Saturday, May 28, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Pimani onyamula mafuta

by Nation Online
26/04/2020
in Chichewa
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kati deru kadaopsa mlenje. Anthu okhala kwa Sonda komwe kuli nkhokwe za mafuta m’zinda wa Mzuzu sakumwa madzi ndi madalaivala amene amadzatula mafuta kuchokera m’dziko la Tanzania.

Pomwe tinkasindikiza nkhanyiyi n’kuti m’dziko la Tanzania anthu 285 akudwala matenda a Covid-19, 11 atachira ndipo 10 atamwalira ndi matendawa.

Izi zikupereka mantha kwa anthu a kwa Sonda kuti madalaivala omwe akubweretsa mafuta m’derali atha kuwatengera imfa.

Madalaivalawa akamalowa m’dziko muno sakuwabindikiza monga zikuyenera kukhalira pamene ukutuluka kapena kulowa m’dziko muno.

Galimoto zonyamula mafuta kungofika kumene kuchokera ku Tanzania

Koma mneneri wa unduna wa zaumoyo Joshua Malango adati anthu asachite mantha chifukwa boma liyamba kubindikiza madalaivalawo kwa sabata ziwiri pachipata cha dziko lino kuyambira sabata ino. 

Iye adati kusunga madalaivalawo kuthandiza kuthana ndi matendawo.

“Anthuwo sadziyezedwa ngati ali ndi Covid-19 kapena ayi mokakamizidwa, koma chizichitika n’chakuti aliyense wolowa m’dziko muno adzikhala kaye kwa sabata ziwiri pa malo olowerawa, kuti tione ngati akuonetsa zizindikiro za nthendayo ndipo aziyesedwa akaonetsa zizindikirozo,” adatero Malango.

Malinga ndi wapampando wa nthambi ya chitetezo m’deralo, Isaac Soko, madalaivalawo akafika kumeneko amakonda kuyendayenda, zomwe zikupereka chiwopsezo kuti atha kubweretsa mliri wa Covid-19 kuderalo.

Soko adati nthawi zina madalaivalawo amakhala oposa 40 koma satsatira ndondomeko zoyenera kuti asafalitse kapena kutenga matendawo.

“Tili pachiwopsezo chachikulu cha nthenda ya Covid-19 chifukwa anthuwa akuchokera m’dziko la Tanzania komwe nthendayi yafala kwambiri,” adatero Soko.

Iye adati mantha awo akuchuluka chifukwa madalaivalawo akafika m’dziko muno akumayendayenda ndi anthu a m’deralo.

Iye adati madalaivala ambiri ndi a chi Swahili ndiye akafika kuno Chichewa chimawavuto, zomwe zimawachititsa kuti atengane ndi Amalawi amene amalankhula Chichewa.

Mfumu ya deralo, Belewa, yomwe idadandaula za vutolo pamaliro mkati mwa sabatayi, idapempha boma kuti lidzionetsetsa kuti madalaivalawo akuyezedwa asadalowe m’dziko muno, komanso adzikhala ku mbindikiro wa sabata ziwiri.

Malo oyezera nthendayo m’chigawo cha kumpoto adatsekulidwa Loweruka pa April 11 ndipo pofika pomwe timalemba nkhaniyi anthu osapitilira khumi ndiwo adayezedwa.

Pa anthuwo, palibe adapezeka ndi nthendayo m’chigawocho.

Mneneri wa bungwe la National Oil Company of Malawi (Nocma), lomwe limabweretsa mafutawo, Telephorous Chigwenembe, adakana kulankhulapo pa zomwe akuchita madalaivalawo akafika m’dziko muno.

Dziko la Malawi nalo lili pa nkhondo yolimbana ndi matendawo. Pofika dzulo, anthu 33 ndi omwe adatsimikizika kuti akudwala matendawo, atatu adamwalira ndipo atatu ena adachira, kutanthauza kuti 27 ndi omwe akudwala matendawa. 

Maiko a Uganda ndi Kenya ndi ena mwa maiko omwe akudadandaula ndi madalaivala a galimoto zonyamula katundu. Mwachitsanzo, m’dziko la Uganda, madalaivala awiri ochokera ku Tanzania apezeka ndi nthendayo Lachitatu m’sabatayi.

Previous Post

Strange, bizzare pronouncements

Next Post

‘Adatuma nthenga kudzandifunsira’

Related Posts

Nkhani

Agwidwa ndi yunifomu za polisi

May 22, 2022
Nkhani

Dollar yasowa

May 21, 2022
Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
Next Post

‘Adatuma nthenga kudzandifunsira’

Opinions and Columns

Business Unpacked

Tame egos, take risks to grow economy

May 26, 2022
People’s Tribunal

What was that press briefing all about?

May 22, 2022
Big Man Wamkulu

Wife, in-law plotting my downfall

May 22, 2022
My Thought

Tonse Alliance died on arrival

May 22, 2022

Trending Stories

  • His case heard in UK court: Sattar

    Acb explains Sattar miss

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Kwacha gets 25% weaker

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • AmaZulu complete signing Gaba

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Gone but still in our midst

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Conforzi to invest K8.2bn in PPP venture

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.