Thursday, February 25, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Otsutsa adzudzula MEC

by Steven Pembamoyo
23/06/2017
in Nkhani
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Bungwe la Malawi Electoral Commission (MEC) liyenera kutambasula bwino za pangano lake ndi bungwe limene likupereka zitupa za unzika la National Registration Bureau (NRB) pa zoti lidzagwiritsa ntchito zitupazo pa kalembera wa chisankho cha 2019, watero kadaulo pa ndale Mustafa Hussein.

Zipani za ndale, makamaka zotsutsa boma zakhala zikunena kuti chikonzero cha MEC n’kufuna kudzathandiza chipani cha DPP kubera mavoti.

RelatedHeadlines

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

Aphungu akumana lolemba

Mtsutso pa zotsegulira sukulu lolemba

registration | The Nation Online
Kalembera wa nzika ali mkati

“Mwati mudzagwiritsa ntchito zitupa za unzika kuti Amalawi alowe m’kaundula wa zisankho. Apatu mpofunika kuti pamveke bwino chifukwa anthu akusokonekera,” adatero Hussein.

Zipani zotsutsa boma zakhala zikudandaula ndi ganizo la MEC lodzagwiritsa ntchito zitupa za unzika kuti munthu adzalowe m’kaundula wa chisankho cha 2019.

Zipanizi zakhala zikubweretsa nkhaniyi m’Nyumba ya Malamulo momwe aphungu akukambirana za bajeti ya 2017/18 ndipo moto weniweni udabuka lolemba lapitali pa nkhumano yomwe bungwe la MEC lidapangitsa kuti lifotokozerane ndi zipani nkhani yokhudza chisankhochi.

Nthumwi za zipani zotsutsazi makamaka za Malawi Congress Party ndi Peoples Party, zidabooleza kuti zikukhulupilira kuti ganizoli ndi njira imodzi yofuna kudzabera chisankhochi ndipo zidanenetsa kuti sizilola kuti pulaniyi idutse.

Phungu wa kummawa kwa boma la Dowa Richard Chimwendo-Banda wa Malawi Congress Party (MCP) adati akuona kuti MEC ikukonza zodzathandiza chipani cholamula cha Democratic Progressive (DPP) kubera chisankho.

Iye adati ndiwodabwa ndi kukakamira kwa bungwe la MEC kuti lidzagwiritse ntchito zitupa za unzika popanga kaundula wa anthu odzaponya voti chonsecho silikutengapo gawo lililonse pa zakapangidwe ka zitupazi.

“Bungwe la MEC lidali kuti pomwe nthambi yopanga kalembera wa zitupazi imayamba ntchito yake? Tili ndi chikhulupiliro kuti ali ndi mapulani odzabera chisankho ndipo ndikuuzeni kuti ulendo uno sitikulekelerani,” adatero Chimwendo-Banda.

Iye adati bungwe la MEC lisiye kulowerera ntchito za eni ndipo lipange pologalamu yake yakalembera wa m’kaundula wa chisankho mmalo modalira kuwolokera pamsana pa anzawo.

Wampampando wa bungwe la MEC Jane Ansah yemwe ndi woweruza milandu ku khothi lalikulu la apilo sadakondwe ndi zomwe adanena aphunguwo ndipo adawadzudzula kuti nawo akulephera udindo wawo posafotokozera anthu awo za kufunika kwa zitupazi.

Iye adatsutsa zoti bungweli lili ndi maganizo odzabera chisankho mwanjira iliyonse koma kuti likufuna kuti anthu ovomerezeka okha ndiwo adzaponye voti mu 2019.

Nduna ya za m’dziko ndi chitetezo Grace Chiumia adavomera kuti kalembera wa zitupa za unzika ikukumana ndi zokhoma monga kufaifa kwa zipangizo zogwiritsa ntchito.

Previous Post

Jeffrey punches Mpoto as her Nkhota Kota rots

Next Post

Workplace manners

Related Posts

Flashback: Learners observing some of the Covid-19 protocols
Nkhani

Ayamikira boma pa ganizo lotsegulanso sukulu

February 19, 2021
Parliament in session
Nkhani

Aphungu akumana lolemba

February 19, 2021
Ophunzira azidziteteza ku Covid
Nkhani

Mtsutso pa zotsegulira sukulu lolemba

February 5, 2021
Next Post
Stressed business woman multitasking in her office

Workplace manners

Opinions and Columns

In pursuit of development

The Chinese approach to network-building

February 25, 2021
Business Unpacked

Back to the drawing board on budget

February 25, 2021
Rise and Shine

How do successful people think?

February 25, 2021
My Thought

Malawi needs fixing, not politicking

February 21, 2021

Trending Stories

  • Co-chaired the task force: Phuka (L) and Mwanamvekha

    K780M Dodma Covid-19 feast

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Bushiri’s daughters blocked from flying out

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Censorship Board acts on ‘Aunt Nellie’ videos

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Inside k6.2bn

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Convention In July 2023—DPP

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.