Tuesday, April 20, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Siteshoni ya Nkaya ifewetsa maulendo

by Bobby Kabango
17/09/2016
in Nkhani
1 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Gawo lachiwiri lomanga siteshoni ya sitima ya Nkaya m’boma la Balaka layamba ndipo ntchitoyi ikuyembekezeka kutha mu November chaka chino.

Mneneri wa bungwe loona sitima zapamtunda la Central East African Railways (CEAR) Chisomo Mwamadi wati gawoli likatha, anthu amene amagwiritsira ntchito sitima zapamtunda athandizika chifukwa sitima zizinyamula katundu wambiri komanso ziziyenda mwachangu.

RelatedHeadlines

Anthu 49 afa ndi mphenzi

Luso la Joe Kellz mpatali

Tambala walira

Mwamadi: Samalani njanji
Mwamadi: Samalani njanji

Mu June chaka chino, bungweli lidamaliza gawo loyamba lomwe kudali kumanga njanji zinayi kuti sitima zapamtunda zizidutsana pamalopa.

Gawo lachiwiri lidayamba litangotha gawo loyamba lomwe kukhale kumanga njanji ina yotalika ndi makilomita awiri komanso kumanga njanji zinayi zomwe zizithandiza kusungirako sitima komanso kumasula mabogi.

“Njanji zimenezi ndizomwe tizimasulira sitima ngati ili ndi vuto komanso kusungirako sitima. Pamene tikupanga izi, sitima zina zizitha kumayenda mopanda kusokonezedwa. Izi sizimachitika poyamba chifukwa tidalibe malo, koma tsopano izi ziyamba kuchitika popanda vuto lililonse,” adatero Mwamadi.

Padakali pano, malo amene amangepo njanjizi asalazidwa kale komanso katundu wafika kuti ntchitoyi iyambe tsiku lililonse.

Njanji yopita ku Nkaya ndi imeneyi
Njanji yopita ku Nkaya ndi imeneyi

Mwamadi akuti gawoli likatha, anthu amene amagwiritsira ntchito sitima asangalala kwambiri komanso bizinesi izichitika mwachangu.

“Zonse zikatha, ndiye kuti Nkaya akhala malo akulu pomwe sitima zizisemphana komanso kumamangirira mabogi. Sitima yochokera ku Mwanza, Blantyre, Liwonde komanso Kanengo zizidutsana pa Nkaya komanso titha kumamanga mabogi.

“Izi sizimachitika poyamba. Kudutsana kwa sitima kudali kovuta, komanso sitimatha kumangirira mabogi. Poyamba ntchitoyi imachitikira ku Liwonde koma malo adali ochepa. Pofika November chilichonse chikhala chikuchitika, sitima ziziyenda mwachangu, zizinyamula mabogi ambiri, kuchoka pa 20 kufika pa 45. Anthu ogwiritsira sitima ayembekezere chimwemwe,” adatero Mwamadi. n

Avatar
Bobby Kabango
Previous Post

Police brutality: Are police officers above the law?

Next Post

Msonda: Tsamba loyoyoka mu PP?

Related Posts

lightning e1446717884574 | The Nation Online
Nkhani

Anthu 49 afa ndi mphenzi

April 3, 2021
Joe Kellz | The Nation Online
Nkhani

Luso la Joe Kellz mpatali

April 3, 2021
Anthu adaponya voti m’madera ena Lachiwiri
Nkhani

Tambala walira

April 2, 2021
Next Post
Was dragged to court in January 2016: Msonda

Msonda: Tsamba loyoyoka mu PP?

Opinions and Columns

Big Man Wamkulu

Hot babe wants to trap me, should I ran?

April 18, 2021
Political Uncensored

Mighty mess!

April 18, 2021
My Thought

Chakwera’s indecisiveness will be his downfall

April 18, 2021
People’s Tribunal

Cut the crap, act on abuse forthwith

April 17, 2021
https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf https://www.mwnation.com/wp-content/uploads/2021/03/WFP-Afikepo-1-2.pdf

Trending Stories

  • Chakwera: We will use the relevant laws to ensure
you pay back what you stole

    Chakwera bites

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Ministry defends ‘borrowing’ of Covid-19 funds

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Chilima in public projects inspection

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • OPC frustrates roads projects

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malewezi’s career, political profile

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.