Saturday, May 21, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Pali mtsutso pa zotsegulira sukulu

by Steven Pembamoyo
03/09/2021
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Pomwe unduna wa zamaphunziro watsindika kuti ophunzira a m’sukulu zogonera komweko akuunikidwa zizindikiro za Corona akafika, bungwe la aphunzitsi la Teachers Union of Malawi (TUM) lakana kuti izi sizikuchitika.

Tamvani adali ndi chidwi kulondoloza ngati zomwe unduzawo adalonjeza potsekera telemu yachiwiri kuti potsegulira telemu yachitatu ophunzira m’sukulu zogonera komweko adzayenera kuunikidwa polowa mumpanda zikuchitika.

Ophunzira ayeneranso kupeza mamasiki

Mlembi wamkulu wa unduna wa zamaphunziro a Chikondano Mussa Lachitatu adati zinthu zikuyenda bwino m’sukulu ndipo mwana aliyense akuunikidwa pofika pasukulu.

“Ndinganene kuti zinthu zayamba bwino ndipo kuunika kukuchitika koma pakalipano tilibe nambala yeniyeni kuti taunika angati ndipo zotsatira zikutuluka zotani. Koma omwe akupezeka ndi zizindikiro tikuwaika pamphepete kuti akayesedwe bwinobwino,” adatsimikiza a Mussa.

Koma Lachitatu lomwelo, mkulu wa bungwe la TUM a Willie Malimba adati ili ndi bodza la mkunkhuniza chifukwa konse komwe bungwelo layendera,  mumpanda osayesedwa.ophunzira akungolowa

“Akunama zimenezo sizikuchitika nkomwe ayi, ngakhale inuyo mutati muyendere sukulu zingapo m’zigawo zonse mutsimikiza chifukwa tisamapakane mafuta pakamwa ayi,” adatero a Malimba.

Kadaulo pa zamaphunziro a Benedicto Kondowe adati kusemphana maganizoku kukuyenera kukhalapo chifukwa olo kuunika kutakhalapo sizingafanane m’sukulu zonse.

“Nkhani yoyamba ndi mapezedwe a sukulu iliyonse komanso boma limapereka zipangizo mosiyana m’sukulu malingana ndi sukuluyo ndiye zambiri zayenera kusiyana,” adatero a Kondowe.

Nkhawa ina ya a Malimba ndiyazipangizo zodzitetezera komanso zaukhondo zomwe akuti mpaka pano sizidagulidwe m’sukulu zambiri komanso sukulu zambiri zatsegulidwa osapopera mankhwala ngati momwe zidakhalira telemu yatha.

“Boma lidapereka K100 miliyoni m’boma lililonse kudzera kumawofese a zamaphunziro koma tikudabwa kuti mpaka pano zipangizo sizikugulidwa. Aphunzitsitu ali pachiopsezo kwambiri,” adatero a Malimba.

Mkulu wa mgwirizano wa mabungwe okjudzidwa ndi zaumoyo wa Malawi Health Equity Network (Mhen) a George Jobe adati mpofunika kusamala makamaka potanthauzira kuunika ndi kuyesa Covid-19 komanso kuti akati zodzitezera kwa aphunzitsi n’chiyani.

“Pali nkhani ziwiri apapa, yoyamba ndi yoti kodi kuunika Corona nchiyani nanga aphunzitsi akati akufuna zodzitetezera akunena chiyani chifukwa zodzitetezera ndi dzina la gulu.

“Aphunzitsiwo abwere poyera kuti akufuna masiki, sopo, ziwiya zosambira mmanja ndi sanitayiza kuti bajeti yawo isavute komanso isaoneke yaikulu ayi,” adatero a Jobe.

Koma a Malimba adati boma lipereke ndondomeko yakagulidwe ka zipangizozo kwa akuluakulu amaphunziro m’maboma nthawi isadathe chifukwa mayeso a Sitandade 8 ayandikira ndipo kudziteteza kudzafunika kwambiri panthawiyo.

A Mussa ati unduna wawo utulutsa zotsatira za kuunika komwe akuti kukuchitika akamaliza kutolera za mmaboma onse.

Previous Post

AIP draining public purse- Cdedi

Next Post

SMEs optimistic on growth

Related Posts

Nkhani

Dollar yasowa

May 21, 2022
Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Next Post
Centre of 
controversy: Chikhosi

SMEs optimistic on growth

Opinions and Columns

Layman's Reflection

New IMF programme pivotal moment for Tonse Alliance

May 21, 2022
Family Table Talk

Historical lessons on the value of forgetting

May 21, 2022
My Diary

Politics of ‘kutola chikwama’

May 21, 2022
Bottom Up

Ukraine war: Sanctions backfire?

May 21, 2022

Trending Stories

  • Left economy in tatters: Muluzi

    Malawi’s public debt now at K5.8 tn

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • CAF accepts FAM’s request on Flames fixture shift

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Gaba comes up with two options

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Onesimus leaves Major One Records

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • UN bets K66bn on LMC’s plan

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.