Friday, January 22, 2021
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa Nkhani

Sitilemba akunja—Ansah

by Steven Pembamoyo
07/09/2018
in Nkhani
3 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Pamene kalembera wachisankho walowa gawo lachisanu, mkulu wa bungwe la zisankho la Malawi Electoral Commission (MEC) Jane Ansah wati Amalawi asade nkhawa, chifukwa anthu a kunja salembetsa nawo m’kaundula.

Ansah adanena izi potsatira ndemanga za ena kuti pali chiopsezo choti nzika zina za dziko la Mozambique zikhonza kulembetsa m’kaundula m’boma la Mulanje. Malinga ndi anthu ena, pali chiopsezo kuti anthu ena a ku Mozambique akhonza kufuna kulembetsa nawo, makamaka ku Limbuli ndi Muloza, komwe ndi dera la m’malire ndi Mozambique.

RelatedHeadlines

Zisangalalo zafika, samalani

Mademo ayambika

Makhansala aderera alawansi

Voter registration | The Nation Online

Koma Ansah adanenetsa: “Taika ndondomeko zonse kuti pasakhale wakunja woti walembetsa. Izi tikuchita poonetsetsa kuti pali mamonitala a kuderalo amenenso adzaonetsetse kuti ofuna kulembetsa ali ndi chitupa cha unzika.”

Mkulu wa nthambi yoona za kalembera wa unzika m’boma la Mulanje, Wellingtone Kalambo wati akumanapo ndi nzika za ku Mozambique zofuna kulembetsa nawo mavoti.

“Taonapo mafumu a ku Muloza akupereka umboni kuti munthu ndi m’Malawi, koma kuwafunsitsa, tidapeza kuti ndi a ku Mozambique,” adatero Kalambo.

Kalembera wa chisankho adalowa m’gawo lachisanu Lolemba ndipo likuyembekezeka kudzatha pa … Malinga ndi MEC, anthu 3 271 744 adalembetsa m’magawo apitawa, pomwe MEC imayembekezera kulembetsa anthu 4 619 174. Izi zikusonyeza kuti anthu 81 mwa 100 alionse amene amayenera kulembetsa ndiwo adatero.

Kutsika kwa anthu amene akulembetsa kwakhudza akadaulo, a mabungwe ndi zipani zandale zina.

Katswiri wa zandale wa ku Chancellor College Ernest Thindwa wati

mchitidwe wamphwayi kukalembetsa ukhonza kukhala kukhumudwa kwa Amalawi

ndi mchitidwe wa andale omwe amasintha mawanga akasankhidwa m’maudindo.

“Mwina anthu adagwa mphwayi ndi nkhani za zisankho

chifukwa amakhumudwa ndi mchitidwe wa atsogoleri omwe amalonjeza

zinthu zina nthawi ya kampeni koma osazikwaniritsa akasankhidwa,” adatero

Thindwa.

Koma zipani zandale, zaalunjika ponena kuti bungwe la MEC silinafalitse bwino uthenga wa kalembera chifukwa likulimbikira pofalitsa mauthenga pa wailesi ndi nyuzipepala basi, mmalo mopitanso kumaderawo.

Mneneri wa chipani cha United Democratic Front (UDF) Ken Ndanga, wati kafukufuku wawo adaonetsa kuti bungwe la MEC silidafalitse uthenga mokwanira m’madera.

“Tikawafunsa bwanji sanalembetse, anthu m’madera amati samadziwa zoti kalembera wafika m’dera lawo. Ngati chipani, tikumapita m’maderamu kumema anthu,” adatero Ndanga.

Mlembi wamkulu wag ulu la United Transformation Movement (UTM) Patricia Kaliati komanso mlembi wamkulu wa Malawi Congress Party (MCP) Eissenhower Mkaka adagwirizana ndi Ndanga podzudzula MEC.

“Ndikunena pano ndili ku Mulanje kumene kalembera ali mkati koma sindinaone galimoto ya MEc ngakhale chimkuzamawu kumema anthu kukalembetsa.

Mkaka adati chipani chawo, chomwe chakhala chikupempha MEC kuti ibwereze kalembera m’madera ena, chimayembekezera kuti pofika gawo lachinayi la kalembera, zinthu zikhala zitasintha koma mmalo mwake zikunkira kuonongeka.

“M’gawo loyamba ndi lachiwiri, zidali zomveka kuti uthenga udali usadamwazidwe mokwanira koma m’gawo lachinayi tizikamba nkhani imeneyi? Ayi sizoona MEC ikadawonapo bwino,” adatero Mkaka.

Mkulu wa mgwirizano wa mabungwe okhudzidwa ndi zisankho la Malawi Electoral Support Network (Mesn) Steve Duwa adagwirizana ndi zipanizi kuti MEC yalephera kumwaza mauthenga a kalembera.

“Ndidali ku Thyolo ndi Luchenza komwe anthu samaonetsa chidwi ndipo n’tafunsa, makhansala ngakhaleso anthu amati sadalandire uthenga uliwonse woti kukuchitika kalembera m’dera lawo kutanthauza kuti ntchito ikadalipo,” adatero Duwa.

Koma malinga ndi Ansah, palibe kuwiringula kulikonse koti mauthenga sadamwazidwe chifukwa MEC ndi mabungwe ena monga National Initiative for Civic Education (Nice) Trust ayesetsa kumwaza mauthenga.

“Kupatula njira yomwaza mauthenga pa wailesi, timagwiritsanso ntchito galimoto zokhala ndi zimkuzamawu. M’gawo loyamba, tidagwiritsa ntchito galimoto 15, gawo lachiwiri galimoto 14, gawo lachitatu galimoto 18 ndipo gawo lachinayi galimoto 17,” adatero Ansah.

Iye adati bungweli lidzaunika pamapeto pa zonse ngati n’koyenera kubwereza ntchito ya kalembera m’maboma omwe sizidayende bwino.

Kalembera wa zisankho wachitika kale m’maboma a Kasungu, Salima, Dowa, Ntchisi, Dedza, Nkhotakota, Lilongwe, Chikwawa, Ntcheu, Blantyre ndi Mwanza.—zoonjezera: madalitso kateta, mtolankhani wa mec

Previous Post

Join savings and investment clusters—Comsip

Next Post

Silver fight eye second position

Related Posts

Malango: We are addressing challenges
Nkhani

Zisangalalo zafika, samalani

December 11, 2020
Pazionetsero za HRDC, chimbaula cha polisi chidaotchedwa
Nkhani

Mademo ayambika

December 11, 2020
Councillors in Mzuzu Nov 2020 | The Nation Online
Nkhani

Makhansala aderera alawansi

December 5, 2020
Next Post
Wanderers (in yellow) and Silver in a match their fans caused trouble

Silver fight eye second position

Trending Stories

  • Escaped South African bail: Bushiris

    Bushiri says not seeking political intervention

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi closes in on hefty US deal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Vendors back on streets amid Covid-19 surge

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Tonse faulted on former presidents’ benefits

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Malawi loses 5% of GDP on donor withdrawal

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Opinions and Columns

These Freedoms

Where is God in the Malawi Vision 2063?

January 22, 2021
Business Unpacked

Towards Malawi2063, lessons from Vision 2020

January 20, 2021
Rise and Shine

Never give up on resolutions

January 20, 2021
In pursuit of development

India’s vaccine drive

January 20, 2021
  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2021 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Opinion
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.