Saturday, July 2, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

Samalani ndi chitopa

by ESMIE KOMWA
07/09/2019
in Chichewa
4 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Kuchokera ku phindu la ulimi wothirira, Catherine Bamusi wa m’boma la Blantyre adaganiza zogulako nkhuku zachikuda kuti zizimupatsa manyowa, ndiwo ngakhalenso ndalama akazingwa.

Iye adayamba ndi nkhuku 6 chaka chathachi ndipo pamene amalowa m’chaka chino zidali zitachulukana kufika 50.

“Ndili mkati modyerera, nkhuku zanga zidagwidwa ndi chitopa ndipo padakalipano ndilibe ndi imodzi yomwe chifukwa zonse zidafa,” adandaula motero Bamusi.

Pezani phindu lochuluka ku nkhuku zachikuda pozipatsa katemera

Marcus Twayah wa m’boma la Mulanje akuti chitopa chimamusautsa chaka chilichonse koma khama pa ulimiwu ndi lomwe limamuchititsa kuti zikafa, agule nkhuku zina ndi kuyambiranso kuweta.

“Padakakhala kuti palibe chitopa, bwenzi ndikutakata kwambiri chifukwa ulimiwu ndi waphindu.

“Ndimakwanitsa kuyambiranso chifukwa siulira zambiri ngati momwe umakhalira ulimi wa nkhuku za mazira ndi zanyama,” adabwekera motero mlimiyu.

Malingana ndi mphunzitsi wa zaulimi wa ziweto ku Lilongwe University of Agriculture and Natural Resources (Luanar) Jonathan Tanganyika, matenda a chitopa ndi oopsa kwambiri.

Iye adati awa ndi matenda omwe amapha nkhuku zambiri zachikuda m’dziko muno.

“Matenda ena akagwira nkhuku amapha koma sangafanane ndi momwe chitopa chomwe ena amachitchula kuti  chideru chimasakazira.

“Matendawa amagwira nkhuku panthawi ndi kupha zambiri ndipo pamadutsa miyezi ingapo asadabwerenso,” iye adafotokoza motero.

Malingana ndi mphunzitsiyo, matendawa amayamba ndi mavayilasi choncho chifukwa choti tizilombo tamtunduwu timavuta kupha, palibe mankhwala omwe amachiza chitopa chikagwa m’khola.

Iye adachenjeza alimi kuti asamanamizidwe kuti pali mankhwala a chitopa kapena zitsamba zochiza matendawa.

“Alimi ayenera kuteteza nkhuku zawo ku matendawa pozipatsa katemera wa matendawa monga I-2 yemwe akupezeka m’sitolo za vetenale za m’dziko muno.

“Katemerayu ndi wotsika mtengo ndipo alimi akuyenera kumapatsira nkhuku zawo m’miyezi inayi iliyonse kuti zizitetezeka,” adatero Tanganyika.

Mphunzisiyu adati m’botolo la katemerayu mumakhala madontho 200 omwe mlimi amayenera kupatsira ku nkhuku 200.

Iye adati mlimi amayenera kudonthetsera m’diso limodzi la nkhuku iliyonse.

Kadaulo wa ulimi wa ziweto m’boma la Blantyre Edwin Nyondo adati katemera wina wotetezera ku chitopa ndi lasota.

“Alimi amayenera kumwetsa nkhuku katemerayu miyezi itatu iliyonse komanso anapiye asanakwane sabata ziwiri,” adafotokoza motero.

Tanganyika adati katemera ndi njira yokhayo yotetezera nkhuku zachikuda ku matendawa m’dziko muno chifukwa n’zosatheka kuziweta m’njira yoti zisamasakanikirane ndi nkhuku zina ngati momwe amachitira m’maiko ena.

Mphunzisiyu adati izi zili chomwechi chifukwa nkhuku zachikuda m’dziko muno zimayendayenda kusakasaka zakudya.

Kuonjezera apo, iye adati nyengo ino ndiyamaukwati komanso zinamwali choncho n’kosavuta kufalitsa matendawa.

“Ichi n’chifukwa china chomwe chimachititsa kuti m’nyengo yotentha matendawa afalikire kwambiri.

“Chinthu china chomwe chimachititsa izi n’choti m’nyengo yotentha nkhuku zimayenda mtunda wautali kusakasaka zakudya chifukwa chimachepa ndipo potero zimakatengako matendawa,” iye adatero.

Mphunzitsiyo adaonjeza kuti katemera wa chitopa sioopsa ndipo sasintha kaonekedwe ndi kakomedwe ka nyama ya nkhuku koma amangoiteteza basi.

Tanganyika adafotokoza kuti katemerayu sagwira ntchito ku nkhuku zomwe zagwidwa kale ndi matendawa choncho alimi akuyenera kutsatira ndondomeko.

“Katemerayu amagwira ntchito kwa miyezi inayi ndipo ichi n’chifukwa chake mlimi ayenera kupatsira m’miyezi inayi iliyonse,” iye adatero.

Tanganyika adaonjeza kuti zizindikiro za matendawa zimaonekera mbali ya thupi yomwe agwira.

Mwachitsanzo, iye adati akagwira mu ubongo khuku imapinda khosi, imazungulira malo amodzi kapena kumangogwa.

“Akagwira mapapo nkhuku imatsokomola, kuyetsemula ndi kutulutsa mamina. Akagwira m’matumbo nkhuku imatsegula m’mimba,” adafotokoza motero.

Previous Post

‘Tobacco market has progressed well’

Next Post

Tetezani ana ku BP

Related Posts

Chilima: Change the mindset toward development
Nkhani

A Chilima abwera poyera

July 1, 2022
Nkhani

Achilima awachepetsera mphamvu zaulamuliro

June 24, 2022
Katundu wa a Mtambo adali kuseri kwa ofesi za khonsolo
Nkhani

Agona ku maofesi a khonsolo ya Mzuzu

June 4, 2022
Next Post

Tetezani ana ku BP

Opinions and Columns

My Diary

God-fearing nation, my foot!

July 2, 2022
Off the Shelf

APM digging a hole for DPP

July 2, 2022
Guest Spot

‘Fighting corruption is not the easiest task of any govt’

July 2, 2022
My Turn

Following spouse is no crime

July 1, 2022

Malawi-Music.com Top10

Trending Stories

  • Alliance partners talk

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • New VP houses draw criticism

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  •  Malawi credit Status at risk

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Britain squeezes Zuneth Sattar

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chilima opens pandora’s box

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.