiki asayende dala

by Steven Pembamoyo
24/07/2021
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kuli cheucheu poyenda paliponse m’dziko muno kuona ngati apolisi ali pafupi makamaka kwa omwe sadachivomereze kuti masiki ikhoza kuwateteza ku matenda a Covid-19.

Kuyambira Lolemba, apolisi akhala ali kalikiliki mmalo osiyanasiyana kuphatikizapo m’misika ya m’makwalala kugwira onse wopanda masiki n’kumawalipiritsa K10 000 ngati chindapusa.

Apolisi kugwira wosavala masiki ku Blantyremwa anthu kuti achite

Ntchitoyi yomwe akuitcha Opaleshoni vala masiki idayamba komiti yotsogolera kulimbana ndi matendawa itatulutsa malamulo atsopano othanirana ndi Covid-19.

Malamulowo adakhazikitsidwa komitiyo itaona kuti anthu opezeka ndi matendawa akuchuluka tsiku lililonse pomwe anthu amakhwefula za kapewedwe ka matendawo.

Malingana ndi mneneri wapolisi a James Kadadzera, apolisiwo sadapange malamulo koma adapatsidwa malamulowo kuti azilimbikitsa.

“Mumadziwa ntchito yapolisi n’kuonetsetsa kuti malamulo a dziko akutsatidwa koma amapanga malamulowo ndi anthu ena. Tidalengeza kuti kuyambira Lolemba lapitali tisintha magiya ndiye anthu asatidandaule,” adatero a Kadadzera.

Koma omenyera ufulu wa anthu a Michael Kaiyatsa wa CHRR wati opeleshoniyo ndi yofunika koma apolisi adziwe mlingo wa mphamvu zawo pogwira ntchitoyo.

“N’zofunikira kuti boma lionetsetse kuti anthu akupewa Covid-19 chifukwa

Nkhani yagona poti apolisiwo ayigwira bwanji ntchitoyo chifukwa sitikufuna aziphwanyaso ufulu wa anthu,” adatero a Kaiyatsa.si nthenda yabwino.

Iwo amayankha nkhawa za anthu pa nkhanza zomwe apolisi ankachita pa opeleshoni ngati yomweyi nyengo ya mphepo yachiwiri ya matenda a Covid-19 kumayambiriro kwa chakachi.

Zina mwa nkhanzazo n’zomwe apolisi ankachitira anthu akawapeza kopemphera, kumowa kapena akuyenda itadutsa 8 koloko usiku nthawi yomwe idakhazikitsidwa.

A Kadadzera ati apolisi onse omwe akugwira nawo ntchitoyi adaunikiridwa kale za kagwiridwe ka ntchitoyo kuti pasamvekenso nkhanza zosagwirizana ndi malamulo.

Anthu m’mizinda yonse ikuluikulu adasonyeza kuti ayamba kutsatira malamulowo koma ena akadanyozera.

Mwachitsanzo, ku Blantyre Lolemba pomwe opaleshoni imayamba anthu ambiri adayesetsa kuvala masiki komanso magalimoto onyamula anthu adayesetsa kutsata mlingo woyenera.

Mumzinda wa Lilongwe zidayamba mwa kasakaniza pomwe anthu ena amavala masiki pomwe ena amangoyenda ngati kuti kulibe matendawa.

Galimoto zonyamula anthu nazo kufikira mpaka Lachitatu zimangonyamulapo bola anthu apezeka ndipo eni galimotozo samalabada kuti anthuwo avala masiki kapena ayi.

Mneneri wapolisi m’chigawo chapakati a Alfred Chimthere adatsimikiza Lolemba kuti aonetsetsa kuti apolisi ali ponseponse kuonetsetsa kuti malamulo a Covid-19 akutsatidwa.

“Tidaunika kale ndipo ndondomeko ili mmalo kwatsala timwaze asilikali anthu kuti anthu ayambe kutsatira zomwe malamulo akunena. Wonyozera n’zawo chifukwa chenjezo lidaperekedwa kale, azilipira chindapusa,” adatero a Chimthere.

Ku Mzuzu ndiko opaleshoni idayamba mozizira kwambiri chifukwa zovala masiki kapena kunyamula mlingo oyenera m’magalimoto kudalibe Lolemba.

Previous Post

For the love of the pencil

Next Post

Mixed fortunes for Nomads

Related Posts

Nkhani

Agwidwa ndi yunifomu za polisi

May 22, 2022
Nkhani

Dollar yasowa

May 21, 2022
Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
Next Post
Wanderers are already getting funds from Salima Sugar

Mixed fortunes for Nomads

Opinions and Columns

Business Unpacked

Tame egos, take risks to grow economy

May 26, 2022
People’s Tribunal

What was that press briefing all about?

May 22, 2022
Big Man Wamkulu

Wife, in-law plotting my downfall

May 22, 2022
My Thought

Tonse Alliance died on arrival

May 22, 2022

Trending Stories

  • Mutharika on the campaign trail in 2019

    APM under pressure

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Musician Martse in hospital after fire accident

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Kalindo earmarked for diplomatic post

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Nyasa Mobile Limited partners Vodafone

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Govt, IMF talk deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.