Friday, May 20, 2022
  • About Us
  • ImagiNATION
  • Adverts
  • Rate Card
  • Contact Us
The Nation Online
Advertisement
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation
No Result
View All Result
No Result
View All Result
Home Chichewa

‘Sosolani mphamvu bwana’ 

by Nation Online
23/04/2022
in Chichewa
2 min read
0
Share on FacebookShare on TwitterShare on WhatsAppShare on LinkedinLinkedinShare via Email

Akadaulo a zandale ati mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera akuchedwa kuthothola mphamvu zina monga momwe adalonjezera.

Bungwe la akadaulowo pa ndale la Political Science Association (PSA) lati papita nthawi kuchokera pomwe apulezidenti adalonjeza kuti adzathothola mphamvu zina koma kuli ziii mpaka lero.

Mlembi wamkulu wa bungwelo a Makhumbo Munthali ati m’malamulo a dziko lino zilimo zoti mtsogoleri akhoza kuthothola mphamvu kuti zina m’dziko ziyende bwino.

A Chakwera kuonekera ku Nyumba ya Malamulo

Mmbuyomo mneneri wa apulezidenti a Anthony Kasunda adayankha funsoli ponena kuti apulezidenti akukwaniritsa lonjezo lawo chifukwa mwa zina amakaonekera ku Nyumba ya Malamulo monga malamulo amanenera.

Koma a Munthali ati: “Si zomveka kunena kuti poti apulezidenti amakaonekera kunyumbayo kapena ku bungwe lolimbana ndi katangale la ACB ndiye kuti athothola mphamvu ayi. Izizi zilimo kale m’malamulo kuti amayenera kutero.”

A Munthali adati n’kofunikanso kumvetsetsa mtundu wa mphamvu zomwe apulezidenti akuyenera kuthothola chifukwa pali mphamvu za ofesi komanso pali mphamvu zongovala.

“Mphamvu zomwe anthu akufuna apulezidenti atathotholako ndi za ofesi chifukwa n’zomwe zimagwira ntchito ngati lamulo,” adatero a Munthali.

Lolemba lapitali a Kasunda adati apulezidenti adathothola mphamvu zina chifukwa salowerera ntchito za ACB, apolisi komanso ofesi yomva madandaulo a anthu ya Ombudsman.

Iwo adati n’zosafuna kuuzidwa kuti apulezidenti amakaonekera n’kukayankha mafunso ku Nyumba ya Malamulo monga momwe malamulo amanenera.

Ndime 89 (4) ya malamulo a dziko lino amati Pulezidenti akuyenera kupita ku Nyumba ya Malamulo kukayankha mafunso ngati nyumbayo yoona kuti n’kufunika kutero pogwiritsa ntchito malamulo ake.

Pa 6 September 2020 a Chakwera polankhula ku mtundu wa Amalawi adati mtsogoleri akakhala ndi mphamvu zambiri zinthu zina zimaonongeka m’dziko.

Kadaulo winanso pandale a Humphrey Mvula wati uthenga wa a Chakwera wa pa 6 September 2020 udali wongofuna kumvetsa kunzuna Amalawi omwe adawavotera pachisankho.

Pomasulira mawu awo, a Mvula adati sichamasewera kuthothola mphamvu za utsogoleri chifukwa n’zofunika kuzukuta malamulo mofatsa zomwe zimatenga nthawi kuti zitheke.

Previous Post

Albinos’ plight: Mere campaign tool

Next Post

More action needed in tackling climate change

Related Posts

Foni kundende monga ya Zomba n’zoletsedwa
Nkhani

Apezeka ndi foni m’mimba

May 15, 2022
A Kamuzu adali katakwe pandale
Nkhani

‘Kamuzu adali chitsime chakuya’

May 14, 2022
Kodi chilango chonyonga chikhalepo, kapena ayi?
Nkhani

Amalawi akupereka maganizo pa zonyonga

May 14, 2022
Next Post

More action needed in tackling climate change

Discussion about this post

Opinions and Columns

Business Unpacked

Fixing economy needs action, not rhetoric

May 19, 2022
Candid Talk

Know your place in his/her life

May 15, 2022
People’s Tribunal

Why can’t we start with implementing the reforms?

May 15, 2022
Big Man Wamkulu

My wife is a WhatsApp addict

May 15, 2022

Trending Stories

  • CAF accepts FAM’s request on Flames fixture shift

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Onesimus leaves Major One Records

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • MCTU pushes for 75% minimum wage hikeof

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • Road traffic spot fines on way out

    0 shares
    Share 0 Tweet 0
  • UN bets K66bn on LMC’s plan

    0 shares
    Share 0 Tweet 0

Malawi-Music.com Top10

  • Values
  • Our Philosophy
  • Editorial policy
  • Advertising Policy
  • Code of Conduct
  • Plagiarism disclaimer
  • Disclaimer
  • Privacy Policy
  • Terms of use

© 2022 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

No Result
View All Result
  • Home
  • News
  • Politics
  • Business
  • Entertainment
  • Life & Style
    • Every Woman
      • Soul
      • Family
    • Religion
    • Feature
  • Society
  • Columns
  • Sports
  • Chichewa
  • Enation

© 2020 Nation Publications Limited. All Rights Reserved.

This website uses cookies. By continuing to use this website you are giving consent to cookies being used. Visit our Privacy and Cookie Policy.