Tuesday, January 19, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Sensasi ili mkati

by Steven Pembamoyo
14/09/2018
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Pamene kalembera wa anthu ndi nyumba ali mkati, mafumu ena ati akuyembekezera kuti mavuto amene amakumana nawo achepa chifukwa boma limagwiritsa ntchito zotsatira za kalemberayo popereka zofunika kwa Amalawi.

Kalemberayo, amene amachitika pakatha zaka 10 zilizonse, adayamba pa 3 mwezi uno ndipo akuyembekezeka kudzatha pa 23.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Kaleembera | The Nation Online
Wogwira ntchito ya kalembera kulembera banja lina ku Lilongwe

Polankhula ndi Tamvani, T/A Mlauli ya ku Mwanza, T/A Chindi ku Mzimba komanso T/A Mkanda ku Mchinji adanena payekhapayekha kuti ali ndi chiyembekezo kuti mavuto amene adza kaamba ka kukula kwa chiwerengero achepa.

“Vuto lalikulu limene tili nalo ndi la madzi. Ngakhale anthu akumanga nyumba zofolera ndi malate, madzi tikumwabe m’zitsime zosasaamalika. Izi zimadzetsa matenda amene timakavutikanso nawo kuchipatala,” adatero Mkanda.

T/A Chindi adati ngakhale kuli mavuto ena monga kusowa vuto la zaumoyo, nkhani yamadzi siyimugoneka tulo.

“Amayi amadzuka mbandakucha kukatunga madzi dzuwa litakwera. Kungochedwa pang’ono ndiye kuti pakhomo pawo. Mukhonza kuona ngati madzi akukanganiranawo ndi a pampope, koma ayi ndi a pachitsime,” adatero Chindi.

T/A Mlauli wa ku Neno idati vuto la madzi likusautsa, makamaka m’chilimwe pomwe dzuwa likuomba kwambiri. Iye adati izi zikukhudzaa kwambiri dera lake limene ndi lotentha kwambiri.

“Akukonza zina ndi zina, koma pa nkhani ya madzi, tisanamizanepo zinthu zikuyipirayipira. Mijigo ili apo ndi apo koma chiwerengero cha anthu ofuna madzi abwino chikungokwererabe,” adatero Mlauli.

Kalemberayu akuyamba kumene, padali mavuto osiyanasiyana, kuphatikizapo la kuchedwa kwa malipiro a ogwira ntchitoyi 25 000 pomwe adangolandira K20 000 mmalo mwa K120 000 imene amayenera kulandira ataphunzira ntchitoyi. Ogwira ntchito enanso adandaula kuti sanapeze nawo lamya zogwirira ntchitoyo. Vuto lina lidali la kubedwa kwa zipangizo za ogwira ntchitoyi ku Ntcheu.

Mneneri wa nthambi yoona za kalemberayu ya National Statistical Office (NSO) Kingsley Manda adatsimikiza za mavutowa koma adati zonse zili tayale tsopano.

“Chilichose chilibwino, onse adalandira ndalama zawo, tawatsimikizira kuti mayunitsi afika sabata ino koma awo amafuna lamyawo, tawafotokozera kuti lamya nzawokhawo omwe akuyenda m’midzi kutenga mafigala,” adatero Manda.

Iye adati vuto lalikulu lomwe lidalipo lidali lokhudza netiweki yotumizira ma figala makamaka mmadera momwe mulibe netiweki koma vutolonso adalikonza.

“Padali vuto la netiweki m’madera ena ndiye poti makina omwe tikugwiritsa ntchito ngolira netiweki kuti tilumikizane, tidapereka galimoto zomwe akumagwiritsa ntchito kuyenda kukafika pomwe pali netiweki n’kutumiza,” adatero Manda.

Mmodzi mwa owelengera anthuwa ku Mpsupsu m’boma la Zomba amene sanadzitchule dzina adati pa tsiku akumawerenga makomo osachepera 40.

Iye adati ngakhale nyumba za derali zili patalipatali koma akumakwanitsa kuwerenga anthu ochuluka chotere chifukwa kufunsa mafunso pogwiritsa ntchito tablet sizikumatenga nthawi kuti atsirize.

M’modzi wa anthu amene awerengedwa kwa Jali m’boma la Zomba Lones Kamwana adati mphindi zosaposera 45 zimene adafunsidwa mafunso akuti mphindizi zidali zopindulitsa kwa iye mwini ngakhalenso ku dziko.

“Mafunso ake akumufukula munthu kuchokera pa phata zinthu zimene a Malawi tikayankha mwachilungamo zithandizira kuti dziko lathu lino likhale lotukuka,” adatero Kamwana.

Kalembera wa m’chaka cha 2008 chiwerengero cha anthu chidapezeka kuti ndi 13 077 160. Lipoti la kalemberayu limasonyeza kuti anthu 48 mwa anthu 100 aliwonse amamwa madzi a pamjigo, anthu 18 pa 100 aliwonse amamwa m’zitsime zosatetezedwa.

Lipotili likusonyezaso kuti anthu 43 pa 100 amakhala mnyumba zawedewede, anthu 34 pa 100 amakhala mnyumba zowonekako bwino ndipo 23 pa 100 aliwose amakhala m’nyumba zolongosoka.

Malinga ndi NSO, chiwerengero cha Amalawi chikhonza kufika pa 17 931 637 chaka chino.

Previous Post

MCCCI for more investment in agro sector research

Next Post

Patricia Mkanda – Lilongwe North Constituency

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Constructions such as the one above have taken place in  Mkanda’s constituency

Patricia Mkanda - Lilongwe North Constituency

Trending Stories

  • Not yet given retirement benefits: Mutharika

    Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Wasteful Chakwera

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Covid-19 initiative raises K18.3m in 2 days

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Laz Chakwera’s Covid-19 strategy

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Fake injury claims soar

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

My Thought

Don’t relax, Covid-19 still here

January 17, 2021
Political Uncensored

Maddening chaotic virus

January 17, 2021
Emily Mkamanga

Chakwera has to instill unity

January 17, 2021
People’s Tribunal

Perilous times and the need for accountability

January 17, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.