Monday, July 4, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Pemphererani dziko lino, ipempha ECM

by Staff Writer
25/02/2012
in Nkhani
1 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Mpingo wa katolika wapempha Amalawi kuti apempherere dziko la Malawi ndi utsogoleri wadziko lino panyengo ya Lenti.

Muuthenga wake wanyengoyi, mkulu wa mabishopu m’gulu la Episcopal Conference of Malawi (ECM) Joseph Zuza wati padakali pano, Amalawi akudutsa mumazunzo.

Zuza adati: “Atsogoleri athu ali ndi udindo waukulu woti moyo uzikhala ofewa wa ife tonse. Monga okhulupirira tiyenera kudziwa kuti Mulungu sangatitaye.”

Zuza adati zina mwa zomwe Amalawi ayenera kupempherera kuti zichepe ndi katangale ndi ziphuphu, kukondera ochokera kudera kwanu, kusankhana mitundu, zilakolako zakuthupi, ufiti, nkhanza kwa ana, uchidakwa ndi kupembedza Satana.

Zuza adapempha akatolika kuti aziyesetsa kukhala Akhristu achitsanzo, ndikutsatira malamulo a Mulungu.

“Aliyense ayenera kuonetsetsa kuti akukhala okhulupirika pamaso pa Mulungu,” adatero Zuza.

Ndipo muuthenga wake m’nyengoyi, Papa Benedict wachikhumi ndi chisanu n’chimodzi adati masiku 40 amene Akatolika akhale akupunguza ayenera kulingalira za mawu opezeka pa Ahebri 10 ndime 24.

“Tiyenera kukhudzidwa ndi mavuto a ena; kukhala okondana kumanso kugwira ntchito zabwino,” adatero Papayo.

Kwa masiku 40, Akatolika amakhala akupunguza ndipo zimayamba ndi tsiku la phulusa, lomwe lidali Lachitatu.

Panthawiyo, iwo amakhala akupemphera, kugawana, kulingalira molimba, kusala komanso kuchita zachifundo mpaka nthawi ya Pasaka mu Epulo.

Previous Post

Group One to create 1 000 new jobs

Next Post

‘I know what people want’

Related Posts

Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Katundu wa a Mtambo adali kuseri kwa ofesi za khonsolo
Nkhani

Agona ku maofesi a khonsolo ya Mzuzu

June 4, 2022
Next Post

‘I know what people want’

Opinions and Columns

My Turn

Child neglect and street robbery

July 4, 2022
Editor's Note

MPs’ houses to cost taxpayers K60bn

July 3, 2022
Big Man Wamkulu

Her body count is too high, should I dump her?

July 3, 2022
My Thought

Women underutilise digital platforms

July 3, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Dubai firm cries foul

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Her body count is too high, should I dump her?

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MPs’ houses to cost taxpayers K60bn

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MP Chihana flops at Sadc elections

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MCP, UTM opt for peaceful discussions

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.